< Josua 4 >
1 Da nu hele Folket havde tilendebragt Overgangen over Jordan, sagde HERREN til Josua:
Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa,
2 "Vælg eder tolv Mænd af Folket, een Mand af hver Stamme,
“Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse.
3 og byd dem: Tag eder tolv Sten her, midt i Jordan, hvor Præsterne stod stille, bring dem med over og stil dem på den Plads, hvor I holder Rast i Nat!"
Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’”
4 Så lod Josua de tolv Mænd kalde, som han havde til Rede af Israeliterne, een Mand af hver Stamme;
Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse,
5 og Josua sagde til dem: "Gå foran HERREN eders Guds Ark midt ud i Jordan, og tag så hver en Sten på Skulderen, svarende til Tallet på Israeliternes Stammer,
ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli,
6 for at det kan tjene til Tegn iblandt eder. Når eders Børn i Fremtiden spørger: Hvad Betydning har disse Sten for eder?
kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
7 så skal I sige til dem: De betyder, at Jordans Vand standsede foran HERRENs Pagts Ark; da den drog over Jordan, standsede Jordans Vand. Og disse Sten skal være Israeliterne et Mindetegn til evig Tid!"
Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’”
8 Da gjorde Israeliterne, som Josua bød, og tog tolv Sten midt i Jordan, som HERREN havde sagt til Josua, svarende til Tallet på Israeliternes Stammer, og de bragte dem med over til det Sted, hvor de holdt Rast, og stillede dem der.
Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko.
9 Og tolv Sten rejste Josua midt i Jordan på det Sted, hvor Præsterne, som bar Pagtens Ark, stod stille, og der står de den Dag i Dag.
Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.
10 Men Præsterne, som bar Arken, blev stående midt i Jordan, indtil alt, hvad HERREN havde pålagt Josua at sige til Folket, var udført, i Overensstemmelse med alt, hvad Moses havde pålagt Josua; og Folket gik skyndsomt over.
Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira.
11 Da hele Folket så havde tilendebragt Overgangen, gik HERRENs Ark og Præsterne over og stillede sig foran Folket.
Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova.
12 Og Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme drog væbnet over i Spidsen for Israeliterne, som Moses havde sagt til dem;
Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira.
13 henved 40000 Mand i Tal, rustede til Strid, drog de foran HERREN over til Jerikos Sletter til Hamp.
Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.
14 På den Dag gjorde HERREN Josua stor i hele Israels Øjne, og de frygtede ham alle hans Livs Dage, som de havde frygtet Moses.
Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.
15 Da sagde HERREN til Josua:
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa,
16 "Byd Præsterne, som bærer Vidnesbyrdets Ark, at stige op fra Jordan!"
“Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”
17 Og Josua bød Præsterne: "Stig op fra Jordan!"
Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.
18 Så steg Præsterne, som bar HERRENs Pagts Ark, op fra Jordan, og næppe havde deres Fødder betrådt det tørre Land, før Jordans Vand vendte tilbage til sit Leje og overalt gik over sine Bredder som før.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.
19 Og Folket steg op fra Jordan den tiende Dag i den første Måned og slog Lejr i Gilgal ved Østenden af Jerikolandet.
Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko.
20 Men de tolv Sten, som de havde taget op fra Jordan, rejste Josua i Gilgal,
Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija.
21 og han sagde til Israeliterne: "Når eders Børn i Fremtiden spørger deres Fædre: Hvad betyder disse Sten?
Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
22 så skal I fortælle eders Børn det og sige: På tør Bund gik Israel over Jordan derhenne;
Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’
23 thi HERREN eders Gud lod Jordans Vand tørre bort foran eder, indtil I var kommet over, ligesom HERREN eders Gud gjorde med det røde Hav, som han lod tørre bort foran os, indtil vi var kommet over,
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma.
24 for at alle Jordens Folk skal kende, at HERRENs Arm er stærk, at de må frygte HERREN eders Gud alle Dage."
Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”