< Job 3 >

1 Derefter oplod Job sin Mund og forbandede sin Dag,
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 og Job tog til Orde og sagde:
Ndipo Yobu anati:
3 Bort med den Dag, jeg fødtes, den Nat, der sagde: "Se, en Dreng!"
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 Denne Dag vorde Mørke, Gud deroppe spørge ej om den, over den stråle ej Lyset frem!
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 Mulm og Mørke løse den ind, Tåge lægge sig over den, Formørkelser skræmme den!
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 Mørket tage den Nat, den høre ej hjemme blandt Årets Dage, den komme ikke i Måneders Tal!
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 Ja, denne Nat vorde gold, der lyde ej Jubel i den!
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 De, der besværger Dage, forbande den, de, der har lært at hidse Livjatan";
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 dens Morgenstjerner formørkes, den bie forgæves på Lys, den skue ej Morgenrødens Øjenlåg,
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 fordi den ej lukked mig Moderlivets Døre og skjulte Kvide for mit Blik!
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 Hvi døde jeg ikke i Moders Liv eller udånded straks fra Moders Skød?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Hvorfor var der Knæ til at tage imod mig, hvorfor var der Bryster at die?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 Så havde jeg nu ligget og hvilet, så havde jeg slumret i Fred
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 blandt Konger og Jordens Styrere, der bygged sig Gravpaladser,
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 blandt Fyrster, rige på Guld, som fyldte deres Huse med Sølv.
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Eller var jeg dog som et nedgravet Foster. som Børn, der ikke fik Lyset at se!
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 Der larmer de gudløse ikke mer, der hviler de trætte ud,
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 alle de fangne har Ro, de hører ej Fogedens Røst;
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 små og store er lige der og Trællen fri for sin Herre.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 Hvi giver Gud de lidende Lys, de bittert sørgende Liv,
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 dem, som bier forgæves på Døden, graver derefter som efter Skatte,
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 som glæder sig til en Stenhøj, jubler, når de finder deres Grav
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 en Mand, hvis Vej er skjult, hvem Gud har stænget inde?
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 Thi Suk er blevet mit daglige Brød, mine Ve råb strømmer som Vand.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 Thi hvad jeg gruer for, rammer mig, hvad jeg bæver for, kommer over mig.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 Knap har jeg Fred, og knap har jeg Ro, knap har jeg Hvile, så kommer Uro!
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

< Job 3 >