< John 9 >

1 As Jesus walked along [with us], he saw a man who had been blind from the time he was born.
Iye akuyendabe, anaona munthu wosaona chibadwire.
2 We disciples asked him, “Teacher, was this man blind from when he was born because his parents sinned or because he himself sinned?”
Ophunzira ake anamufunsa Iye kuti, “Rabi anachimwa ndani, munthuyu kapena makolo ake, kuti iye abadwe wosaona?”
3 Jesus replied, “His being blind was not because he or his parents sinned. Instead, [he has been blind] in order that [people can] see the power of God {the power of God can be seen} as a result of [what will now happen] to him.
Yesu anayankha kuti, “Sikuti iyeyu anachimwa kapena makolo ake, koma izi zinachitika kuti Mulungu aonetse ntchito zake mwa iyeyu.
4 While there is still time, I must do the work that the one who sent me [wants me to do. Just like daytime is followed by] nighttime when people do not work, [at the end of our lives] [MET] [it is too late for us to do what God wants].
Ife tiyenera kugwira ntchito za Iye amene anandituma kukanali masana. Usiku ukubwera, pamene wina aliyense sadzagwira ntchito.
5 While I am still [living] in this world, I am the [one who enables people to know about God, like] [MET] [a] light enables the people in [MTY] this world [to see what is in the darkness].”
Pamene Ine ndili mʼdziko lapansi, Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi.”
6 After he said that, he spat on the ground. He made [a little bit of] mud with the saliva, and put it on the man’s eyes.
Atanena izi, Iye anathira malovu pansi ndi kukanda dothi, napaka matopewo mʼmaso a munthuyo.
7 Then he said to him, “Go and wash in Siloam pool!” (That name means ‘sent;’ [just like they sent the water by a channel into the pool, God sent Jesus]). So the man went and washed [in the pool], and when he went home he was able to see!
Yesu anamuwuza iye kuti, “Pita kasambe mʼdziwe la Siloamu” (mawu awa akutanthauza Wotumidwa). Choncho munthuyo anapita ndi kukasamba ndipo anabwerako akupenya.
8 His neighbors and others who previously had seen him when he was begging said, “He is the man who used to sit here and beg, isn’t he?”
Anzake ndi iwo amene anamuona iye poyamba akupempha anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene amapemphapempha uja?”
9 Some said, “[Yes], he is.” Others said, “No, [he is not]. It is [just] a man who looks like him!” But the man himself said, “Yes, I am that man!”
Ena ananena kuti anali yemweyo. Ena anati, “Ayi, sakuoneka ngati yemweyo.” Koma iye mwini ananenetsa kuti, “Munthuyo ndine.”
10 So they said to him, “How is it that now you can see?”
Iwo anafunsitsa kuti, “Kodi nanga maso ako anatsekuka bwanji?”
11 He replied, “The man whose name is Jesus made some mud and put it on my eyes. Then he told me to go to Siloam [pool] and wash. So I went there and washed, and then I could see.”
Iye anayankha kuti, “Munthu wina wotchedwa Yesu anakanda dothi ndi kupaka mʼmaso anga. Iye anandiwuza kuti ndipite ku Siloamu ndi kukasamba. Choncho ndinapita kukasamba, ndipo ndikuona.”
12 They said to him, “Where is that man [now]?” He said, “I do not know.”
Iwo anamufunsa iye kuti, “Ali kuti munthu ameneyu?” Iye anati, “Ine sindikudziwa.”
13 They took to the Pharisees the man who was previously blind.
Iwo anabwera naye munthu amene poyamba anali wosaona kwa Afarisi.
14 The day on which Jesus made the mud and enabled the man to see again was a (Sabbath/Jewish day of rest). [The Pharisees considered that healing someone was work, and their rules did not permit people to do any work] ([on the Sabbath/on the Jewish rest day]).
Tsono linali la Sabata tsiku limene Yesu anakanda dothi ndi kutsekula maso a munthuyu.
15 So the Pharisees also asked that man, “How did you become able to see?” He said to them, “The man put mud on my eyes. Then I washed, and now I can see!”
