< Proverbs 1 >
1 The proverbs of Solomon, son of David, king of Israel.
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 They are for achieving wisdom and instruction, and to recognize sayings that bring insight.
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 They provide education in what makes sense, living right, judging correctly, and acting fairly.
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 They give discernment to the immature, knowledge and discretion to the young.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Wise people will listen and gain in learning, and those who have good judgment will gain skills in guidance,
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 understanding the proverbs and puzzles, the sayings and questions of the wise.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 Honoring the Lord is where true knowledge begins, but fools treat wisdom and good advice with contempt.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 My son, pay attention to your father's instruction, and don't reject your mother's teaching.
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 They are a wreath of grace to decorate your head; they are pendants for your neck.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 My son, if evil people try to tempt you, don't give into them.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 They may tell you, “Come with us. Let's go and hide, ready to kill someone. Let's ambush someone for fun!
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Let's bury them alive; let's put them in the grave while they're still healthy! (Sheol )
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
13 We'll take from them all kinds of valuable things and fill our homes with the stuff we steal!
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Come and join us and we'll all share what we get!”
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 My son, don't follow their ways. Don't go in that direction with them.
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 For they rush to do evil; they hurry to commit violence and murder.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 There's no point in trying to lure birds into a net when they can see it.
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 However, these evil people hide ready to kill others, but they themselves are the victims. They're only ambushing themselves!
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 This is what happens to you if you try to become rich through crime—it kills you!
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Wisdom calls out in the streets; she shouts aloud in the squares.
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 She cries out at busy corners; she explains her message at the town gates:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 “How long will you stupid people love stupidity? How long will scornful people enjoy their mocking? How long will fools hate knowledge?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Pay attention to my warnings, and I'll pour out my deepest thoughts to you—I'll explain what I know to you.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 For I have called you, but you refused to listen; I reached out my hand to you, but you didn't care.
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 You ignored everything I said; you wouldn't accept any of my warnings.
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 So I'll laugh at you when you're in trouble; I'll mock you when you're in a panic.
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 When panic rains down on you like a storm, when trouble hits you like a whirlwind, when sorrow and pain come on you,
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 then you'll call out to me for help, but I won't answer; you'll search hard for me, but won't find me.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Why?—because they hated knowledge, and they didn't choose to respect the Lord.
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 They're not willing to accept my advice; they despise all my warnings.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 So they'll have to eat the fruit of their own choices, bloated by their own devious schemes.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Stupid people are killed by their rebellion; foolish people are destroyed by their lack of concern.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 But everyone who listens to me will be kept safe, and will live without worrying about problems.”
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”