< Genesis 31 >

1 And he heard the words of Laban's sons, saying: 'Jacob hath taken away all that was our father's; and of that which was our father's hath he gotten all this wealth.'
Yakobo anamva zimene ana aamuna a Labani ankanena kuti, “Yakobo watenga chilichonse cha abambo athu ndipo wapeza chuma chonsechi pogwiritsa ntchito chuma cha abambo athu.”
2 And Jacob beheld the countenance of Laban, and, behold, it was not toward him as beforetime.
Choncho Yakobo anaona kuti Labani sankamuonetsanso nkhope yabwino monga kale.
3 And the LORD said unto Jacob: 'Return unto the land of thy fathers, and to thy kindred; and I will be with thee.'
Pamenepo Yehova anati kwa Yakobo, “Bwerera ku dziko la makolo ako ndi kwa abale ako, ndipo Ine ndidzakhala nawe.”
4 And Jacob sent and called Rachel and Leah to the field unto his flock,
Choncho Yakobo anatumiza mawu kukayitana Rakele ndi Leya kuti abwere ku busa kumene ankaweta ziweto zake.
5 and said unto them: 'I see your father's countenance, that it is not toward me as beforetime; but the God of my father hath been with me.
Iye anawawuza kuti, “Abambo anu sakundionetsanso nkhope yabwino monga kale, koma Mulungu wa makolo anga wakhala ali nane.
6 And ye know that with all my power I have served your father.
Inu mukudziwa kuti ndagwirira ntchito abambo anu ndi mphamvu zanga zonse,
7 And your father hath mocked me, and changed my wages ten times; but God suffered him not to hurt me.
chonsecho abambo anu akhala akundinyenga posintha malipiro anga kakhumi konse. Komabe Mulungu sanalole kuti andichitire choyipa
8 If he said thus: The speckled shall be thy wages; then all the flock bore speckled; and if he said thus: The streaked shall be thy wages; then bore all the flock streaked.
Pamene abambo anu anati, ‘Zamawangamawanga zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana amawangamawanga; ndipo pamene anati, ‘Zamichocholozi zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana a michocholozi.
9 Thus God hath taken away the cattle of your father, and given them to me.
Motero Mulungu walanda abambo anu ziweto zawo ndi kundipatsa.
10 And it came to pass at the time that the flock conceived, that I lifted up mine eyes, and saw in a dream, and, behold, the he-goats which leaped upon the flock were streaked, speckled, and grizzled.
“Pa nthawi imene ziweto zimatenga mawere ndinalota maloto, ndipo ndinaona kuti atonde onse amene ankakwerawo anali amichocholozi, amawangamawanga kapena amathothomathotho
11 And the angel of God said unto me in the dream: Jacob; and I said: Here am I.
Kutulo komweko, mngelo wa Mulungu anati, ‘Yakobo.’ Ine ndinayankha, ‘Ee, Ambuye.’
12 And he said: Lift up now thine eyes, and see, all the he-goats which leap upon the flock are streaked, speckled, and grizzled; for I have seen all that Laban doeth unto thee.
Ndipo iye anati, ‘Tayangʼana ndipo taona kuti atonde onse okwerana ndi ziweto ali amichocholozi, amawangamawanga kapena a mathothomathotho, popeza ndaona zonse zimene Labani wakhala akukuchitira.
13 I am the God of Beth-el, where thou didst anoint a pillar, where thou didst vow a vow unto Me. Now arise, get thee out from this land, and return unto the land of thy nativity.'
Ine ndine Mulungu amene ndinadza kwa iwe pa Beteli paja. Beteli ndi kumalo kuja kumene unayimika mwala ndi kuwudzoza mafuta, komanso kulumbira kwa Ine. Tsopano choka mʼdziko lino msanga ndi kubwerera ku dziko la kwanu.’”
14 And Rachel and Leah answered and said unto him: 'Is there yet any portion or inheritance for us in our father's house?
Pamenepo Rakele ndi Leya anayankha, “Kodi ngati ife tilinso ndi gawo ngati cholowa pa chuma cha abambo athu?
15 Are we not accounted by him strangers? for he hath sold us, and hath also quite devoured our price.
Kodi abambo athu samationa ife ngati alendo? Iwo anatigulitsa ndi kuwononga ndalama zonse anazipeza pa ifezo.
