< Psalms 71 >

1 in/on/with you LORD to seek refuge not be ashamed to/for forever: enduring
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 in/on/with righteousness your to rescue me and to escape me to stretch to(wards) me ear your and to save me
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 to be to/for me to/for rock habitation to/for to come (in): come continually to command to/for to save me for crag my and fortress my you(m. s.)
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 God my to escape me from hand: power wicked from palm to act unjustly and to oppress
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 for you(m. s.) hope my Lord YHWH/God confidence my from youth my
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 upon you to support from belly: womb from belly mother my you(m. s.) to cut me in/on/with you praise my continually
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 like/as wonder to be to/for many and you(m. s.) refuge my strength
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 to fill lip my praise your all [the] day beauty your
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 not to throw me to/for time old age like/as to end: expend strength my not to leave: forsake me
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 for to say enemy my to/for me and to keep: look at soul: life my to advise together
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 to/for to say God to leave: forsake him to pursue and to capture him for nothing to rescue
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 God not to remove from me God my to/for help my (to hasten [emph?] *Q(K)*)
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 be ashamed to end: destroy to oppose soul: myself my to enwrap reproach and shame to seek distress: harm my
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 and I continually to wait: hope and to add upon all praise your
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 lip my to recount righteousness your all [the] day deliverance: salvation your for not to know number
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 to come (in): come in/on/with might Lord YHWH/God to remember righteousness your to/for alone you
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 God to learn: teach me from youth my and till here/thus to tell to wonder your
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 and also till old age and greyheaded God not to leave: forsake me till to tell arm your to/for generation to/for all to come (in): come might your
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 and righteousness your God till height which to make: do great: large God who? like you
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 which (to see: see me *Q(K)*) distress many and bad: harmful to return: again (to live me *Q(K)*) and from abyss [the] land: country/planet to return: again to ascend: establish me
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 to multiply greatness my and to turn: again to be sorry: comfort me
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 also I to give thanks you in/on/with article/utensil harp truth: faithful your God my to sing to/for you in/on/with lyre holy Israel
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 to sing lips my for to sing to/for you and soul my which to ransom
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 also tongue my all [the] day to mutter righteousness your for be ashamed for be ashamed to seek distress: harm my
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

< Psalms 71 >