< Lukas 18 >

1 Men han talte til dem en Lignelse om, at de burde altid bede og ikke blive trætte,
Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
2 og sagde: „Der var i en By en Dommer, som ikke frygtede Gud og ikke undsaa sig for noget Menneske.
Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
3 Og der var en Enke i den By, og hun kom til ham og sagde: Skaf mig Ret over min Modpart!
Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
4 Og længe vilde han ikke. Men derefter sagde han ved sig selv: Om jeg end ikke frygter Gud, ej heller undser mig for noget Menneske,
“Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
5 saa vil jeg dog, efterdi denne Enke volder mig Besvær, skaffe hende Ret, for at hun ikke uophørligt skal komme og plage mig.‟
koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
6 Men Herren sagde: „Hører, hvad den uretfærdige Dommer siger!
Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
7 Skulde da Gud ikke skaffe sine udvalgte Ret, de, som raabe til ham Dag og Nat? og er han ikke langmodig, naar det gælder dem?
Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
8 Jeg siger eder, han skal skaffe dem Ret i Hast. Men mon Menneskesønnen, naar han kommer, vil finde Troen paa Jorden?‟
Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
9 Men han sagde ogsaa til nogle, som stolede paa sig selv, at de vare retfærdige, og foragtede de andre, denne Lignelse:
Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
10 „Der gik to Mænd op til Helligdommen for at bede; den ene var en Farisæer, og den anden en Tolder.
“Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
11 Farisæeren stod og bad ved sig selv saaledes: Gud! Jeg takker dig, fordi jeg ikke er som de andre Mennesker, Røvere, uretfærdige, Horkarle, eller ogsaa som denne Tolder.
Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
12 Jeg faster to Gange om Ugen, jeg giver Tiende af al min Indtægt.
Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
13 Men Tolderen stod langt borte og vilde end ikke opløfte Øjnene til Himmelen, men slog sig for sit Bryst og sagde: Gud, vær mig Synder naadig!
“Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
14 Jeg siger eder: Denne gik retfærdiggjort hjem til sit Hus fremfor den anden; thi enhver, som ophøjer sig selv, skal fornedres; men den, som fornedrer sig selv, skal ophøjes.‟
“Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
15 Men de bare ogsaa de smaa Børn til ham, for at han skulde røre ved dem; men da Disciplene saa det, truede de dem.
Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
16 Men Jesus kaldte dem til sig og sagde: „Lader de smaa Børn komme til mig, og formener dem det ikke; thi Guds Rige hører saadanne til.
Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
17 Sandelig, siger jeg eder, den, som ikke modtager Guds Rige ligesom et lille Barn, han skal ingenlunde komme ind i det.‟
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
18 Og en af de Øverste spurgte ham og sagde: „Gode Mester! hvad skal jeg gøre, for at jeg kan arve et evigt Liv?‟ (aiōnios g166)
Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
19 Men Jesus sagde til ham: „Hvorfor kalder du mig god? Ingen er god uden een, nemlig Gud.
Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
20 Du kender Budene: Du maa ikke bedrive Hor; du maa ikke slaa ihjel; du maa ikke stjæle; du maa ikke sige falsk Vidnesbyrd; ær din Fader og din Moder.‟
Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
21 Men han sagde: „Det har jeg holdt alt sammen fra min Ungdom af.‟
Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
22 Men da Jesus hørte det, sagde han til ham: „Endnu een Ting fattes dig: Sælg alt, hvad du har, og uddel det til fattige, saa skal du have en Skat i Himmelen; og kom saa og følg mig!‟
Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
23 Men da han hørte dette, blev han dybt bedrøvet; thi han var saare rig.
Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
24 Men da Jesus saa, at han blev dybt bedrøvet, sagde han: „Hvor vanskeligt komme de, som have Rigdom, ind i Guds Rige!
Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
25 thi det er lettere for en Kamel at gaa igennem et Naaleøje end for en rig at gaa ind i Guds Rige.‟
Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
26 Men de, som hørte det, sagde: „Hvem kan da blive frelst?‟
Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
27 Men han sagde: „Hvad der er umuligt for Mennesker, det er muligt for Gud.‟
Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
28 Men Peter sagde: „Se, vi have forladt vort eget og fulgt dig.‟
Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
29 Men han sagde til dem: „Sandelig, siger jeg eder, der er ingen, som har forladt Hus eller Forældre eller Brødre eller Hustru eller Børn for Guds Riges Skyld,
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
30 uden at han skal faa det mange Fold igen i denne Tid og i den kommende Verden et evigt Liv.‟ (aiōn g165, aiōnios g166)
adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Men han tog de tolv til sig og sagde til dem: „Se, vi drage op til Jerusalem, og alle de Ting, som ere skrevne ved Profeterne, skulle fuldbyrdes paa Menneskesønnen.
Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
32 Thi han skal overgives til Hedningerne og spottes, forhaanes og bespyttes,
Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
33 og de skulle hudstryge og ihjelslaa ham; og paa den tredje Dag skal han opstaa.‟
adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
34 Og de fattede intet deraf, og dette Ord var skjult for dem, og de forstode ikke det, som blev sagt.
Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
35 Men det skete, da han nærmede sig til Jeriko, sad der en blind ved Vejen og tiggede.
Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
36 Og da han hørte en Skare gaa forbi, spurgte han, hvad dette var.
anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
37 Men de fortalte ham, at Jesus af Nazareth kom forbi.
Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
38 Og han raabte og sagde: „Jesus, du Davids Søn, forbarm dig over mig!‟
Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
39 Og de, som gik foran, truede ham, for at han skulde tie; men han raabte meget stærkere: „Du Davids Søn, forbarm dig over mig!‟
Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
40 Og Jesus stod stille og bød, at han skulde føres til ham; men da han kom nær til ham, spurgte han ham og sagde:
Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
41 „Hvad vil du, at jeg skal gøre for dig?‟ Men han sagde: „Herre! at jeg maa blive seende.‟
“Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
42 Og Jesus sagde til ham: „Bliv seende! din Tro har frelst dig.‟
Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
43 Og straks blev han seende, og han fulgte ham og priste Gud; og hele Folket lovpriste Gud, da de saa det.
Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.

< Lukas 18 >