< John 8 >

1 But Jesus went [with us disciples] to Olive [Tree] Hill [and we stayed near there that night].
Koma Yesu anapita ku phiri la Olivi.
2 Early the next morning, we returned to the Temple [courtyard]. Many people gathered around Jesus, so he sat down to teach them.
Mmamawa Iye anaonekeranso ku Nyumba ya Mulungu kumene anthu onse anamuzungulira ndipo Iye anakhala pansi nawaphunzitsa.
3 Then men who taught the [Jewish] laws and some of [SYN] the Pharisee [religious group] brought a woman to him. She was seized {[They] had [arranged to] seize her} while she was having sex with a man who was not her husband. They made her stand up in front of the group [that was listening to Jesus].
Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi anabweretsa mkazi amene anagwidwa akuchita chigololo. Iwo anamuyimiritsa patsogolo pa anthu ndipo
4 Then they said to Jesus, “Teacher, this woman was seized {[we] seized this woman} while she was having sex with a man who is not her husband.
anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, mkazi uyu tinamugwira akuchita chigololo.
5 Moses commanded us in the laws that [he gave us] that we should throw stones at such women [and kill them]. So what do you say [we should do]?”
Mʼmalamulo a Mose anatilamulira kuti akazi otere tiwagende ndi miyala. Tsopano Inu mukuti chiyani?”
6 They asked this question as a trap so that they could accuse him. [If he said that they should not kill her, they would shame him for disobeying the law of Moses. If he said that they should kill her, they could accuse him to the Roman governor]. But Jesus bent down and wrote something on the ground with his finger.
Iwo anagwiritsa ntchito funsoli ngati msampha, ndi cholinga choti apeze chifukwa cha kumuneneza Iye. Koma Yesu anawerama pansi ndi kuyamba kulemba pa dothi ndi chala chake.
7 While they continued to question him, he stood up and said to them, “Whichever one of you has never sinned can be the first one to start throwing stones at her.”
Pamene iwo anapitirira kumufunsa, Iye anaweramuka ndipo anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu alipo wopanda tchimo, ayambe iyeyo kumugenda ndi miyala mkaziyu.”
8 Then he stooped down and wrote [some more] on the ground.
Iye anaweramanso pansi ndi kulemba pa dothi.
9 After they heard what he said, those [who were questioning him] went away, one by one, the older ones first [and then the younger ones, knowing they were all sinners]. Finally only Jesus was there, along with the woman.
Iwo atamva izi anayamba kuchoka mmodzimmodzi, akuluakulu poyamba, mpaka Yesu anatsala yekha ndi mkaziyo atayimirira pomwepo.
10 Jesus stood up and asked her, “Woman, where are they? Has no one said you must die for your sin?”
Yesu anaweramuka ndipo anamufunsa iye kuti, “Akuluakulu aja ali kuti? Kodi palibe amene wakutsutsa?”
11 She said, “No, sir, no one.” Then Jesus said, “I do not condemn you either. Go [home] now, and do not continue your sinful [life] any longer!”]
Iye anati, “Ambuye, palibe ndi mmodzi yemwe.” “Inenso sindikukutsutsa iwe. Pita kuyambira tsopano usakachimwenso.”
12 Jesus spoke to the people again. He said, “I am [like] a light [MET] for [all the people in] [MTY] the world. [Just like a light reveals what has been in the darkness] [MET], [I reveal God’s truth to them]. Those who walk in the darkness [are unaware of what is around them]. But those who become my disciples will always be aware [of God’s truth] [MET]. They will have my light [which shows them how to have eternal] life.”
Yesu atayankhulanso kwa anthu, anati, “Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi. Aliyense amene anditsata Ine sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo.”
13 So the Pharisees said to him, “You are just telling about yourself! [Since there is no one else to verify these things that you say about yourself], [we] do not [need to accept that] what you say is true.”
Afarisi anamutsutsa Iye nati, “Iwe ukudzichitira umboni wa Iwe mwini, umboni wako siwoona.”
