< Ezekiel 12 >
1 And the word of the Lord came to me, saying:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 Son of man, thou dwellest in the midst of a provoking house: who have eyes to see, and see not: and ears to hear, and hear not: for they are a provoking house.
“Iwe mwana wa munthu, ukukhala pakati pa anthu owukira, iwowo maso openyera ali nawo, koma sakuona ndipo makutu omvera ali nawo, koma sakumva chifukwa choti ndi anthu owukira.
3 Thou, therefore, O son of man, prepare thee all necessaries for removing, and remove by day in their sight: and thou shalt remove out of thy place to another place in their sight, if so be they will regard it: for they are a provoking house.
“Choncho, iwe mwana wa munthu, longedza katundu wako wopita naye ku ukapolo. Unyamuke nthawi yamasana iwo akuona. Uchite ngati wanyamuka kuchoka kumene ukukhala kupita ku dziko lachilendo iwowo akuona. Mwina adzamvetsetsa, paja ndi anthu aupandu.
4 And thou shalt bring forth thy furniture as the furniture of one that is removing by day in their sight: and thou shalt go forth in the evening in their presence, as one goeth forth that removeth his dwelling.
Utulutse katundu wako wopita naye ku ukapolo nthawi ya masana iwo akuona. Ndipo nthawi ya madzulo, iwo akuona, uchoke monga ngati ukupita ku ukapolo.
5 Dig thee a way through the wall before their eyes: and thou shalt go forth through it.
Iwo akuona, ubowole pa khoma ndipo utulutsirepo katundu wako.
6 In their sight thou shalt be carried out upon men’s shoulders, thou shalt be carried out in the dark: thou shalt cover thy face, and shalt not see the ground: for I have set thee for a sign of things to come to the house of Israel.
Usenze katundu wako pa phewa iwo akuona, ndipo upite kunja ku mdima. Uphimbe nkhope yako kuti usaone pansi, pakuti ndakusandutsa iwe chizindikiro chochenjeza Aisraeli.”
7 I did therefore as he had commanded me: I brought forth my goods by day, as the goods of one that removeth: and in the evening I digged through the wall with my hand: and I went forth in the dark, and was carried on men’s shoulders in their sight.
Choncho ine ndinachita monga momwe anandilamulira. Nthawi yamasana ndinatulutsa zinthu zanga nditazimanga ngati ndikupita ku ukapolo. Ndipo nthawi yamadzulo ndinabowola khoma ndi manja anga. Pamene chisisira chinkayamba, ndinasenza katundu wanga pa phewa kutuluka naye iwo akuona.
8 And the word of the Lord came to me in the morning, saying:
Mmawa mwake Yehova anandiyankhula nati:
9 Son of man, hath not the house of Israel, the provoking house, said to thee: What art thou doing?
“Iwe mwana wa munthu, kodi anthu aupandu a Israeli sanakufunse kuti ukuchita chiyani?
10 Say to them: Thus saith the Lord God: This burden concerneth my prince that is in Jerusalem, and all the house of Israel, that are among them.
“Uwawuze kuti, ‘zimene ndikunena Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndi izi: Uthengawu ndi wonena za kalonga wa ku Yerusalemu pamodzi ndi banja lonse la Israeli amene akukhala kumeneko.’
11 Say: I am a sign of things to come to you: as I have done, so shall it be done to them: they shall be removed from their dwellings, and go into captivity.
Uwawuze kuti, ‘Ndiwe chizindikiro chowachenjeza.’ “Zidzakuchitikirani monga momwe zakuchitikira iwemu. Iwo adzatengedwa kupita ku ukapolo.”
12 And the prince that is in the midst of them, shall be carried on shoulders, he shall go forth in the dark: they shall dig through the wall to bring him out: his face shall be covered, that he may not see the ground with his eyes.
“Kalonga wawo adzatenga katundu wake nʼchisisira nʼkunyamuka. Adzatulukira pa bowo limene anthu anabowola pa khoma. Adzaphimba nkhope yake kuti asaone kumene akupita.
13 And I will spread my net over him, and he shall be taken in my net: and I will bring him into Babylon, into the land of the Chaldeans, and he shall not see it, and there he shall die.
Ndidzayala ukonde wanga pa iye ndi kumukola mu msampha wanga. Ndidzabwera naye ku Babuloni, dziko la Akaldeya, koma sadzaliona dzikolo, ndipo adzafera kumeneko.
14 And all that are about him, his guards, and his troops I will scatter into every wind: and I will draw out the sword after them.