16 For all the riches which God hath taken away from our father, that is ours and our children's. Now then, whatsoever God hath said unto thee, do.'
Chuma chonse chimene Mulungu walanda abambo athu, ndi chathu ndi ana athu. Tsono inu chitani zimene Mulungu wakuwuzani.”
17 Then Jacob rose up, and set his sons and his wives upon the camels;
Pamenepo Yakobo anakonzeka nakweza ana ake ndi akazi ake pa ngamira,
18 and he carried away all his cattle, and all his substance which he had gathered, the cattle of his getting, which he had gathered in Paddan-aram, to go to Isaac his father unto the land of Canaan.
anakusa ziweto zake zonse patsogolo natenga katundu wake yense amene anamupeza ku Padanaramu, ndipo ananyamuka kupita ku Kanaani, ku dziko la abambo ake, Isake.
19 Now Laban was gone to shear his sheep. And Rachel stole the teraphim that were her father's.
Labani atachoka pa khomo kupita kukameta nkhosa, mʼmbuyomu Rakele anaba timafano ta milungu ta abambo ake.
20 And Jacob outwitted Laban the Aramean, in that he told him not that he fled.
Komanso nthawi iyi nʼkuti Yakobo atamunamiza Labani Mwaramu posamuwuza zoona kuti afuna kuthawa.
21 So he fled with all that he had; and he rose up, and passed over the River, and set his face toward the mountain of Gilead.
Choncho anathawa ndi zonse anali nazo. Ananyamuka nawoloka mtsinje wa Yufurate kupita cha ku Giliyadi, dziko la mapiri.
22 And it was told Laban on the third day that Jacob was fled.
Patapita masiku atatu, Labani anawuzidwa kuti Yakobo wathawa.
23 And he took his brethren with him, and pursued after him seven days' journey; and he overtook him in the mountain of Gilead.
Pomwepo anatengana ndi abale ake namulondola Yakobo kwa masiku asanu ndi awiri ndipo anakamupezera ku Giliyadi, dziko la mapiri.
24 And God came to Laban the Aramean in a dream of the night, and said unto him: 'Take heed to thyself that thou speak not to Jacob either good or bad.'
Koma Mulungu anabwera kwa Labani, Mwaramu kutulo usiku nati kwa iye, “Samala kuti usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.”
25 And Laban came up with Jacob. Now Jacob had pitched his tent in the mountain; and Laban with his brethren pitched in the mountain of Gilead.
Pamene Labani amamupeza Yakobo, nʼkuti Yakobo atamanga matenti ake ku mapiri a dziko la Giliyadi. Nayenso Labani ndi abale ake anamanga matenti awo komweko.
26 And Laban said to Jacob: 'What hast thou done, that thou hast outwitted me, and carried away my daughters as though captives of the sword?
Tsono Labani anati kwa Yakobo, “Kodi ndakuchita chiyani kuti iwe undinamize ndi kutenga ana anga ngati anthu ogwidwa ku nkhondo?
27 Wherefore didst thou flee secretly, and outwit me; and didst not tell me, that I might have sent thee away with mirth and with songs, with tabret and with harp;
Chifukwa chiyani unandinamiza ndi kuthawa mozemba wosandiwuza? Ukanandiwuza, bwezi titatsanzikana mwa chisangalalo ndi kuyimba nyimbo ndi zisekese ndi azeze.
28 and didst not suffer me to kiss my sons and my daughters? now hast thou done foolishly.
Sunandilole kuti ndingopsompsona adzukulu anga ndi ana anga aakazi motsanzikana nawo. Unachita zopusa.
29 It is in the power of my hand to do you hurt; but the God of your father spoke unto me yesternight, saying: Take heed to thyself that thou speak not to Jacob either good or bad.
Ndili nayo mphamvu yakukuchita choyipa; koma usiku wapitawu, Mulungu wa abambo ako wandiwuza ine kuti, ‘Usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.’
30 And now that thou art surely gone, because thou sore longest after thy father's house, wherefore hast thou stolen my gods?'
Ndikudziwa kuti unachoka chifukwa unapukwa kufuna kubwerera kwanu kwa abambo ako. Koma nʼchifukwa chiyani unaba milungu yanga?”