14 Jesus replied, “Even if I were the [only one to] say these things about myself, what I say is true, because I know that I came from [heaven], and I know that I am going [back to heaven]. But you do not know where I came from or where I am going.
Yesu anayankha kuti, “Ngakhale Ine ndidzichitire umboni, umboni wangawu ndi woona, pakuti Ine ndikudziwa kumene ndinachokera ndi kumene ndikupita. Koma inu simukudziwa ndi pangʼono pomwe kumene ndinachokera kapena kumene ndikupita.
15 You judge people according to human standards. [The reason] that I am [here is] not (to condemn people/to say that I will punish people) [for their sins].
Inu mumaweruza potsata maganizo a anthu chabe. Ine sindiweruza munthu wina aliyense.
16 But if I did judge [people], what I decided would be correct, because I am not the [only] one [who will decide those things]. I and the one who sent me will both decide.
Koma Ine ndikati ndiweruze, ndimaweruza molondola, chifukwa Ine sindili ndekha koma ndili ndi Atate amene anandituma.
17 It is written {[Moses] wrote} in your law that if [at least] two people testify that [some event has happened], [people should consider] that what they say is true.
Mʼmalamulo anu munalembedwa kuti umboni wa anthu awiri ndi wovomerezeka.
18 I am telling you about myself, and the other one who is telling you about me is [my] Father who sent me. [So you should believe that what we declare is true].”
Ine ndikudzichitira ndekha umboni; ndipo mboni inanso ndi Atate amene anandituma.”
19 Then they asked him, “[If you have a] father whom [we can question about you], where is he?” Jesus replied, “You do not know [who] I [really am]. If you knew who I [really am], you would know who my Father is also.”
Kenaka iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi Atate anuwo ali kuti?” Yesu anayankha kuti, “Inu simundidziwa Ine. Atate anganso simuwadziwa. Mukanandidziwa Ine, mukanawadziwanso Atate anga.”
20 He said these things when he was in the Temple [courtyard], near the place where the people put their offerings. [This was also very close to the place where the Jewish council met]. But no one seized him to arrest him, because it was not yet time [MTY] [for him to suffer and die].
Iye anayankhula mawu awa pamene amaphunzitsa Nyumba ya Mulungu pafupi ndi malo amene amaponyapo zopereka. Komabe palibe amene anamugwira Iye, chifukwa nthawi yake inali isanakwane.
21 Jesus also said to them, “I [will soon be] going away. Then [at the end of your life] you will seek me, but you will die [without God forgiving] your sins. Where I will go, you will not be able to come.”
Kenakanso Yesu anawawuza kuti, “Ine ndikupita, ndipo mudzandifunafuna, koma mudzafa muli mʼmachimo anu. Kumene ndikupita, inu simungabwereko.”
22 So the Jewish [leaders] said among themselves, “Is he going to kill himself? Is that the reason that he said, ‘Where I go, you will not be able to come’?”
Izi zinachititsa Ayuda kufunsa kuti, “Kodi adzadzipha yekha? Kodi ndicho chifukwa chake akuti, ‘Kumene ndikupita, inu simungabwereko?’”
23 But Jesus continued by saying to them, “You were born here in this world, but I came from heaven. You belong to those who are opposed to God [MTY]. I do not belong to them.
Koma Iye anapitiriza kuti, “Inu ndi ochokera pansi pano. Ine ndine wochokera kumwamba. Inu ndinu anthu a dziko la pansi. Ine sindine wa dziko lapansi lino.
24 I told you that you will die [without God forgiving] your sins. If you do not believe that I am [who I say that I am], you will die [without God forgiving] your sins.”
Ine ndinakuwuzani kuti mudzafera mʼmachimo anu ngati simukhulupirira kuti Ine Ndine. Ndithu inu mudzafera mʼmachimo anu.”
25 So they said to him, “You! Who do you think you are?” Jesus said to them, “Ever since I began [teaching], I have been telling you who I am!
