< 1 Mosebog 50 >
1 Da kastede Josef sig over sin Faders Ansigt, græd og kyssede ham;
Kenaka Yosefe anadzigwetsa pa nkhope ya abambo ake, nawapsompsona kwinaku akulira.
2 og Josef befalede de lægekyndige blandt sine Tjenere at balsamere hans Fader, og Lægerne balsamerede Israel.
Ndipo Yosefe analamula antchito ake a chipatala kuti akonze thupi la Israeli ndi mankhwala kuti lisawole. Kotero antchitowo anakonzadi thupilo.
3 Dermed gik fyrretyve Dage, thi saa lang Tid tager Balsameringen: og Ægypterne begræd ham i halvfjerdsindstyve Dage.
Antchito aja zinawatengera masiku 40 kuti akonze mtembo uja popeza ntchito ngati imeneyi inafunikira masiku monga amenewa. Ndipo Aigupto anamulira Yakobo kwa masiku makumi asanu ndi awiri.
4 Da Grædetiden var omme, sagde Josef til Faraos Husfolk: »Hvis I har Godhed for mig, saa sig paa mine Vegne til Farao:
Yosefe atatha kulira maliro a abambo ake, anayankhula kwa nduna za Farao nati, “Ngati mungandikomere mtima, chonde mundiyankhulire kwa Farao kumuwuza kuti,
5 Min Fader tog mig i Ed, idet han sagde: Naar jeg er død, saa jord mig i den Grav, jeg lod mig grave i Kana'ans Land! Lad mig derfor drage op og jorde min Fader og saa vende tilbage hertil!«
‘Abambo anga anandilumbiritsa ndipo anati, ‘Ndatsala pangʼono kumwalira, ukandiyike mʼmanda amene ndinakumba ndekha mʼdziko la Kanaani.’ Tsono mundilole ndikayike abambo anga, ndipo ndikabweranso.’”
6 Da sagde Farao: »Drag kun op og jord din Fader, som han har ladet dig sværge.«
Farao anati, “Pita ukayike abambo ako monga anakulumbiritsa kuti uchite.”
7 Saa drog Josef op for at jorde sin Fader, og med ham drog alle Faraos Tjenere, de ypperste i hans Hus og de ypperste i Ægypten,
Kotero Yosefe anapita kukayika abambo ake. Nduna zonse za Farao, akuluakulu a bwalo lake ndi akuluakulu a ku Igupto, anapita naye pamodzi.
8 hele Josefs Hus og hans Brødre og hans Faders Hus, kun deres Kvinder og Børn, Smaakvæg og Hornkvæg lod de blive tilbage i Gosen;
Anapitanso onse a pa banja la Yosefe ndi abale ake ndi onse amene anali a pa banja la abambo ake. Ana awo okha, nkhosa ndi ngʼombe zinatsala ku Goseni
9 og med ham fulgte baade Stridsvogne og Ryttere, saa det blev en overmaade stor Karavane.
Asilikali okwera pa magaleta ndi asilikali a pa akavalo anapita nayenso pamodzi. Linali gulu lalikulu.
10 Da de kom til Goren-ha-atad hinsides Jordan, holdt de der en overmaade stor og højtidelig Dødeklage, og han fejrede Sørgefest for sin Fader i syv Dage.
Atafika pa Goreni ha-Atadi, pafupi ndi Yorodani, anachita mwambo waukulu wa maliro. Choncho Yosefe analira maliro a abambo ake masiku asanu ndi awiri.
11 Men da Landets Indbyggere, Kana'anæerne, saa denne Sørgefest i Goren-ha-atad, sagde de: »Ægypterne holder en højtidelig Sørgefest.« Derfor gav man det Navnet Abel-Mizrajim; det ligger hinsides Jordan.
Akanaani amene ankakhala ku Goreni ha-Atadi ataona mwambo wa maliro anati, “Aigupto ali ndi mwambo wa maliro a akulu.” Ndi chifukwa chake malo amenewo a pafupi ndi Yorodani amatchedwa Abeli-Mizraimu.
12 Og hans Sønner gjorde, som han havde paalagt dem;
Choncho ana a Yakobo anachita monga momwe abambo awo anawalamula:
13 hans Sønner førte ham til Kana'ans Land og jordede ham i Hulen paa Makpelas Mark, den Mark, som Abraham havde købt til Gravsted af Hetiten Efron over for Mamre.