Ine ndidzabalalitsa kumbali zonse zinayi onse okhala naye pafupi, ndiwo omuthandiza ake pamodzi ndi ankhondo ake. Ndidzawalondola ndi lupanga losolola.
15 And they shall know that I am the Lord, when I shall have dispersed them among the nations, and scattered them in the countries.
“Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsira ku mayiko ena.
16 And I will leave a few men of them from the sword, and from the famine, and from the pestilence: that they may declare all their wicked deeds among the nations whither they shall go: and they shall know that I am the Lord.
Koma ndidzasiyako ena pangʼono amene adzapulumuke ku lupanga, njala ndi mliri, kuti akafotokoze ntchito zawo zonse zonyansa pakati pa anthu achilendo kumene akupitako. Pamenepo adzadziwa kuti ndine Yehova.”
17 And the word of the Lord came to me, saying:
Pambuyo pake Yehova anandiyankhulanso nati,
18 Son of man, eat thy bread in trouble: and drink thy water in hurry and sorrow.
“Iwe mwana wa munthu, uzinjenjemera ukamadya chakudya chako, ndipo uzinthunthumira ndi mantha ukamamwa madzi ako.
19 And say to the people of the land: Thus saith the Lord God to them that dwell in Jerusalem in the land of Israel: They shall eat their bread in care, and drink their water in desolation: that the land may become desolate from the multitude that is therein, for the iniquity of all that dwell therein.
Uwawuze anthu a mʼdzikomo kuti izi ndi zimene Ambuye Wamphamvuzonse akunena za anthu okhala mu Yerusalemu ndi dziko la Israeli: Iwo adzadya chakudya chawo ndi mantha ndi kumwa madzi awo ndi nkhawa. Zonse za mʼdziko lawo zidzalandidwa chifukwa cha ziwawa za anthu onse okhala mʼmenemo.
20 And the cities that are now inhabited shall be laid waste, and the land shall be desolate: and you shall know that I am the Lord.
Mizinda imene ili ndi anthu idzasakazika ndipo dziko lidzasanduka chipululu. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
21 And the word of the Lord came to me, saying:
Yehova anayankhulanso nane kuti,
22 Son of man, what is this proverb that you have in the land of Israel? saying: The days shall be prolonged, and every vision shall fail.
“Iwe mwana wa munthu, kodi mwambi umene ukunenedwa mu Israeli ndi wotani: ‘Masiku akupita koma masomphenya onse sakukwaniritsidwa?’
23 Say to them therefore: Thus saith the Lord God: I will make this proverb to cease, neither shall it be any more a common saying in Israel: and tell them that the days are at hand, and the effect of every vision.
Choncho uwawuze anthuwo kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndidzawuthetsa mwambi umenewu ndipo sadzawunenanso mu Israeli.’ Uwawuze kuti, ‘masiku ayandikira oti zonse zimene ndinanena mʼmasomphenya zichitikedi.
24 For there shall be no more any vain visions, nor doubtful divination in the midst of the children of Israel.
Pakuti masiku amenewo sikudzakhalanso masomphenya abodza kapena kuwombeza kwa chinyengo pakati pa anthu a Israeli.
25 For I the Lord will speak: and what word soever I shall speak, it shall come to pass, and shall not be prolonged any more: but in your days, ye provoking house, I will speak the word, and will do it, saith the Lord God.
Koma Ine Ambuye ndidzayankhula chimene ndikufuna, ndipo chidzachitikadi, osachedwa ayi. Pakuti mʼmasiku anu omwe ano, inu anthu opanduka, ndidzakwaniritsa chilichonse chimene ndidzanena. Ndikutero Ine Yehova.’”
26 And the word of the Lord came to me, saying:
Yehova anandiyankhula nati:
27 Son of man, behold the house of Israel, they that say: The vision that this man seeth, is for many days to come: and this men prophesieth of times afar off.
“Iwe mwana wa munthu, Aisraeli akunena kuti, ‘masomphenya amene ukuona sadzachitika kwa zaka zambiri. Iwo akuti ukulosa za zinthu zimene zidzachitika ku tsogolo kwambiri.’
28 Therefore say to them: Thus saith the Lord God: Not one word of mine shall be prolonged any more: the word that I shall speak shall be accomplished, saith the Lord God.
“Choncho uwawuze kuti, ‘zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena ndi izi: Zonena zanga sizidzachedwanso; chilichonse chimene ndikunena chidzachitikadi. Ndikutero Ine Yehova.’”