< Psalms 70 >

1 to/for to conduct to/for David to/for to remember God to/for to rescue me LORD to/for help my to hasten [emph?]
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho. Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
2 be ashamed and be ashamed to seek soul: life my to turn back and be humiliated delighting distress: harm my
Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu.
3 to return: return upon consequence shame their [the] to say Aha! Aha!
Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.
4 to rejoice and to rejoice in/on/with you all to seek you and to say continually to magnify God to love: lover salvation your
Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
5 and I afflicted and needy God to hasten [emph?] to/for me helper my and to escape me you(m. s.) LORD not to delay
Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.

< Psalms 70 >