< Genesis 5 >

1 This is the book of the generations of Adam. In the day that God created man, in the likeness of God made He him;
Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
2 male and female created He them, and blessed them, and called their name Adam, in the day when they were created.
Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
3 And Adam lived a hundred and thirty years, and begot a son in his own likeness, after his image; and called his name Seth.
Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
4 And the days of Adam after he begot Seth were eight hundred years; and he begot sons and daughters.
Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
5 And all the days that Adam lived were nine hundred and thirty years; and he died.
Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
6 And Seth lived a hundred and five years, and begot Enosh.
Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
7 And Seth lived after he begot Enosh eight hundred and seven years, and begot sons and daughters.
Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
8 And all the days of Seth were nine hundred and twelve years; and he died.
Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
9 And Enosh lived ninety years, and begot Kenan.
Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
10 And Enosh lived after he begot Kenan eight hundred and fifteen years, and begot sons and daughters.
Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
11 And all the days of Enosh were nine hundred and five years; and he died.
Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
12 And Kenan lived seventy years, and begot Mahalalel.
Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
13 And Kenan lived after he begot Mahalalel eight hundred and forty years, and begot sons and daughters.
Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
14 And all the days of Kenan were nine hundred and ten years; and he died.
Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
15 And Mahalalel lived sixty and five years, and begot Jared.
Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
16 And Mahalalel lived after he begot Jared eight hundred and thirty years, and begot sons and daughters.
Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
17 And all the days of Mahalalel were eight hundred ninety and five years; and he died.
Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
18 And Jared lived a hundred sixty and two years, and begot Enoch.
Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
19 And Jared lived after he begot Enoch eight hundred years, and begot sons and daughters.
Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
20 And all the days of Jared were nine hundred sixty and two years; and he died.
Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
21 And Enoch lived sixty and five years, and begot Methuselah.
Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
22 And Enoch walked with God after he begot Methuselah three hundred years, and begot sons and daughters.
Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
23 And all the days of Enoch were three hundred sixty and five years.
Zaka zonse za Enoki zinali 365.
24 And Enoch walked with God, and he was not; for God took him.
Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
25 And Methuselah lived a hundred eighty and seven years, and begot Lamech.
Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
26 And Methuselah lived after he begot Lamech seven hundred eighty and two years, and begot sons and daughters.
Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
27 And all the days of Methuselah were nine hundred sixty and nine years; and he died.
Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
28 And Lamech lived a hundred eighty and two years, and begot a son.
Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
29 And he called his name Noah, saying: 'This same shall comfort us in our work and in the toil of our hands, which cometh from the ground which the LORD hath cursed.'
Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
30 And Lamech lived after he begot Noah five hundred ninety and five years, and begot sons and daughters.
Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
31 And all the days of Lamech were seven hundred seventy and seven years; and he died.
Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
32 And Noah was five hundred years old; and Noah begot Shem, Ham, and Japheth.
Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.

< Genesis 5 >