Iwo anafunsa kuti, “Ndinu ndani?” Yesu anayankha kuti, “Monga Ine ndakhala ndikunena nthawi yonseyi,
26 I could judge you and say that [you are guilty of] many things. But instead, [I will say only] what the one who sent me tells me to say. [What he says] is true, and I tell the people in the world [MTY] what I have heard from him.”
ndili ndi zambiri zoti ndinene zoweruza inu. Koma Iye amene anandituma ndi woona, ndipo chimene Ine ndamva kuchokera kwa Iye, ndi chimene ndimaliwuza dziko lapansi.”
27 They did not understand that he was talking about his Father [in heaven].
Iwo sanazindikire kuti Iye amawawuza za Atate ake.
28 So Jesus said, “I am the one who came down from heaven, but when you lift me up [on a cross to kill me], you will know who I am. You will also know that I do not do anything with my own [authority]. Instead, I say just what [my] Father has taught me.
Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa.
29 He is the one who sent me, and he helps me. Because I always do the things that please him, he has never abandoned me.”
Iye amene anandituma Ine ali nane pamodzi. Iye sanandisiye ndekha popeza nthawi zonse ndimachita zomwe zimamukondweretsa Iye.”
30 As Jesus was saying these things, many people believed that he [was] ([from God/the Messiah]).
Pamene Iye ankayankhula zimenezi, ambiri anamukhulupirira.
31 Then Jesus said to the Jews who now said they believed in him, “If you continue to [live in accordance with] my message, you will truly be my disciples.
Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga.
32 Then you will know [God’s] truth, and as a result of [your believing his] truth, he [PRS] will free you [from being controlled by the one who has made you his slaves].”
Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”
33 They replied to him, “We are descendants of Abraham. We have never been anyone’s slaves. So why do you say [we will] be freed [from being someone’s slaves]?”
Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’”
34 Jesus replied, “Listen carefully to what I am going to tell you. All those who continue to sin are [forced to obey] their sinful desires [MET], [just like] a slave [is forced to obey his master].
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo.
35 A slave is not a permanent member of a family. But a son is a member of a family forever. [Similarly, you say you are members of God’s family because you are descendants of Abraham, but really, because you are like slaves of your sinful desires, you are no longer permanent members of God’s family]. (aiōn g165)
Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. (aiōn g165)
36 So if you allow me to free you, you will truly be free.
Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu.
37 I know that you are Abraham’s descendants. But you are trying to kill me because [you are not] allowing [PRS] my message to continue [to change] your inner being.
Ine ndikudziwa kuti inu ndinu zidzukulu za Abrahamu. Chonsecho inu mwakonzeka kundipha Ine, chifukwa mawu anga alibe malo mwa inu.
38 I am telling you what I saw when I was with [my] Father. But you do the things that you have heard from your father.”
Ine ndikukuwuzani zimene ndaziona pamaso pa Atate, ndipo inu mukuchita zimene mwazimva kwa abambo anu.”
39 They replied to him, “Abraham is our ancestor.” Jesus said to them, “If you were Abraham’s descendants, [your character would be like Abraham’s character, and] you would do [good] things like Abraham did.
Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.” Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita.
40 I have been telling you the truth that I heard from God, but you are trying to kill me. Abraham did not do things like that.
Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi.
41 No! You are doing the things that your [real] father does.” They said to him, “[We do not know about you, but] we are not illegitimate children. And [spiritually], we have only one Father. That is God, and you do not know who your father is!”
Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.” Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”
42 Jesus said to them, “If God were your father, you would love me, because I came from God, and now I have come here [to this world]. My coming was not (because I [appointed] myself/with my own [authority]). He sent me.
Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha.
43 (And I will tell you why you do not understand what I say./Do you know why you do not understand what I say?) [RHQ] It is because you do not want to accept my message.
Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga.
44 You belong to your father, (the devil/Satan), and you desire to do what he wants. He has [caused people to become] murderers from the time when [people] first [sinned]. He has abandoned [God’s] truth because he is a liar by his nature. Whenever he lies, he is speaking according to his [nature], because he is a liar and is the one who originates [MET] all lies.
Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza.
