< Psalms 41 >
1 For the Leader. A Psalm of David. Happy is he that considereth the poor; the LORD will deliver him in the day of evil.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka; Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.
2 The LORD preserve him, and keep him alive, let him be called happy in the land; and deliver not Thou him unto the greed of his enemies.
Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake; Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.
3 The LORD support him upon the bed of illness; mayest Thou turn all his lying down in his sickness.
Yehova adzamuthandiza pamene akudwala ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.
4 As for me, I said: 'O LORD, be gracious unto me; heal my soul; for I have sinned against Thee.'
Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo; chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”
5 Mine enemies speak evil of me: 'When shall he die, and his name perish?'
Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti, “Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”
6 And if one come to see me, he speaketh falsehood; his heart gathereth iniquity to itself; when he goeth abroad, he speaketh of it.
Pamene wina abwera kudzandiona, amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe; kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.
7 All that hate me whisper together against me, against me do they devise my hurt:
Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane, iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,
8 'An evil thing cleaveth fast unto him; and now that he lieth, he shall rise up no more.'
“Matenda owopsa amugwira; sadzaukapo pamalo pamene wagona.”
9 Yea, mine own familiar friend, in whom I trusted, who did eat of my bread, hath lifted up his heel against me.
Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira, iye amene amadya pamodzi ndi ine watukula chidendene chake kulimbana nane.
10 But Thou, O LORD, be gracious unto me, and raise me up, that I may requite them.
Koma Yehova mundichititre chifundo, dzutseni kuti ndiwabwezere.
11 By this I know that Thou delightest in me, that mine enemy doth not triumph over me.
Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane, pakuti mdani wanga sandigonjetsa.
12 And as for me, Thou upholdest me because of mine integrity, and settest me before Thy face for ever.
Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.
13 Blessed be the LORD, the God of Israel, from everlasting and to everlasting. Amen, and Amen.
Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli kuchokera muyaya mpaka muyaya. Ameni ndi Ameni.