31 And Jacob answered and said to Laban: 'Because I was afraid; for I said: Lest thou shouldest take thy daughters from me by force.
Yakobo anayankha Labani kuti, “Ine ndinkaopa chifukwa ndinkaganiza kuti mukhoza kundilanda anawa.
32 With whomsoever thou findest thy gods, he shall not live; before our brethren discern thou what is thine with me, and take it to thee.' — For Jacob knew not that Rachel had stolen them. —
Koma mukapeza wina aliyense ndi milungu yanu, ameneyo sakhala ndi moyo. Anthu onse akupenya, lozani chilichonse chanu chimene chili ndi ine, ndipo ngati muchipeze tengani. Koma Yakobo sankadziwa kuti Rakele anabadi milunguyo.”
33 And Laban went into Jacob's tent, and into Leah's tent, and into the tent of the two maid-servants; but he found them not. And he went out of Leah's tent, and entered into Rachel's tent.
Choncho Labani analowadi mu tenti ya Yakobo, ya Leya ndi mʼmatenti a adzakazi awiri aja, koma sanapeze kalikonse. Atatuluka mu tenti ya Leya, analowa ya Rakele.
34 Now Rachel had taken the teraphim, and put them in the saddle of the camel, and sat upon them. And Laban felt about all the tent, but found them not.
Koma Rakele anatengadi milungu ija ndi kuyiika mʼkati mwa chokhalira cha pa ngamira, iye nʼkukhalapo. Choncho Labani anafunafuna mu tenti monse koma wosapeza kanthu.
35 And she said to her father: 'Let not my lord be angry that I cannot rise up before thee; for the manner of women is upon me.' And he searched, but found not the teraphim.
Rakele anati kwa abambo ake, “Pepanitu musandikwiyire mbuye wanga chifukwa choti sinditha kuyimirira pamaso panu chifukwa ndili kumwezi.” Choncho Labani anafunafuna koma sanayipeze milungu ija.
36 And Jacob was wroth, and strove with Laban. And Jacob answered and said to Laban: 'What is my trespass? what is my sin, that thou hast hotly pursued after me?
Yakobo anapsa mtima nafunsa Labani mwaukali kuti, “Kodi ndalakwa chiyani? Ndi tchimo lanji limene ndachita kuti muchite kundisaka chonchi?
37 Whereas thou hast felt about all my stuff, what hast thou found of all thy household stuff? Set it here before my brethren and thy brethren, that they may judge betwixt us two.
Chifukwa chiyani mwafunyulula katundu wanga? Ndipo mwapeza chiyani cha inu pamenepa? Chimene mwapezapo chiyikeni poyera pamaso pa abale anu ndi anga kuti atiweruze.
38 These twenty years have I been with thee; thy ewes and thy she-goats have not cast their young, and the rams of thy flocks have I not eaten.
“Ndakhala nanu kwa zaka makumi awiri tsopano ndipo nkhosa ndi mbuzi zanu sizinapoloze, kapena ine kudyapo nkhosa za mʼkhola mwanu.
39 That which was torn of beasts I brought not unto thee; I bore the loss of it; of my hand didst thou require it, whether stolen by day or stolen by night.
Chiweto chikakhadzulidwa ndi chirombo, sindinkabwera nacho kwa inu. Ineyo ndinkalipira. Inuyo munkandilipiritsa kalikonse kobedwa masana kapena usiku.
40 Thus I was: in the day the drought consumed me, and the frost by night; and my sleep fled from mine eyes.
Moyo wanga unali wotere: Dzuwa limanditentha masana ndipo usiku ndimazunzika ndi kuzizira. Tulo sindimalipeza konse.
41 These twenty years have I been in thy house: I served thee fourteen years for thy two daughters, and six years for thy flock; and thou hast changed my wages ten times.
Zinthu zinali chonchi kwa zaka makumi awiri zimene ndinali mʼnyumba mwanu. Ndinakugwirirani ntchito kwa zaka khumi ndi zinayi chifukwa cha ana anu aakazi awiri ndipo zaka zina zisanu ndi chimodzi chifukwa cha ziweto zanu, ndipo munandisinthira malipiro kakhumi konse.