45 But because I tell you the truth, you do not believe me!
Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine!
46 [Since I have never sinned], (none of you can show that I have sinned./can anyone among you show that I have sinned?) [RHQ] So, since I tell you the truth, (there is no good reason for your not believing me!/why is it that you do not believe me?) [RHQ]
Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira?
47 Those who belong to God habitually obey God’s message. You do not belong to God, so you do not obey his message.”
Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”
48 The Jewish [leaders] [SYN] replied to him, “(We are certainly right by saying that you [believe what is false as] the Samaritans [do]!/Are we not right by saying that you [believe what is false as] the Samaritans [do]?) [RHQ] And that (a demon/an evil spirit) [controls] you!”
Ayuda anamuyankha Iye kuti, “Kodi ife sitikulondola ponena kuti Inu ndi Msamariya ndi wogwidwa ndi chiwanda?”
49 Jesus replied, “A demon does not [control] me! I honor my Father, and you do not honor me!
Yesu anati, “Ine sindinagwidwe ndi chiwanda, koma ndimalemekeza Atate anga, koma inu mukundinyoza.
50 I am not trying to honor myself. There is someone else who desires [to honor me], and he is the one who will judge [whether it is I who am telling the truth or whether it is you who are telling the truth].
Ine sindidzifunira ndekha ulemu; koma alipo wina amene amandifunira, ndipo Iyeyo ndiye woweruza.
51 But the truth is that anyone who obeys what I say will never die!” (aiōn g165)
Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.” (aiōn g165)
52 Then the Jewish [leaders] [SYN], [thinking that he was talking about ordinary death and not about spiritual death], said to him, “Now we are sure that a demon [controls] you! Abraham and the prophets died [long ago]! But you say that anyone who obeys what you teach will never die! (aiōn g165)
Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ (aiōn g165)
53 (You are certainly not greater than our ancestor Abraham!/Do you think you are greater than our ancestor Abraham?) [RHQ] He died, and all the prophets died, so who do you think you are [by saying something like that]?”
Kodi ndinu wa mkulu kuposa abambo athu Abrahamu? Iye anafa, ndiponso aneneri onse. Inu mukuganiza kuti ndinu yani?”
54 Jesus replied, “If I were honoring myself, that would be worthless. My Father is the one who you say is your God. He is the one who honors me.
Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemu wangawo ndi wosatanthauza kanthu. Atate anga amene inu mukuti ndi Mulungu wanu, ndiye amene amandilemekeza Ine.
55 Although you do not know him, I know him [and have a close relationship with him]. If I said that I did not know him, I would be a liar like you are. But I know him, and I obey what he says.
Ngakhale kuti inuyo simukumudziwa, Ineyo ndikumudziwa. Ngati Ine nditanena kuti sindikumudziwa, Ineyo nditha kukhala wabodza ngati inuyo, koma Ine ndimamudziwa ndipo ndimasunga mawu ake.
56 Your ancestor Abraham was happy when he thought about what I would [do during] my life [MTY]. [It was as though] he saw that, and was happy.”
Abambo anu Abrahamu anakondwera poyembekezera kubwera kwanga. Iwo anandiona ndipo anasangalala.”
57 Then the Jewish [leaders] [SYN] said to him, “You are not 50 years old yet! So (you certainly did not see him!/how could you have seen him?) [RHQ] [Because he died long ago]!”
Ayuda anati kwa Iye, “Inu sumunafike nʼkomwe zaka makumi asanu, ndipo mukuti munamuona Abrahamu!”
58 Jesus said to them, “The truth is that I existed before Abraham was born!”
Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani choonadi, Abrahamu asanabadwe, Ine Ndine!”
59 So, [because they were very angry about Jesus thus saying that he] ([had eternally existed/was equal with God]), they picked up stones to throw at him [to kill him]. But [Jesus] caused them not to be able to see him, and he left the Temple courtyard.
Pamenepo iwo anatola miyala kuti amugende, koma Yesu anabisala, nachoka mozemba mʼNyumba ya Mulungu.

< John 8 >