< Ezekiel 11 >

1 And the spirit lifted me up, and brought me into the east gate of the house of the Lord, which looketh towards the rising of the sun: and behold in the entry of the gate five and twenty men: and I saw in the midst of them Jezonias the son of Azur, and Pheltias the son of Banaias, princes of the people.
Pamenepo Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kubwera nane ku chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Kumeneko pa khomo la chipata panali anthu 25, ndipo ndinaona pakati pawo atsogoleri awa: Yaazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya.
2 And he said to me: Son of man, these are the men that study iniquity, and frame a wicked counsel in this city,
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi anthu amene akukonza zoyipa ndi kupereka malangizo oyipa mu mzindamo.
3 Saying: Were not houses lately built? This city is the caldron, and we the flesh.
Iwo amawuza anthu kuti, ‘Nthawi sinafike yoti timange Nyumba? Mzindawu uli ngati mʼphika umene uli pa moto ndipo ife tili ngati nyama mu mʼphikamo.
4 Therefore prophesy against them, prophesy, thou son of man.
Choncho iwe mwana wa munthu, unenere mowadzudzula. Nenera ndithu.’”
5 And the spirit of the Lord fell upon me, and said to me: Speak: Thus saith the Lord: Thus have you spoken, O house of Israel, for I know the thoughts of your heart.
Ndipo Mzimu wa Yehova unandigwera ndipo unandiwuza kuti, “Unene kuti zimene akunena Yehova ndi izi. Iye akuti. ‘Izi ndi zimene mukunena, Inu Aisraeli, koma Ine ndikudziwa zimene zili mu mtima mwanu.’
6 You have killed a great many in this city, and you have filled the streets thereof with the slain.
Mwapha anthu ambiri mu mzinda muno ndipo mwadzaza misewu yake ndi mitembo.
7 Therefore thus saith the Lord God: Your slain, whom you have laid in the midst thereof, they are the flesh, and this is the caldron: and I will bring you forth out of the midst thereof.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mitembo imene mwayiponya mʼmisewuyo ndiyo nyama ndipo mzinda uno ndiwo mʼphika, koma Ine ndidzakuthamangitsanimo.
8 You have feared the sword, and I will bring the sword upon you, saith the Lord God.
Inu mumaopa lupanga, koma lupangalo ndi limene ndidzakubweretsereni, akutero Ambuye.
9 And I will cast you out of the midst thereof, and I will deliver you into the hand of the enemies, and I will execute judgments upon you.
Ine ndidzakuthamangitsani mu mzinda ndipo ndidzakuperekani mʼdzanja la alendo kuti akulangeni.
10 You shall fall by the sword: I will judge you in the borders of Israel, and you shall know that I am the Lord.
Mudzaphedwa ndi lupanga ndipo ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
11 This shall not be as a caldron to you, and you shall not be as flesh in the midst thereof: I will judge you in the borders of Israel.
Mzinda uno sudzakhala ngati mʼphika wokutetezani ndipo simudzakhalanso ngati nyama ya mʼmenemo. Ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli.
12 And you shall know that I am the Lord: because you have not walked in my commandments, and have not done my judgments, but you have done according to the judgments of the nations that; are round about you.
Ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. Inu simunatsatire malangizo anga kapena kusunga malamulo anga koma mwakhala mukutsata zochita za mitundu ina ya anthu imene yakuzungulirani.’”
13 And it came to pass, when I prophesied, that Pheltias the son of Banaias died: and I fell down upon my face, and cried with a loud voice: and said: Alas, alas, alas, O Lord God: wilt thou make an end of all the remnant of Israel?
Tsono pamene ndinkanenera, Pelatiya mwana wa Benaya anafa. Pomwepo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba ndipo ndinafuwula ndi mawu aakulu kuti “Mayo, Ambuye Yehova! Kodi mudzawatheratu Aisraeli onse otsala?”
14 And the word of the Lord came to me, saying:
Yehova anayankhula nane kuti,
15 Son of man, thy brethren, thy brethren, thy kinsmen, and all the house of Israel, all they to whom the inhabitants of Jerusalem have said: Get ye far from the Lord, the land is given in possession to us.
“Anthu okhala ku Yerusalemu akuwanena abale ako, anthu a ku ukapolo, onse a banja la Israeli, kuti, ‘Anthu onse amene anatengedwa ukapolo ali kutali ndi Yehova. Dziko lanu Yehova anatipatsa kuti likhale lathulathu.’”
16 Therefore thus saith the Lord God: Because I have removed them far off among the Gentiles, and because I have scattered them among the countries: I will be to them a little sanctuary in the countries whither they are come.
“Nʼchifukwa chake nena kwa anzako a ku ukapolo kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Ine ndinawatumiza kutali pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinawabalalitsa ku mayiko ambiri. Komabe ndakhala ndikuwasunga ku mayiko kumene anapitako!’
17 Therefore speak to them: Thus saith the Lord God: I will gather you from among the peoples, and assemble you out of the countries wherein you are scattered, and I will give you the land of Israel.
“Nʼchifukwa chake uwawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kuti, Ndidzawasonkhanitsa kuchokera kwa anthu a mitundu inayo ndi kuwasonkhanitsira pamodzi kuchokera ku mayiko kumene ndinawabalalitsirako. Pambuyo pake ndidzawapatsa dziko la Israeli.
18 And they shall go in thither, and shall take away all the scandals, and all the abominations thereof from thence.
“Akadzalowa mʼdzikomo adzachotsa mafano awo onse oyipa ndi onyansa.
19 And I will give them one heart, and will put a new spirit in their bowels: and I will take away the stony heart out of their flesh, and will give them a heart of flesh:
Ndidzawapatsa mtima watsopano ndipo ndidzayika mzimu watsopano mwa iwo. Ndidzachotsa mtima wowuma ngati mwala mwa iwo, ndipo ndidzawapatsa mtima wofewa ngati mnofu.
20 That they may walk in my commandments, and keep my judgments, and do them: and that they may be my people, and I may be their God.
Motero adzatsata malamulo anga ndipo adzasunga mosamala malamulo anga. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
21 But as for them whose heart walketh after their scandals and abominations, I will lay their way upon their head, saith the Lord God.
Koma kunena za amene akupembedza mafano oyipa ndi onyansa, ndidzawalanga chifukwa cha zimene achita. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
22 And the cherubims lifted up their wings, and the wheels with them: and the glory of the God of Israel was over them.
Tsono akerubi aja anatambasula mapiko awo kuyamba kuwuluka, mikombero ili mʼmbali mwawo. Ulemerero wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
23 And the glory of the Lord went up from the midst of the city, and stood over the mount that is on the east side of the city.
Ulemerero wa Yehova unakwera ndi kusiya mzindawo ndipo unakayima pa phiri cha kummawa kwake kwa mzindawo.
24 And the spirit lifted me up, and brought me into Chaldea, to them of the captivity, in vision, by the spirit of God: and the vision which I had seen was taken up from me.
Pambuyo pake Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kukandifikitsa. Zimenezi zinkachitika mʼmasomphenya monga mmene Mzimu wa Mulungu unkandionetsera. Kenaka masomphenya amene ndinkawaonawo anayamba kuzimirira.
25 And I spoke to them of the captivity all the words of the Lord, which he had shewn me.
Ndipo ndinafotokozera akapolowo zonse zimene Yehova anandionetsa.

< Ezekiel 11 >