< Psalms 122 >

1 A Song of Ascents; of David. I rejoiced when they said unto me: 'Let us go unto the house of the LORD.'
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
2 Our feet are standing within thy gates, O Jerusalem;
Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
3 Jerusalem, that art builded as a city that is compact together;
Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
4 Whither the tribes went up, even the tribes of the LORD, as a testimony unto Israel, to give thanks unto the name of the LORD.
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
5 For there were set thrones for judgment, the thrones of the house of David.
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
6 Pray for the peace of Jerusalem; may they prosper that love thee.
Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
7 Peace be within thy walls, and prosperity within thy palaces.
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
8 For my brethren and companions' sakes, I will now say: 'Peace be within thee.'
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
9 For the sake of the house of the LORD our God I will seek thy good.
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.

< Psalms 122 >