Ndiye kuti ana a Yakobo anamunyamula kupita naye ku Kanaani kuti akamuyike mʼphanga limene lili mʼmunda wa Makipela pafupi ndi Mamre. Abrahamu anagula mundawo kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
14 Efter at have jordet sin Fader vendte Josef tilbage til Ægypten med sine Brødre og alle dem, der var draget op med ham til hans Faders Jordefærd.
Atatha kuyika abambo ake, Yosefe anabwerera ku Igupto, pamodzi ndi abale ake ndi onse amene anapita nawo kukayika abambo ake.
15 Da Josefs Brødre saa, at deres Fader var død, sagde de: »Blot nu ikke Josef vil vise sig fjendsk mod os og gengælde os alt det onde, vi har gjort ham!«
Abale ake a Yosefe ataona kuti abambo awo amwalira, anati, “Nanga tidzatani ngati Yosefe anatisungira mangawa nafuna kutibwezera pa zoyipa zonse zimene tinamuchitira?”
16 Derfor sendte de Bud til Josef og sagde: »Din Fader paalagde os før sin Død
Motero anatumiza mawu kwa Yosefe kuti, “Abambo anu anasiya malangizo asanafe nati:
17 at sige til Josef: Tilgiv dog dine Brødres Brøde og Synd, thi de har gjort ondt imod dig! Saa tilgiv nu din Faders Guds Tjenere deres Brøde!« Da græd Josef over deres Ord til ham.
‘Zimene mudzayenera kunena kwa Yosefe ndi izi: Ndikukupempha kuti uwakhululukire abale ako cholakwa chawo ndi machimo awo, popeza anakuchitira zoyipa.’ Ndiye tsopano chonde tikhululukireni zolakwa zimene ife akapolo a Mulungu wa abambo anu tinachita.” Yosefe atangomva mawu amenewa anayamba kulira.
18 Siden kom hans Brødre selv og faldt ham til Fode og sagde: »Se, vi vil være dine Trælle!«
Kenaka abale ake anabwera nadzigwetsa pansi pamaso pake, nati, “Ife ndife akapolo anu.”
19 Da sagde Josef til dem: »Frygt ikke, er jeg vel i Guds Sted?
Koma Yosefe anawawuza kuti, “Musachite mantha. Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu?
20 I tænkte ondt mod mig, men Gud tænkte at vende det til det gode for at gøre, hvad nu er sket, og holde mange Folk i Live;
Inu munafuna kundichitira zoyipa, koma Mulungu anasandutsa zoyipazo kuti zikhale zabwino kuti zikwaniritsidwe zimene zikuchitika panozi, zopulumutsa miyoyo yambiri.
21 frygt ikke, jeg vil sørge for eder og eders Kvinder og Børn!« Saaledes trøstede han dem og satte Mod i dem.
Kotero, musachite mantha. Ine ndidzasamalira inu pamodzi ndi ana anu omwe.” Tsono iye anawalimbitsa mtima powayankhula moleza mtima.
22 Josef blev nu i Ægypten, baade han og hans Faders Hus, og Josef blev 110 Aar gammel.
Yosefe anakhala mu Igupto pamodzi ndi banja lonse la abambo ake. Anakhala ndi moyo zaka 110
23 Josef saa Børn i tredje Led af Efraim; ogsaa Børn af Manasses Søn Makir fødtes paa Josefs Knæ.
ndipo anaona mʼbado wachitatu wa ana a Efereimu. Yosefe anatenganso ana a Makiri, mwana wa Manase kukhala ngati ana a mʼbanja lake.
24 Derpaa sagde Josef til sine Brødre: »Jeg dør snart, men Gud vil se til eder og føre eder fra Landet her til det Land, han tilsvor Abraham, Isak og Jakob.«
Kenaka Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndatsala pangʼono kufa. Koma mosakayika Mulungu adzakuyangʼanirani nadzakutengani kukutulutsani mʼdziko lino kupita ku dziko limene Iye analonjeza kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.”
25 Og Josef tog Israels Sønner i Ed og sagde: »Naar Gud ser til eder, skal I føre mine Ben bort herfra!«
Ndipo Yosefe analumbiritsa ana a Israeli lumbiro nati, “Lonjezani kuti Mulungu akadzakusungani mudzanyamula mafupa anga kuwachotsa ku malo kuno.”
26 Josef døde 110 Aar gammel, og man balsamerede ham og lagde ham i Kiste i Ægypten.
Choncho Yosefe anafa ali ndi zaka 110. Motero iwo atakonza thupi lake ndi mankhwala kuti lisawole, analiyika mʼbokosi ku Igupto.