< 2 Samuel 4 >

1 When Saul’s son Ishbosheth heard that Abner had been killed at Hebron, [he realized that he might also be killed]. He became discouraged, and all the Israeli people (trembled/became afraid).
Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
2 Ishbosheth had two officers who were leaders of groups that raided other villages. [They were brothers; ] their names were Baanah and Rechab, sons of Rimmon from Beeroth [town] in the tribe of Benjamin. Beeroth is in the area that had [been assigned to] the tribe of Benjamin.
Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
3 But the people of Beeroth had fled to Gittaim [town], and they still live there.
chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
4 Saul’s son Jonathan had a son named Mephibosheth. When Mephibosheth was five years old, Saul and Jonathan died in the battle. When people brought that news from Jezreel, Mephibosheth’s nursemaid picked him up and ran away. She ran very fast, with the result that she dropped him, and his legs became crippled.
(Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
5 One day, Rechab and Baanah left [their home] to go to Ishbosheth’s house. They arrived there about noontime, when Ishbosheth was taking his midday nap.
Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
6 The woman who was the doorkeeper was sifting wheat. While doing that, she became sleepy, and fell asleep. So Rechab and his brother Baanah were able to creep in quietly.
Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
7 They entered Ishbosheth’s bedroom, where he was sleeping. They killed him [with their swords] and cut off his head. They carried his head and walked all night through the Jordan [River] Valley.
Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
8 They took the head of Ishbosheth to David at Hebron. They said to him, “Here is the head of Ishbosheth, the son of your enemy Saul, who tried to kill you. Your majesty, today Yahweh has allowed you to get revenge on Saul and his descendants!”
Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
9 But David replied to them, “Yahweh is the one who has rescued me from all my troubles. And just as surely as Yahweh lives, what I am now saying is also true.
Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
10 When a messenger came to Ziklag and told me ‘Saul is dead!’ and he thought that the news that he was bringing to me was good news, I seized him and [commanded one of my soldiers to] kill him. That was the reward I gave to him for his news!
pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
11 So because you two evil men murdered a man who is (innocent/has done nothing wrong) when he was sleeping on his bed in his own house, I will do something worse to you. I will surely [RHQ] get revenge on you two for murdering [MTY] him, and (wipe you/cause you to disappear) from the earth!”
Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
12 Then, following David’s orders, his soldiers killed the two men, and cut off their hands and their feet, and hung their bodies (OR, their hands and feet) [on a pole] near the pool at Hebron. But they took the head of Ishbosheth and buried it [respectfully] in the tomb of Abner, there at Hebron.
Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.

< 2 Samuel 4 >