< Zephaniah 3 >

1 Woe to her that is rebellious and polluted, The oppressing city!
Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
2 She listeneth to no voice, She receiveth not admonition; She trusteth not in Jehovah, She draweth not near to her God.
Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
3 Her princes within her are roaring lions; Her judges are evening wolves; They reserve nothing for the morning.
Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
4 Her prophets are vainglorious, Men of treachery; Her priests pollute the sanctuary, They violate the law.
Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
5 But Jehovah is just in the midst of her; He doeth no iniquity. Every morning bringeth he his righteousness to light; he faileth not; Yet the wicked knoweth not shame.
Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
6 I have cut off nations; their towers are destroyed; I have laid waste their streets so that none passeth through; Their cities are made desolate, without a man, without an inhabitant.
“Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
7 Then I said, “Surely thou wilt fear me; thou wilt receive admonition, That thy habitation may not be cut off, As I have commanded concerning thee.” But they were diligent to commit iniquity In all their doings.
Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
8 Therefore wait for me, saith Jehovah. Until the day when I rise up to the prey. For my purpose is to gather the nations, to assemble the kingdoms, To pour upon them my indignation, Even all the heat of my wrath. For with the fire of mine anger shall all the earth be devoured.
Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
9 Then will I again bestow upon the nations pure lips, So that they shall all of them call upon the name of Jehovah, And serve him with one consent.
“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 From beyond the rivers of Ethiopia My suppliants, the sons of my dispersed ones, shall bring my offering.
Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
11 In that day thou shalt not be ashamed For all thy doings, wherein thou hast transgressed against me; For I will take away from the midst of thee thy proud exulters, And thou shalt no more exalt thyself upon my holy mountain.
Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
12 I will leave in the midst of thee a humble and lowly people, Who trust in the name of Jehovah.
Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
13 The residue of Israel shall not do iniquity, nor speak falsehood; Neither shall a deceitful tongue be found in their mouth; Therefore shall they feed and lie down, and none shall make them afraid.
Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
14 Sing, O daughter of Zion! Shout, O Israel! Rejoice and exult with all thy heart, O daughter of Jerusalem!
Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 Jehovah hath taken away thy punishments; He hath removed thine enemies. The king of Israel, Jehovah, is in the midst of thee; Thou shalt see evil no more.
Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
16 In that day shall it be said to Jerusalem, Fear not! And to Zion, Let not thy hands hang down!
Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
17 Jehovah thy God will be in the midst of thee; The mighty one will save thee. He will rejoice over thee with gladness; He will pardon thee in his love; He will exult over thee with singing.
Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
18 I will gather them that mourn, far from the solemn assembly, They were far from thee; the reproach was a burden upon thee.
“Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Behold, at that time I will destroy all that afflict thee; And I will save the halting, and gather the scattered, And I will make them a praise and a name In every land where they have been put to shame.
Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 At that time I will bring you back, And at that time I will gather you; For I will make you a name and a praise among all the nations of the earth, When I bring back your captives before your eyes, saith Jehovah.
Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.

< Zephaniah 3 >