< Job 17 >

1 My breath is corrupt: my dayes are cut off, and the graue is readie for me.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 There are none but mockers with mee, and mine eye continueth in their bitternesse.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 Lay downe nowe and put me in suretie for thee: who is hee, that will touch mine hand?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 For thou hast hid their heart from vnderstanding: therefore shalt thou not set them vp on hie.
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 For the eyes of his children shall faile, that speaketh flattery to his friends.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 Hee hath also made mee a byword of the people, and I am as a Tabret before them.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 Mine eye therefore is dimme for griefe, and all my strength is like a shadowe.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 The righteous shalbe astonied at this, and the innocent shalbe moued against ye hypocrite.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 But the righteous wil holde his way, and he whose hands are pure, shall increase his strength.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 All you therefore turne you, and come nowe, and I shall not finde one wise among you.
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 My dayes are past, mine enterprises are broken, and the thoughts of mine heart
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 Haue changed the nyght for the day, and the light that approched, for darkenesse.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 Though I hope, yet the graue shall bee mine house, and I shall make my bed in the darke. (Sheol h7585)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
14 I shall say to corruption, Thou art my father, and to the worme, Thou art my mother and my sister.
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 Where is then now mine hope? or who shall consider the thing, that I hoped for?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 They shall goe downe into the bottome of the pit: surely it shall lye together in the dust. (Sheol h7585)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)

< Job 17 >