< Isaiah 23 >
1 [the] oracle of Tyre wail - O ships of Tarshish for it has been devastated from house from coming from [the] land of Cyprus it has been revealed to them.
Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
2 Be silent O inhabitants of [the] coastland [the] trader of Sidon [who] passed over [the] sea they have filled you.
Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
3 And on waters many [was] [the] seed of Shihor [the] harvest of [the] River revenue her and it became [the] traffic of nations.
Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
4 Be ashamed O Sidon for it has said [the] sea [the] stronghold of the sea saying not I have been in labor and not I have given birth and not I have brought up young men I have raised young women.
Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
5 When a report [is] to Egypt people will be in anguish like [the] report of Tyre.
Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
6 Pass over Tarshish towards wail O inhabitants of [the] coastland.
Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
7 ¿ [is] this Of you jubilant [city] [which is] from days of antiquity beginning its [which] they have carried it feet its from a distance to sojourn.
Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
8 Who? did he plan this on Tyre which bestows crowns which traders its [were] princes merchants its [were the] honored [people] of [the] earth.
Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
9 Yahweh of hosts he planned it to profane [the] pride of all splendor to treat with contempt all [the] honored [people] of [the] earth.
Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
10 Pass over land your like the River O daughter of Tarshish there not [is] a restraint still.
Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
11 Hand his he has stretched out over the sea he has made tremble kingdoms Yahweh he has commanded concerning Canaan to destroy strongholds its.
Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
12 And he said not you will repeat again to exult O oppressed [one] [the] virgin of [the] daughter of Sidon (Cyprus *Q(k)*) arise pass over also there not it will be rest to you.
Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
13 There! - [the] land of [the] Chaldeans this [is] the people [which] not it was Assyria it allocated it to desert-dwellers they raised up (siege-towers its *Q(k)*) they stripped bare palaces its it made it a ruin.
Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
14 Wail O ships of Tarshish for it has been devastated stronghold your.
Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
15 And it will be in the day that and [will be] forgotten Tyre seventy year[s] like [the] days of a king one from [the] end of seventy year[s] it will happen to Tyre like [the] song of the prostitute.
Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
16 Take a harp go around [the] city O prostitute forgotten do well to play multiply song so that you may be remembered.
“Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
17 And it will be from [the] end of - seventy year[s] he will visit Yahweh Tyre and it will return to hire its and it will act [the] prostitute with all [the] kingdoms of the earth on [the] surface of the earth.
Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
18 And it will be profit its and hire its a holy thing to Yahweh not it will be stored up and not it will be hoarded for to [those who] dwell before Yahweh it will belong profit its for eating to satiety and for covering magnificent.
Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.