< Job 18 >

1 Then responded Bildad the Shuhite, and said: —
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 How long will ye make a perversion of words? Ye should understand, and, afterwards, we could speak.
“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
3 Wherefore are we accounted like beasts? or appear stupid, in thine eyes?
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
4 One tearing in pieces his own soul in his anger, —For thy sake, shall the earth be forsaken? or the rock be moved out of its place?
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
5 Even the light of the lawless, shall go out, —Neither shall shine the flame of his fire;
“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
6 The light, hath darkened in his tent, Yea, his lamp above him, goeth out;
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
7 The steppings of his strength are hemmed in, and his own counsel casteth him down;
Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
8 For he is thrust into a net by his own feet, and, upon a trap, he marcheth;
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
9 There catcheth him—by the heel—a gin, there holdeth him fast—a noose:
Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 Concealed in the ground is a cord for him, —and a snare for him, on the path.
Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
11 Round about, terrors have startled him, and have driven him to his feet.
Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 Let his strength be famished, and, calamity, be ready at his side;
Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
13 Let it devour the members of his body, Let the firstborn of death devour his members;
Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 Uprooted, out of his tent, be his confidence, and let it drive him down to the king of terrors;
Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 There shall dwell in his tent, what is naught-of-his, Let brimstone be strewed over his dwelling;
Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 Beneath, let his roots be dried up, and, above, be cut off his branch;
Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
17 His memorial, have perished out of the land, and let him have no name over the face of the open field;
Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 Let them thrust him out of light into darkness, Yea, out of the world, let them chase him;
Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 Let him have neither scion nor seed among his people, neither any survivor in his place of sojourn:
Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 Over his day, have they been astounded who come behind, and, them who are in advance, a shudder hath seized.
Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Surely, these, are the dwellings of him that is perverse, and, this, is the place of him that knoweth not GOD.
Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

< Job 18 >