< Job 17 >
1 My spirit, is broken, My days, are extinguished, Graves, are left me.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 Verily there are mockers, with me! And, on their insults, mine eye doth rest.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 Appoint it, I pray thee—be thou surety for me with thyself, Who is there that, on my side, can pledge himself?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 For, their heart, hast thou kept back from understanding, On this account, thou wilt not exalt them.
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 He that, for a share, denounceth friends, even, the eyes of his children, shall be dim.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 But he hath set me, as the byword of peoples, And, one to be spit on in the face, do I become.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 Therefore hath mine eye become dim from vexation, and, my members, are like a shadow, all of them.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 Upright men shall be astounded over this, and, the innocent, against the impious, shall rouse themselves.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 That the righteous may hold on his way, and, the clean of hands, increase in strength.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 But indeed, as for them all, will ye bethink yourselves and enter into it, I pray you? Or shall I not find, among you, one who is wise?
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 My days, are past, my purposes, are broken off, the possessions of my heart!
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 Night for day, they appoint, Light, is near, by reason of darkness!
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 If I wait for hades as my house, in darkness, have spread out my couch; (Sheol )
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol )
14 To corruption, have exclaimed, My father, thou! My mother! and My sister! to the worm.
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 Where then would be my hope? And, as for my blessedness, who should see it!
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 With me to hades, would they go down, If, wholly—into the dust, is the descent! (Sheol )
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol )