< Job 23 >

1 Then Job answered,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 "Even today my complaint is rebellious. His hand is heavy in spite of my groaning.
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 Oh that I knew where I might find him. That I might come even to his seat.
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 I would set my cause in order before him, and fill my mouth with arguments.
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 I would know the words which he would answer me, and understand what he would tell me.
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 Would he contend with me in the greatness of his power? No, but he would listen to me.
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 There the upright might reason with him, so I should be delivered forever from my judge.
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 "If I go east, he is not there; if west, I can't find him;
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 He works to the north, but I can't see him. He turns south, but I can't catch a glimpse of him.
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 But he knows the way that I take. When he has tried me, I shall come forth like gold.
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 My foot has held fast to his steps. I have kept his way, and not turned aside.
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 I haven't gone back from the commandment of his lips. I have treasured up the words of his mouth more than my necessary food.
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 But he stands alone, and who can oppose him? What his soul desires, even that he does.
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 For he performs that which is appointed for me. Many such things are with him.
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 Therefore I am terrified at his presence. When I consider, I am afraid of him.
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 For God has made my heart faint. Shaddai has terrified me.
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 Because I was not cut off before the darkness, neither did he cover the thick darkness from my face.
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

< Job 23 >