< Job 22 >

1 Then Eliphaz the Temanite answered,
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 "Can a man be profitable to God? Surely he who is wise is profitable to himself.
“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
3 Is it any pleasure to Shaddai, that you are righteous? Or does it benefit him, that you make your ways perfect?
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
4 Is it for your piety that he reproves you, that he enters with you into judgment?
“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
5 Isn't your wickedness great? Neither is there any end to your iniquities.
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
6 For you have taken pledges from your brother for nothing, and stripped the naked of their clothing.
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
7 You haven't given water to the weary to drink, and you have withheld bread from the hungry.
Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
8 But as for the mighty man, he had the earth. The honorable man, he lived in it.
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
9 You have sent widows away empty, and the arms of the fatherless have been broken.
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
10 Therefore snares are around you. Sudden fear troubles you,
Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
11 or darkness, so that you can not see, and floods of waters cover you.
nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
12 "Isn't God in the heights of heaven? See the height of the stars, how high they are.
“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
13 You say, 'What does God know? Can he judge through the thick darkness?
Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
14 Thick clouds are a covering to him, so that he doesn't see. He walks on the vault of the sky.'
Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
15 Will you keep the old way, which wicked men have trodden,
Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
16 who were snatched away before their time, whose foundation was poured out as a stream,
Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
17 who said to God, 'Depart from us;' and, 'What can Shaddai do for us?'
Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
18 Yet he filled their houses with good things, but the counsel of the wicked is far from me.
Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
19 The righteous see it, and are glad. The innocent ridicule them,
“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
20 saying, 'Surely those who rose up against us are cut off. The fire has consumed the remnant of them.'
Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
21 "Acquaint yourself with him, now, and be at peace. Thereby good shall come to you.
“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
22 Please receive instruction from his mouth, and lay up his words in your heart.
Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
23 If you return to Shaddai, you shall be built up, if you put away unrighteousness far from your tents.
Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
24 Lay your treasure in the dust, the gold of Ophir among the stones of the brooks.
ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
25 Shaddai will be your treasure, and precious silver to you.
Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
26 For then you will delight yourself in Shaddai, and shall lift up your face to God.
Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
27 You shall make your prayer to him, and he will hear you. You shall pay your vows.
Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
28 And you will also decree a thing, and it will be established for you, and light will shine on your ways.
Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
29 When they cast down, you shall say, 'be lifted up.' And he will save the humble.
Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
30 He will even deliver him who is not innocent. Yes, he shall be delivered through the cleanness of your hands."
Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”

< Job 22 >