< Jeremiah 36 >

1 And it came to pass, in the fourth year of Jehoiakim son of Josiah, king of Judah, that this word came unto Jeremiah from Yahweh, saying:
Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Take thee a scroll, and write therein all the words which I have spoken unto thee concerning Israel and concerning Judah and concerning all the nations, —from the day I began to speak unto thee from the days of Josiah, even until this day:
“Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
3 Peradventure, the house of Judah will hearken unto all the calamity, which I am devising to execute against them, —to the end they may return every man from his wicked way, whereupon I will forgive their iniquity, and their sin.
Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
4 So Jeremiah called Baruch, son of Neriah, —and Baruch wrote, from the mouth of Jeremiah, all the words of Yahweh which he had spoken unto him upon a scroll.
Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
5 Then did Jeremiah command Baruch, saying, —I, am hindered, I cannot enter the house of Yahweh;
Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
6 Thou, therefore shalt enter and read in the roll which thou hast written from my mouth the words of Yahweh in the ears of the people in the house of Yahweh on the day of a fast, —moreover also, in the ears of all Judah who are coming in out of their cities, shalt thou read them:
Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
7 Peradventure, their supplication, will fall prostrate, before Yahweh, and they return every man from his wicked way, —For, great, are the anger and the indignation which Yahweh hath spoken against this people.
Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
8 So then Baruch son of Neriah did according to all which Jeremiah the prophet commanded him, reading in the book the words of Yahweh in the house of Yahweh.
Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
9 And it came to pass in the fifth year of Jehoiakim son of Josiah king of Judah in the ninth month, that all the people of Jerusalem, and all the people who were coming in out of the cities of Judah into Jerusalem, had proclaimed a fast before Yahweh;
Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
10 Baruch, therefore, read in the book the words of Jeremiah, in the house of Yahweh, —in the chamber of Gemariah son of Shaphan—the scribe, in the upper court, at the opening of the new gate of the house of Yahweh, in the ears of all the people.
Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
11 When Micaiah, son of Gemariah son of Shaphan, heard all the words of Yahweh out of the book,
Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
12 then went he down unto the house of the king up to the chamber of the scribe, and lo! there, all the princes sitting, —Elishama the scribe, and Delaiah son of Shemaiah, and Elnathan son of Achbor, and Gemariah son of Shaphan and Zedekiah son of Hananiah, and all the princes,
anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
13 So Micaiah told them all the words which he heard, —when Baruch read in the book in the ears of the people.
Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
14 All the princes, therefore sent unto Baruch, Jehudi, son of Nethaniah son of Shelemiah son of Cushi saying, The roll wherein thou didst read in the ears of the people, take it in thy hand, and come, So Baruch son of Neriah took the roll in his hand, and came in unto them.
Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
15 Then said they unto him, Sit down we pray thee and read it in our ears, So Baruch read it in their ears.
Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
16 And it came to pass when they heard all the words, that they turned with fear one to another, —and said unto Baruch, We must, surely tell, the king, all these words!
Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
17 Then unto Baruch, put they questions saying, —Tell us, we pray thee, How, didst thou write all these words at his mouth?
Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
18 So Baruch said unto them, With his own mouth, used he to proclaim unto me all these words, —and I kept on writing in the book, with ink.
Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
19 Then said the princes unto Baruch, Go hide thee, thou and Jeremiah, and let no man, know where ye, are!
Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
20 Then went they in unto the king, into the court, but the roll, had they put in charge, in the chamber of Elishama the scribe, —so they declared in the ears of the king all the words.
Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
21 The king, therefore sent, Jehudi, to fetch the roll, and he fetched it out of the chamber of Elishama the scribe, —and Jehudi read it in the ears of the king, and in the ears of all the princes who were standing near the king.
Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
22 Now, the king, was sitting in the winter house in the ninth month, —with the fire-stove before him burning.
Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
23 So then it came to pass when Jehudi had read three or four columns that he cut it up into fragments with a scribe’s knife, and cast them into the fire that was in the stove, —until, all the roll, was consumed on the fire that was on the stove.
Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
24 Yet were they not in dread, neither rent they their garments, —the king, nor any of his servants that were hearing all these words.
Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
25 Nevertheless Elnathan and Delaiah and Gemariah, interceded with the king, not to burn the roll, —but he hearkened not unto them.
Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
26 Then did the king command Jerahmeel son of the king, and Seraiah son of Azriel, and Shelemiah son of Abdeel, to fetch Baruch the scribe, and Jeremiah the prophet, —but Yahweh had hid them.
Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
27 Then came the word of Yahweh unto Jeremiah, after the king had burned the roll, and the words which Baruch had written from the mouth of Jeremiah saying:
Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
28 Again take thee another roll, and write thereon, all the former words which were on the first roll, which Jehoiakim king of Judah hath burned.
“Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
29 But unto Jehoiakim king of Judah, shalt thou say, Thus, saith Yahweh, —Thou, hast burned this roll saying, Why hast thou written thereon—saying, The king of Babylon shall, certainly, come and lay waste this land, and cause to cease therefrom man and beast?
Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
30 Therefore, Thus, saith Yahweh, Concerning Jehoiakim king of Judah, —He shall have none to sit upon the throne of David, —And, his dead body, shall be cast out—to the heat by day, and to the frost by night;
Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
31 And I will visit upon him and upon his seed and upon his servants the punishment of their iniquity, —and will bring upon them and upon the inhabitants of Jerusalem and against, the men of Judah, all the calamity, which I have spoken against them but they have not hearkened.
Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
32 So, Jeremiah, took another roll and gave it unto Baruch son of Neriah the scribe, who wrote thereon, from the mouth of Jeremiah all the words of the book, which Jehoiakim king of Judah had burned, in the fire, —and further were added thereunto many words like unto them
Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.

< Jeremiah 36 >