< Micah 7 >
1 Woe is me! I live where the summer fruits are gathered, And the vintage is gleaned; There is no cluster to eat; I long for the first-ripe fig.
Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
2 The good man is perished from the land, And there is none upright among men. They all lie in wait for blood; Every one hunteth his brother with a net.
Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
3 Their hands are diligent for evil; The prince asketh a bribe, And the judge decideth for money! The great man giveth judgment according to his desire; They conspire to pervert justice.
Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
4 The best of them is like a brier; The most upright of them is sharper than a thorn-hedge. The day of recompense, announced by thy watchmen, cometh; Then shall come their perplexity.
Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
5 Trust ye not in a friend! Put no confidence in a guide! From her that lieth in thy bosom Keep the doors of thy mouth!
Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
6 For the son dishonoreth his father, The daughter riseth up against her mother, And the daughter-in-law against her mother-in-law; The inmates of a man's house are his foes.
Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
7 I will look to Jehovah; I will hope in the God of my salvation; My God will hear me.
Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
8 Rejoice not over me, O my enemy! Though I have fallen, I shall arise; Though I sit in darkness, Jehovah will be my light.
Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
9 I will bear the indignation of Jehovah, Because I have sinned against him, Until he maintain my cause, and execute judgment for me, Until he bring me to the light, And I behold his mercy.
Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
10 She that is my enemy shall see it, and shame shall cover her, That said to me, Where is Jehovah thy God? Mine eyes shall gaze upon her; Soon shall she be trodden down, as the mire of the streets.
Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
11 The day cometh when thy walls are to be built; In that day shall the decree be far removed.
Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
12 In that day shall they come to thee From Assyria, and the cities of Egypt, And from Egypt to the river, From sea to sea, from mountain to mountain.
Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
13 But first the land shall be desolate on account of its inhabitants, For the fruit of their doings.
Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
14 Feed thy people with thy crook, The flock of thine inheritance, That dwell solitarily in the forest in the midst of Carmel! Let them feed in Bashan and Gilead, as in the days of old.
Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
15 As in the day when thou camest from Egypt, So will I show thee wonders.
“Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
16 The nations shall see, and be ashamed of all their might: They shall lay their hands upon their mouths; Their ears shall be deaf.
Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
17 They shall lick the dust like the serpent; Like the creeping things of the earth, they shall come trembling from their strongholds; To Jehovah our God shall they come with awe, And shall fear on account of thee.
Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
18 Who is a God like thee, that pardoneth iniquity and passeth by transgression, In the remnant of his inheritance? He retaineth not his anger forever, For he delighteth in mercy.
Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
19 He will again have compassion on us, He will blot out our iniquities; Yea, thou wilt cast all our sins into the depths of the sea.
Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
20 Thou wilt show faithfulness to Jacob, And mercy to Abraham, Which thou swarest to our fathers from the days of old.
Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.