< 2 Samuel 3 >

1 There was a long war between those who wanted Saul’s son to be their king and those who wanted David to be their king. But more and more people began to want David to be the king, while the number of people who wanted Saul’s son to be the king continued to become smaller.
Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.
2 David’s wives gave birth to six sons at Hebron. The oldest was Amnon, whose mother was Ahinoam, from Jezreel [city].
Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.
3 The next one was Kileab, whose mother was Abigail, the widow of Nabal, from Carmel [city]. The next one was Absalom, whose mother was Maacah, the daughter of Talmai, the king of [the] Geshur [region].
Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli. Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;
4 The next one was Adonijah, whose mother was Haggith. The next one was Shephatiah, whose mother was Abital.
wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti; wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;
5 The youngest one was Ithream, whose mother was Eglah, [another one of] David’s wives. Those sons of David were all born in Hebron.
ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide. Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.
6 While those who wanted Saul’s son to rule over them and those who wanted David to rule over them continued to fight against each other, Abner was becoming more influential among those who wanted Saul’s son to be the king.
Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli.
7 When Saul was alive, he had as one of his wives a slave woman named Rizpah, the daughter of Aiah. [But one day Abner had sexual relations with her]. So Ishbosheth said to Abner, “Why have you had sexual relations with [EUP] my father’s slave wife?”
Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”
8 Abner became very angry about what Ishbosheth said to him. He said to Ishbosheth, “(Do you think that I am a [worthless] dog [MET] from Judah?/You are treating me as though I am a [worthless] dog [MET] from Judah.) [RHQ] From the beginning, I have been loyal to Saul your father, to his brothers, and to his friends. And I have prevented you from being defeated by David’s army. So now (why are you criticizing me about [what I have done with] some woman?/you should not be criticizing me about [what I have done with] some woman.) [RHQ]
Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu!
9 Yahweh solemnly promised that he would not allow Saul and his descendants to continue to rule. He promised that he would cause David to rule over all the tribes of Israel and Judah, from Dan [city] far in the north to Beersheba [city] far in the south. So I hope/desire that God will punish me severely [HYP] if I do not enable that to happen!”
Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro.
Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.”
11 Ishbosheth was very afraid of Abner, so he did not say anything in reply to Abner.
Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.
12 Then Abner sent messengers to David [when he was at Hebron], to say to him, “[Either you or I] should be [RHQ] the ruler of this entire nation, [but not Isbosheth. However, ] if you make an agreement with me, I will help you by encouraging all the people of Israel to (be want you to be their king/start to support) you.”
Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”
13 David sent back this reply: “Good! I am willing to make an agreement with you. But before that happens, there is one thing that you must do. When you come to see me, you must bring my wife Michal, Saul’s daughter.”
Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.”
14 Then David sent messengers to Ishbosheth, to say to him, “I [had to kill] 100 men from Philistia [and cut off] their foreskins to give to Saul to pay for Michal [to be my wife]. So now give her back to me!”
Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”
15 So Ishbosheth sent some men to take Michal from her husband Palti. But [when they took her, ] her husband followed them all the way to Bahurim [town], crying as he went.
Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi.
16 Then Abner [turned and] said to him, “Go back [home]!”, so he did.
Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.
17 Abner went to the Israeli leaders and talked with them. He said, “For a long time you have wanted David to be your king.
Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu.
18 So now you have an opportunity to do that. Keep in mind that Yahweh promised this: ‘With the help of David, who serves me [well], I will rescue my people from the people of Philistia, and from the power [MTY] of all their other enemies’.”
Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’”
19 Abner also spoke to the people of the tribe of Benjamin. Then he went to Hebron, to tell David what all the people of Israel and the people of the tribe of Benjamin had agreed to do.
Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita.
20 When Abner came with 20 of his soldiers to see David at Hebron, David made a feast for all of them.
Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake.
21 Afterwards, Abner said to David, “Sir/Your majesty, I will now go and encourage all the people of Israel to accept you to be their king, as you have desired.” Then Abner left, peacefully.
Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.
22 Soon after that, Joab and some of David’s other soldiers returned [to Hebron] after raiding [one of their enemies’ villages], bringing with them a lot of things that they had captured. But Abner was not there at Hebron, because David had sent him safely home.
Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere.
23 When Joab and the soldiers who were with him arrived, someone told him that Abner had come there and talked with the king, and that the king allowed to go home safely.
Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.
24 So Joab went to the king and said, “Why have you done that? Listen to me! Abner [is your enemy, but] when he came to you, you allowed him [RHQ] to leave!
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
25 Do you not know that he came to you to deceive you and to find out everything that you are doing, and all the places that you go to?”
Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”
26 After Joab left David, he sent some messengers to get Abner. They found him at Sirah Well, and brought him back to Hebron, but David did not know that they had done that.
Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi.
27 So when Abner returned to Hebron, Joab met him at the city gate, and took him aside as though he wanted to speak with him privately. Then he stabbed Abner in the stomach [with his knife/sword]. In that way he murdered Abner because Abner had killed [MTY] Joab’s brother Asahel.
Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.
28 Later, after David heard what had happened, he said, “Yahweh knows that I and the people of my kingdom are not at all (responsible for/guilty of) murdering [MTY] Abner.
Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri.
29 I hope/desire that Joab and all his family will be punished [MTY] for doing that! I hope/desire that there will always be someone in his family who has sores, or someone who is a leper, or some man who is forced to do women’s work, or someone who is killed in a battle, or someone who does not have enough food to eat!”
Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”
30 That is how Joab and his brother Abishai murdered Abner, because he had killed their brother Asahel in the battle at Gibeon.
(Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).
31 Then David said to Joab and to all Joab’s soldiers, “Tear your clothes and put on coarse cloth [to show that you are sad], and mourn for Abner!” And [at the funeral], King David walked behind [the men who were carrying] the coffin.
Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho.
32 They buried Abner’s body at Hebron. And at the grave, the king cried loudly, and all the other people also cried.
Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.
33 David sang this sad song to lament for Abner: “It is not right that [RHQ] Abner died like outlaws die!
Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri: “Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
34 No one tied his hands or put chains on his feet, [like they do to criminals]. No, he was murdered by wicked men!”
Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.
35 Then many [HYP] people came to David to tell him to eat some food before sunset, but David refused. He said, “I hope/desire that God will punish me severely [HYP] if I eat any food before the sun goes down!”
Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”
36 All the people saw what David did, and they were pleased. Truly, everything that the king did pleased the people.
Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa.
37 So all the people realized that the king had not wanted Abner to be killed.
Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.
38 The king said to his officials, “(Do you not realize that a leader and a great man has died today in Israel?/You should realize that a leader and a great man has died today in Israel.) [RHQ]
Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu?
39 Even though Yahweh appointed me to be the king, today I feel weak. These two sons of Zeruiah, [Joab and Abishai], are very violent; I cannot control them. So I hope/desire that Yahweh will punish them severely in return for this wicked thing that they have done!”
Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”

< 2 Samuel 3 >