< Josua 3 >
1 Tidligt næste Morgen gjorde Josua sig rede, og hele Israel brød op fra Sjittim sammen med ham og kom til Jordan, og de tilbragte Natten der, før de drog over.
Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
2 Efter tre Dages Forløb gik Tilsynsmændene omkring i Lejren
Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
3 og bød Folket: »Naar I ser HERREN eders Guds Pagts Ark og Levitpræsterne komme bærende med den, saa skal I bryde op fra eders Plads og følge efter —
kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
4 dog skal der være en Afstand af 2000 Alen mellem eder og den; I maa ikke komme den for nær for at I kan vide, hvilken Vej I skal gaa; thi I er ikke kommet den Vej før!«
Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
5 Og Josua sagde til Folket: »Helliger eder; thi i Morgen vil HERREN gøre Undere iblandt eder!«
Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
6 Og Josua sagde til Præsterne: »Løft Pagtens Ark op og drag over foran Folket!« Saa løftede de Pagtens Ark op og gik foran Folket.
Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
7 Men HERREN sagde til Josua: »I Dag begynder jeg at gøre dig stor i hele Israels Øjne, for at de kan vide, at jeg vil være med dig, som jeg var med Moses.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
8 Du skal byde Præsterne, som bærer Pagtens Ark: Naar I kommer til Kanten af Jordans Vand, skal I standse der ved Jordan!«
Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
9 Da sagde Josua til Israeliterne: »Kom hid og hør HERREN eders Guds Ord!«
Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
10 Og Josua sagde: »Derpaa skal I kende, at der er en levende Gud iblandt eder, og at han vil drive Kana'anæerne, Hetiterne, Hivviterne, Perizziterne, Girgasjiterne, Amoriterne og Jebusiterne bort foran eder:
Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
11 Se, HERRENS, al Jordens Herres, Ark skal gaa foran eder gennem Jordan.
Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
12 Vælg eder nu tolv Mænd af Israels Stammer, een Mand af hver Stamme.
Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
13 Og saa snart Præsterne, som bærer HERRENS, al Jordens Herres, Ark, sætter Foden i Jordans Vand, skal Jordans Vand standse, det Vand, som kommer ovenfra, og staa som en Vold.«
Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
14 Da Folket saa brød op fra deres Telte for at gaa over Jordan med Præsterne, som bar Arken, i Spidsen,
Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
15 og da de, som bar Arken, kom til Jordan, og Præsterne, som bar Arken, rørte ved Vandkanten med deres Fødder — Jordan gik overalt over sine Bredder i hele Høsttiden —
Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
16 standsede Vandet, som kom ovenfra, og stod som en Vold langt borte, oppe ved Byen Adam, som ligger ved Zaretan, medens det Vand, som flød ned mod Araba— eller Salthavet, løb helt bort; saaledes gik Folket over lige over for Jeriko.
madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
17 Men Præsterne, som bar HERRENS Pagts Ark, blev staaende paa tør Bund midt i Jordan, medens hele Israel gik over paa tør Bund, indtil hele Folket havde tilendebragt Overgangen over Jordan.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.