< Job 2 >
1 Nu hændte det en Dag, at Guds Sønner kom og trådte frem for HERREN, og iblandt dem kom også Satan og trådte frem for ham.
Tsiku linanso pamene ana a Mulungu anabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anabwera nawo limodzi kudzadzionetsa pamaso pa Yehova.
2 HERREN spurgte Satan: "Hvor kommer du fra?" Satan svarede HERREN: "Jeg bar gennemvanket Jorden på Kryds og tværs."
Ndipo Yehova anati kwa Satana, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
3 HERREN spurgte da Satan: "Har du lagt Mærke til min Tjener Job? Der findes ingen som han på Jorden, så from og retsindig en Mand, som frygter Gud og viger fra det onde. Endnu holder han fast ved sin Fromhed, og uden Grund har du ægget mig til at ødelægge ham!"
Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa. Ndipo iye akanalibe wangwiro, ngakhale iwe unandiwumiriza kuti ndikulole kuti umuvutitse popanda chifukwa.”
4 Men Satan svarede HERREN: "Hud for Hud! En Mand giver alt, hvad han ejer, for sit Liv!
Satana anayankha kuti, “Iye ayesedwe mʼthupi mwake. Munthu angathe kupereka zonse ali nazo malingana iyeyo ali ndi moyo.
5 Men ræk engang din Hånd ud og rør ved hans Ben og Kød! Sandelig, han vil forbande dig lige op i dit Ansigt!"
Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kuwononga thupi lake, ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
6 Da sagde HERREN til Satan: "Se, han er i din Hånd; kun skal du skåne hans Liv!"
Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, iye ali mʼmanja mwako; koma moyo wake usawuchotse.”
7 Så gik Satan bort fra HERRENs Åsyn, og han slog Job med ondartet Bylder fra Fodsål til Isse,
Choncho Satana anachoka pamaso pa Yehova napita kukazunza Yobu ndi zilonda zaululu pa thupi lake lonse.
8 Og Job tog sig et Potteskår til at skrabe sig med, medens han sad i Askedyngen.
Pamenepo Yobu anatenga phale ndi kumadzikanda nalo atakhala pa dzala la phulusa.
9 Da sagde hans Hustru til ham: "Holder du endnu fast ved din Fromhed? Forband Gud og dø!"
Mkazi wake anati kwa iye, “Kodi ukuwumirirabe kukhala wangwiro? Tukwana Mulungu kuti ufe!”
10 Men han svarede hende: "Du taler som en Dåre! Skulde vi tage imod det gode fra Gud, men ikke imod det onde?" I alt dette syndede Job ikke med sine Læber.
Yobu anayankha kuti, “Ukuyankhula ngati mkazi wopusa. Kodi tidzalandira zokoma zokhazokha kwa Mulungu, osalandiranso zowawa?” Mu zonsezi, Yobu sanachimwe pa zimene anayankhula.
11 Da Jobs tre Venner hørte om al den Ulykke, der havde ramt ham, kom de hver fra sin Hjemstavn. Temaniten Elifaz, Sjuhiten Bildad og Na'amatiten Zofar, og aftalte at gå hen og vise ham deres Medfølelse og trøste ham.
Abwenzi atatu a Yobu, Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama, atamva za tsoka lonse limene linamugwera iye, ananyamuka ku nyumba zawo nakumana malo amodzi mopangana kuti apite ndi kukamupepesa Yobu ndi kumutonthoza.
12 Men da de i nogen Frastand så op og ikke kunde genkende ham, opløftede de deres Røst og græd, sønderrev alle tre deres Kapper og kastede Støv op over deres Hoveder.
Atamuona Yobuyo, iwo ali chapatalipo, sanathe kumuzindikira. Choncho anayamba kulira mokweza mawu ndipo anangʼamba mikanjo yawo ndi kuwaza fumbi pa mitu yawo.
13 Så sad de på Jorden hos ham i syv Dage og syv Nætter, uden at nogen af dem mælede et Ord til ham; thi de så, at hans Lidelser var såre store.
Tsono anakhala naye pamodzi pansi kwa masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku omwe. Palibe ndi mmodzi yemwe anayankhula naye, chifukwa anazindikira kuti Yobu amavutika kwambiri.