< Psalms 66 >

1 For the music director. A song. A psalm. Everyone on earth, shout for joy to God!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 Sing about his marvelous reputation; praise him for his goodness!
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 Tell God, “What you do is awesome! Your enemies are forced to bow before you because of your power.
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 Everyone on earth worships you, singing your praises—singing praises because of who you are.” (Selah)
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 Come and see what God has done! What he does for people is truly awesome!
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 He turned the Red Sea into dry land, and his people walked across through the waters. We celebrated there because of what he did.
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 He rules forever through his power. He keeps an eye on the nations, watching to make sure no rebels rise up in opposition. (Selah)
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 Let all people everywhere bless our God, and loudly sing praises to him.
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 He has kept us alive, and he has not let us fall.
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 God, you have tested us, refining us like silver.
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 You caught us in your net; you placed heavy burdens on our backs.
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 You let people ride roughshod over us; we suffered through fire and flooding, but you brought us to a safe place.
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 I will come to your Temple with burnt offerings; I will fulfill my promises to you,
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 the promises I made when I was in trouble.
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 I will sacrifice burnt offerings to you of fattened livestock—the smoke of the sacrifice of rams, offerings of bulls and goats. (Selah)
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 Come and listen, everyone who honors God, and I will tell you all he has done for me.
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 I called out to him, and praised him with my voice.
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 If my thinking had been sinful, the Lord would not have listened to me.
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 But God did hear me! He listened to what I had to say in my prayer!
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 Praise God, who did not disregard my prayer or take his trustworthy love from me.
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< Psalms 66 >