< Psalms 79 >

1 A psalm of Asaph. God, heathen nations have invaded your land. They have defiled your holy Temple. They have turned Jerusalem into heaps of rubble.
Salimo la Asafu. Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu; ayipitsa Nyumba yanu yoyera, asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.
2 They have given the dead bodies of your servants as food to the birds of the air, the flesh of your faithful people to the beasts of the earth.
Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya, matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.
3 They have poured out the blood of Jerusalem's people like water all through the city; no one remains to bury the dead.
Akhetsa magazi monga madzi kuzungulira Yerusalemu yense, ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.
4 We have been made a mockery before our neighbors, ridiculed and laughed at by those around us.
Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu, choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.
5 How long, Lord? Will you be angry with us forever? Will your jealousy always burn like fire?
Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya? Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?
6 Pour out your anger on the heathen nations that don't know you, and on those kingdoms that don't worship you!
Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina amene sakudziwani Inu, pa maufumu amene sayitana pa dzina lanu;
7 For they have destroyed the descendants of Jacob, and turned our country into a wasteland.
pakuti iwo ameza Yakobo ndi kuwononga dziko lawo.
8 Don't hold the sins of our forefathers against us! Come to us quickly for we desperately need your compassion.
Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe, pakuti tili ndi chosowa chachikulu.
9 Help us, God of our salvation, because of your wonderful character! Save us and forgive us our sins because that's the kind of person you are!
Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu; tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu chifukwa cha dzina lanu.
10 Why should the heathen nations be able to say, “Where is their God?” May they experience your punishment for shedding the blood of your servants, and may we see it.
Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti, “Ali kuti Mulungu wawo?” Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.
11 Listen to the groans of the prisoners; with your great power save those condemned to die.
Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu; ndi mphamvu ya dzanja lanu muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.
12 Pay each of these neighbors back seven times for the scorn and ridicule they directed against you, Lord.
Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.
13 Then we your people, the flock of your pasture, will praise you forever. We will thank you for all generations to come.
Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu, tidzakutamandani kwamuyaya, kuchokera mʼbado ndi mʼbado tidzafotokoza za matamando anu.

< Psalms 79 >