< Isaiah 22 >
1 [the] oracle of [the] valley of Vision what? [is] to you then that you have gone up all of you to the roofs.
Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
2 Noises - full O city turbulent O town jubilant slain [ones] your not [are] slain of a sword and not [are] dead of battle.
Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
3 All rulers your they have fled together from a bow they have been captured all found [ones] your they were captured together from a distance they had fled.
Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
4 There-fore I said look away from me I will show bitterness with weeping may not you insist to comfort me on [the] devastation of [the] daughter of people my.
Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
5 For a day of consternation and trampling and confusion [belongs] to [the] Lord Yahweh of hosts in [the] valley of vision a breaking down of a wall and a crying out to the mountain.
Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
6 And Elam it took up a quiver with chariotry of a man horsemen and Kir it uncovered a shield.
Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
7 And it was [the] choicest of valleys your they were full chariotry and the horsemen certainly they took a stand the gate towards.
Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
8 And he uncovered [the] covering of Judah and you looked in the day that to [the] weaponry of [the] House of the Forest.
zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
9 And [the] breaches of [the] city of David you saw that they were many and you gathered [the] waters of the pool lower.
inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
10 And [the] houses of Jerusalem you counted and you pulled down the houses to fortify the city wall.
Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
11 And a reservoir - you made between the two walls for [the] water of the pool old and not you looked to [the] [one who] made it and [the] [one who] planned it from distant [time] not you considered.
Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
12 And he called [the] Lord Yahweh of hosts in the day that for weeping and for wailing and for baldness and for girding of sackcloth.
Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
13 And there! - joy and gladness they are killing - cattle and they are slaughtering sheep they are eating meat and they are drinking wine we will eat and we will drink for tomorrow we will die.
Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
14 And he has revealed himself in ears my Yahweh of hosts if it will be atoned for (the iniquity *LA(bh)*) this for you until you will die! he says [the] Lord Yahweh of hosts.
Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
15 Thus he says [the] Lord Yahweh of hosts come go to the steward this to Shebna who [is] over the house.
Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
16 What? [belongs] to you here and who? [belongs] to you here that you have dug out for yourself here a tomb digging out high place tomb his cutting in the rock a dwelling for himself.
Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
17 There! Yahweh [is] about to hurl away you hurling O man and [is] about to grasp you completely.
“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
18 Certainly he will wind up you a winding a ball to a land broad of both hands there you will die and there [the] chariots of splendor your [will be] [the] disgrace of [the] house of master your.
Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
19 And I will push you from office your and from post your he will tear down you.
Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
20 And it will be in the day that and I will summon servant my Eliakim [the] son of Hilkiah.
“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
21 And I will clothe him tunic your and sash your I will make firm on him and authority your I will put in hand his and he will become a father of [the] inhabitant[s] of Jerusalem and of [the] house of Judah.
Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
22 And I will put [the] key of [the] house of David on shoulder his and he will open and there not [will be one who] shuts and he will shut and there not [will be one who] opens.
Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
23 And I will drive him a tent peg in a place firm and he will become a seat of honor for [the] house of father his.
Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
24 And they will hang on him all - [the] honor of [the] house of father his the descendants and the offshoot all [the] vessels of the small from [the] vessels of the bowls and unto all [the] vessels of the jars.
Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
25 In the day that [the] utterance of Yahweh of hosts it will be removed the tent peg that was driven in a place firm and it will be cut down and it will fall and it will be cut off the burden which [was] on it for Yahweh he has spoken.
“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.