< Job 18 >

1 And he answered Bildad the Shuhite and he said.
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Until when? - will you make! ends of words you will consider and after we will speak.
“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
3 Why? are we regarded like cattle are we considered stupid? in view your.
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
4 O [one who] tears self his in anger his ¿ for sake your may it be abandoned [the] earth so it may move? a rock from place its.
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
5 Also [the] light of wicked [people] it is extinguished and not it shines [the] flame of fire his.
“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
6 [the] light It grows dark in tent his and lamp his above him it is extinguished.
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
7 They are restricted [the] steps of vigor his and it throws down him own plan[s] his.
Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
8 For he is caught in a net by feet his and on a network he walks about.
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
9 It takes hold on a heel a trap it takes hold on him a snare.
Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 [is] hidden On the ground rope his and trap his on [the] path.
Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
11 All around they terrify him sudden terror and they scatter him to feet his.
Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 It is hungry trouble his and disaster [is] prepared for stumbling his.
Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
13 It consumes [the] parts of skin his it consumes parts his [the] firstborn of death.
Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 He is torn away from tent his trust his and it makes march him to [the] king of sudden terror.
Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 It dwells in tent his because not [belonging] to him it is scattered over estate his sulfur.
Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 Beneath roots his they are dried up and above it withers branch[es] his.
Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
17 Memory his it perishes from [the] earth and not a name [belongs] to him on [the] face of [the] street.
Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 People drive him from light into darkness and from [the] world they chase away him.
Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 Not posterity [belongs] to him and not progeny [is] among people his and there not [is] a survivor in sojourning-places his.
Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 On day his they are appalled [those] behind and [those] before they take hold of a shudder.
Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Surely these [are] [the] dwelling places of an evil-doer and this [is the] place of [one who] not he knows God.
Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

< Job 18 >