< Job 19 >
1 And he answered Job and he said.
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Until when? will you torment! self my and will you crush? me with words.
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 This ten times you have insulted me not you have been ashamed you have ill-treated me.
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 And even truly I have erred with me it lodges error my.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 If truly above me you will magnify yourselves and you may argue on me disgrace my.
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Know then that God he has wronged me and net his over me he has closed.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 There! I cry out violence and not I am answered I cry for help and there not [is] justice.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 Way my he has walled up and not I will pass and on paths my darkness he puts.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 Honor my from on me he has stripped off and he has removed [the] crown of head my.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 He has torn down me all around and I have gone and he has uprooted like a tree hope my.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 And he has kindled towards me anger his and he has considered me himself like foes his.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 Together - they have come troops his and they have piled up on me way their and they have encamped all around tent my.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 Brothers my from with me he has put far away and acquaintances my surely they have become estranged from me.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 They have ceased kindred my and acquaintances my they have forgotten me.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 [the] sojourners of House my and female servants my to a stranger they consider me a foreigner I have become in view their.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 To servant my I call and not he answers with mouth my I seek favor to him.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 Breath my it is loathsome to wife my and I am repulsive to [the] sons of womb my.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Also young boys they reject me I arise and they spoke against me.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 They abhor me all [the] men of council my and whom I love they have turned against me.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 On skin my and on flesh my it clings bone my and I have escaped! with [the] skin of teeth my.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Show favor to me show favor to me O you friends my for [the] hand of God it has touched me.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Why? are you persecuting me like God and from flesh my not are you satisfied?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 Who? will he give then and they will be written down! words my who? will he give on the scroll so they may be inscribed.
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 With a stylus of iron and lead for ever in the rock they will be engraved!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 And I I know vindicator my he lives and last on dust he will stand.
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 And after skin my people have struck off this and from flesh my I will see God.
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Whom I - I will see for myself and own eyes my they will see and not a stranger they are faint kidneys my in bosom my.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 If you will say what? will we persecute him and [the] root of [the] matter it has been found in me.
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Be afraid yourselves - of [the] sword for rage [is] iniquities of [the] sword so that you may know! (that a judgment. *Q(k)*)
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”