Choncho Afarisi anamufunsanso iye momwe analandirira kuona kwake. Munthuyo anayankha kuti, “Iye anapaka matope mʼmaso anga, ndipo ine ndinakasamba, ndipo ndikuona.”
16 So some of the Pharisees said, “Since this man [Jesus] disobeys [our rules about working] (on the Sabbath/on the Jewish rest day), he is not from God.” But others said, “If he was a sinner, (he could certainly not do such miracles!/how could he do such miracles?) [RHQ]” So they were divided.
Ena a Afarisi anati, “Munthu uyu siwochokera kwa Mulungu, pakuti sasunga Sabata.” Koma enanso anafunsa kuti, “Kodi munthu wochimwa angachite bwanji zizindikiro zodabwitsa ngati izi?” Choncho iwo anagawanika.
17 So one of them said to the blind man again, “You are the man whom he enabled to see. What do you yourself say about him?” The man said, “[I think] he is a prophet!” [So they told him to go].
Pomaliza iwo anatembenukiranso kwa munthu amene anali wosaona uja nati, “Kodi iwe unena chiyani za Iye poti ndi maso ako amene watsekula?” Munthuyo anayankha kuti, “Iye ndi mneneri.”
18 The Jewish [leaders] [SYN] still did not believe that the man was blind when he was born, and that he was [now] able to see. So they sent someone to bring the man’s parents.
Ayuda sanakhulupirirebe kuti iye anali wosaona ndi kuti anayamba kuona kufikira atayitana makolo ake.
19 [When they got there], one of [the Jewish leaders] asked them, “Is that man your son? Do you say that he was blind when he was born? [If that is true], how is he now able to see?”
Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu ndi mwana wanu? Kodi iyeyu ndi amene mukunena kuti anabadwa wosaona? Nanga zikutheka bwanji kuti akuona?”
20 His parents replied, “We know that he is our son. We know that he was blind when he was born.
Makolo anayankha kuti, “Ife tikudziwa kuti ndi mwana wathu, ndipo tikudziwa kuti anabadwa wosaona.
21 But we do not know how he is able to see now. We also do not know who enabled him to see. Ask our son! He is old enough [to answer questions from authorities like you] He can tell you himself!”
Koma sitidziwa zimene zachitika kuti tsopano azipenya. Amenenso wamupenyetsa sitikumudziwa. Mufunseni ndi wamkulu; iye adziyankhira yekha.”
22 The Jewish [leaders] [SYN] had previously declared that they would prevent anyone who declared that Jesus was the Messiah from [entering] their synagogues. His parents [knew that, so] they were afraid of the Jewish [leaders] [SYN].
Makolo ake ananena izi chifukwa amaopa Ayuda, popeza Ayuda anatsimikiza kale kuti aliyense amene adzamuvomereza Yesu kuti anali Khristu adzatulutsidwa mʼsunagoge.
23 That is the reason that they said, “He is old enough [to answer questions], so ask him!”
Ichi ndi chifukwa chake makolo ake anati, “Mufunseni iye ndi wamkulu.”
24 So they sent someone to bring back to them the man who had been blind. [When he got there], the [Jewish leaders] said to him, “Knowing that God [is listening] [IDM], tell the truth! We know that the man who healed you is a sinner.”
Iwo anamuyitanitsa kachiwiri munthu amene anali wosaonayo. Iwo anati, “Lemekeza Mulungu. Ife tikudziwa kuti munthu uyu ndi wochimwa.”
25 He replied, “I do not know if he is a sinner or not. But one thing I do know is that I was blind, but now I can see!”
Iye anayankha kuti, “Zakuti Iye ndi wochimwa kapena ayi, ine sindikudziwa. Ine ndikudziwa chinthu chimodzi. Ndinali wosaona koma tsopano ndikuona!”
26 So they said to him, “What did he do to you? How did he enable you to see?”
Kenaka anamufunsa kuti, “Kodi Iye anachita chiyani kwa iwe? Iye anatsekula motani maso ako?”
27 He replied, “I told you that already, but you did not [RHQ] pay attention! Why do you want to hear me tell you again? (Do you also want to become his disciples?/You talk as though [IRO] you also want to become his disciples [RHQ]).”
