< Psalms 63 >
1 A psalm of David, when he was in the Judean desert. God, you are my God, I eagerly look for you. I am thirsty for you; all that I am longs for you in this dry, weary, waterless land.
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 I see you in the Temple; I watch your power and glory.
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 Your trustworthy love is better than life itself; I will praise you.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 I will thank you as long as I live; I lift up my hands as I celebrate your wonderful character.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 You satisfy me more than the richest food; I will praise you with joyful songs.
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 I think of you all night long as I lie on my bed meditating about you.
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 For you are the one who helps me; I sing happily from under your wings.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 I hold on to you; your strong arms lift me up.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 Those who are trying to destroy me will go down into the grave.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 They will be killed by the sword; they will become food for jackals.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 But the king will be happy for what God has done. All who follow God will praise him, but those who tell lies will be silenced.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.