42 Except the God of my father, the God of Abraham, and the Fear of Isaac, had been on my side, surely now hadst thou sent me away empty. God hath seen mine affliction and the labour of my hands, and gave judgment yesternight.'
Akanapanda kukhala nane Mulungu wa abambo anga, Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu amene Isake ankamuopa, mosakayika inu mukanandichotsa chimanjamanja. Koma Mulungu waona zovuta zanga ndi kulimbikira ntchito kwanga, ndipo usiku wapitawu anakudzudzulani.”
43 And Laban answered and said unto Jacob: 'The daughters are my daughters, and the children are my children, and the flocks are my flocks, and all that thou seest is mine; and what can I do this day for these my daughters, or for their children whom they have borne?
Labani anayankha Yakobo nati, “Ana aakaziwa ndi anga, ana awo ndi anganso. Ziwetozi ndi zanga. Chilichonse ukuona apa ndi changa. Koma tsopano ndingachite chiyani ndi ana anga aakaziwa kapena ndi ana awo?
44 And now come, let us make a covenant, I and thou; and let it be for a witness between me and thee.'
Tsono, tiye tichite pangano pakati pa iwe ndi ine, ndipo likhale mboni pakati pathu.”
45 And Jacob took a stone, and set it up for a pillar.
Choncho Yakobo anayimiritsa mwala ngati chipilala.
46 And Jacob said unto his brethren: 'Gather stones'; and they took stones, and made a heap. And they did eat there by the heap.
Nati kwa abale ake, “Tutani miyala ina.” Choncho anawunjika miyalayo, ndipo anadya chakudya atakhala pa mbali pa muluwo.
47 And Laban called it Jegar-sahadutha; but Jacob called it Galeed.
Labani anawutcha muluwo Yegara-sahaduta, ndipo Yakobo anawutcha Galeeda.
48 And Laban said: 'This heap is witness between me and thee this day.' Therefore was the name of it called Galeed;
Labani anati, “Mulu uwu ndi mboni pakati pa inu ndi ine lero.” Ndi chifukwa chake unatchedwa Galeeda.
49 and Mizpah, for he said: 'The LORD watch between me and thee, when we are absent one from another.
Unatchedwanso Mizipa, chifukwa iye anati, “Yehova aonetsetsa kuti palibe mmodzi mwa ife adzaswe panganoli ngakhale titatalikirana.
50 If thou shalt afflict my daughters, and if thou shalt take wives beside my daughters, no man being with us; see, God is witness betwixt me and thee.'
Ngati ukazunza ana anga kapena kukwatira akazi enanso, ngakhale kuti palibe wina amene ali nafe pano, koma kumbukira kuti Mulungu ndiye mboni pakati pathu.”
51 And Laban said to Jacob: 'Behold this heap, and behold the pillar, which I have set up betwixt me and thee.
Labani anatinso kwa Yakobo, “Taona pano pali miyala ndi chipilala chimene ndayimika pakati pa iwe ndi ine.
52 This heap be witness, and the pillar be witness, that I will not pass over this heap to thee, and that thou shalt not pass over this heap and this pillar unto me, for harm.
Mulu wa miyala uwu ndi chipilalachi ndi mboni. Ine sindidzadutsa mulu wa miyalawu kudzalimbana ndi iwe. Iwenso usadzadutse mulu wa miyalawu kudzalimbana nane.
53 The God of Abraham, and the God of Nahor, the God of their father, judge betwixt us.' And Jacob swore by the Fear of his father Isaac.
Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu wa Nahori ndiye adzatiweruze.” Choncho Yakobo analumbira mʼdzina la Mulungu amene Isake, abambo ake ankamuopa.
54 And Jacob offered a sacrifice in the mountain, and called his brethren to eat bread; and they did eat bread, and tarried all night in the mountain.
Yakobo anapereka nsembe pa phiri paja, ndipo anayitana abale ake kuti adzadye chakudya. Atadya chakudya anagona pa phiri pomwepo.
55 And early in the morning Laban rose up, and kissed his sons and his daughters, and blessed them. And Laban departed, and returned unto his place.
Mmamawa wake, Labani anapsompsona zidzukulu zake ndi ana ake nawadalitsa. Kenaka ananyamuka kubwerera ku mudzi.

< Genesis 31 >