Iye anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kale ndipo inu simunamvetsetse. Chifukwa chiyani mukufuna mumvenso? Mukufuna kuti inu mukhale ophunzira akenso?”
28 Then they insulted him angrily. They said, “You are that man’s disciple, but we are Moses’ disciples!
Pamenepo anamunyoza ndipo anati, “Iwe ndiye ophunzira wa munthuyu! Ife ndife ophunzira a Mose!
29 We know that God spoke to Moses; but this man, we do not know where he is from or where he [gets any authority] from!”
Ife tikudziwa kuti Mulungu anayankhula kwa Mose, koma za munthu uyu, ife sitikudziwa ngakhale kumene akuchokera.”
30 The man replied, “That is very surprising! You [say that] you do not know where he [gets any authority]. But he enabled me to see!
Munthuyo anayankha kuti, “Tsopano izi ndi zodabwitsa! Inu simukudziwa kumene akuchokera, komabe iye watsekula maso anga.
31 We know that God does not help sinners [who ask God to help them]. Instead, he listens to [and helps] godly people who pray. He listens to people who do what God wants.
Ife tikudziwa kuti Mulungu samvera wochimwa. Iye amamvera munthu woopa Mulungu amene amachita chifuniro chake.
32 No one has ever enabled a man to see who was blind when he was born [like I was]. That has never happened since the world began! (aiōn g165)
Palibe amene anamvapo za kutsekula maso a munthu wobadwa wosaona. (aiōn g165)
33 So if this man had not come from God, he would not be able to do anything [like that]!”
Ngati munthu uyu akanakhala wosachokera kwa Mulungu, palibe chimene Iye akanachita.”
34 They replied to him, “You (were born [as a result of your parents’] sin [EUP]/bastard)! (Do you think you are qualified to teach us?/You are not qualified to teach us!) [RHQ]” Then they threw him out [of the synagogue].
Pamenepo anayankha kuti, “Iwe unabadwa mu uchimo kotheratu; bwanji ukuyesa kutiphunzitsa ife!” Ndipo anamutulutsa kunja.
35 Jesus heard [people say] that they had thrown that man out. He found the man and said to him, “Do you believe that the one who came down from heaven [is the Messiah]?”
Yesu anamva kuti anamutulutsa kunja ndipo pamene anamupeza anati, “Kodi ukukhulupirira Mwana wa Munthu?”
36 The man answered, “Sir, who is he? [Tell me], in order that I may believe in him.”
Munthuyo anafunsa kuti, “Kodi, Ambuye, ameneyo ndi ndani? Ndiwuzeni kuti ndimukhulupirire Iye?”
37 Jesus said to him, “You have seen him. [In fact, it is I], the one who am speaking to you.”
Yesu anati, “Iwe wamuona tsopano. Zoonadi ndiye amene akuyankhula nawe.”
38 The man said, “Lord, I believe that [you are the Messiah]!” Then he [knelt down before] Jesus and worshipped him.
Pamenepo munthuyo anati, “Ambuye, ndikukhulupirira,” ndipo anamulambira Iye.
39 Jesus said, “I have come into this world to judge [the people in the world]. The result will be that [those who realize that they do not know God’s truth will perceive it. That is like] [MET] [enabling] those who are blind to see. But the result will also be that people who [falsely think] [IRO] that [they understand God’s truth will never understand it. That is like] [MET] [people] who are blind remaining blind permanently.”
Yesu anati, “Ndinabwera pansi pano kudzaweruza kuti osaona aone ndi openya asaone.”
40 Some of the Pharisees who were with him heard him say that, and said to him, “You are not suggesting that we are [like] blind people, are you?”
Afarisi ena amene anali pafupi naye anamva akunena izi ndipo anafunsa kuti, “Chiyani? Kodi ndife osaonanso?”
41 Jesus said to them, “If you [realized that you did not yet know God’s truth, but you wanted to, then you would be like] blind people [who wanted to see. God would be able to] forgive your sins. But you are now [falsely] claiming that you [know God’s truth, so you are like people who are blind who claim that they] can see. [Because of that, God is not able to] forgive your sins.”
Yesu anati, “Mukanakhala osaona, simukanachimwa; koma tsopano popeza mukuti mumaona, ndinu ochimwabe.”

< John 9 >