< Lukas 17 >

1 Men han sagde til sine Disciple: „Det er umuligt, at Forargelser ikke skulde komme; men ve den, ved hvem de komme!
Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo.
2 Det er bedre for ham, om en Møllesten er lagt om hans Hals, og han er kastet i Havet, end at han skulde forarge een af disse smaa.
Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa.
3 Vogter paa eder selv! Dersom din Broder synder, da irettesæt ham; og dersom han angrer, da tilgiv ham!
Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha. “Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni.
4 Og dersom han syv Gange om Dagen synder imod dig og syv Gange vender tilbage til dig og siger: Jeg angrer det, da skal du tilgive ham.‟
Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”
5 Og Apostlene sagde til Herren: „Giv os mere Tro!‟
Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”
6 Men Herren sagde: „Dersom I havde Tro som et Sennepskorn, da kunde I sige til dette Morbærfigentræ: Ryk dig op med Rode, og plant dig i Havet, og det skulde adlyde eder.
Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.
7 Men hvem af eder, som har en Tjener, der pløjer eller vogter, siger til ham, naar han kommer hjem fra Marken: Gaa straks hen og sæt dig til Bords?
“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’
8 Vil han ikke tværtimod sige til ham: Tilbered, hvad jeg skal have til Nadvere, og bind op om dig, og vart mig op, medens jeg spiser og drikker; og derefter maa du spise og drikke?
Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’
9 Mon han takker Tjeneren, fordi han gjorde det, som var befalet? Jeg mener det ikke.
Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita?
10 Saaledes skulle ogsaa I, naar I have gjort alle de Ting, som ere eder befalede, sige: Vi ere unyttige Tjenere; kun hvad vi vare skyldige at gøre, have vi gjort.‟
Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’”
11 Og det skete, medens han var paa Vej til Jerusalem, at han drog midt imellem Samaria og Galilæa.
Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu.
12 Og da han gik ind i en Landsby, mødte der ham ti spedalske Mænd, som stode langt borte,
Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali
13 og de opløftede Røsten og sagde: „Jesus, Mester, forbarm dig over os!‟
ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”
14 Og da han saa dem, sagde han til dem: „Gaar hen og fremstiller eder for Præsterne!‟ Og det skete, medens de gik bort, bleve de rensede.
Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.
15 Men en af dem vendte tilbage, da han saa, at han var helbredet, og priste Gud med høj Røst.
Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza.
16 Og han faldt paa sit Ansigt for hans Fødder og takkede ham; og denne var en Samaritan.
Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.
17 Men Jesus svarede og sagde: „Bleve ikke de ti rensede? hvor ere de ni?
Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti?
18 Fandtes der ingen, som vendte tilbage for at give Gud Ære, uden denne fremmede?‟
Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?”
19 Og han sagde til ham: „Staa op, gaa bort; din Tro har frelst dig!‟
Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”
20 Men da han blev spurgt af Farisæerne om, naar Guds Rige kommer, svarede han dem og sagde: „Guds Rige kommer ikke saaledes, at man kan vise derpaa.
Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso,
21 Ikke heller vil man sige: Se her, eller: Se der er det; thi se, Guds Rige er inden i eder.‟
kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”
22 Men han sagde til Disciplene: „Der skal komme Dage, da I skulle attraa at se en af Menneskesønnens Dage, og I skulle ikke se den.
Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona.
23 Og siger man til eder: Se der, eller: Se her er han, saa gaar ikke derhen, og løber ikke derefter!
Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo.
24 Thi ligesom Lynet, naar det lyner fra den ene Side af Himmelen, skinner til den anden Side af Himmelen, saaledes skal Menneskesønnen være paa sin Dag.
Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake.
25 Men først bør han lide meget og forkastes af denne Slægt.
Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.
26 Og som det skete i Noas Dage, saaledes skal det ogsaa være i Menneskesønnens Dage:
“Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu.
27 De spiste, drak, toge til Ægte, bleve bortgiftede indtil den Dag, da Noa gik ind i Arken, og Syndfloden kom og ødelagde alle.
Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.
28 Ligeledes, som det skete i Loths Dage: De spiste, drak, købte, solgte, plantede, byggede;
“Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga.
29 men paa den Dag, da Loth gik ud af Sodoma, regnede Ild og Svovl ned fra Himmelen og ødelagde dem alle:
Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.
30 paa samme Maade skal det være paa den Dag, da Menneskesønnen aabenbares.
“Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera.
31 Paa den Dag skal den, som er paa Taget og har sine Ejendele i Huset, ikke stige ned for at hente dem; og ligesaa skal den, som er paa Marken, ikke vende tilbage igen!
Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse.
32 Kommer Loths Hustru i Hu!
Kumbukirani mkazi wa Loti!
33 Den, som søger at bjærge sit Liv, skal miste det; og den, som mister det, skal beholde Livet.
Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga.
34 Jeg siger eder: I den Nat skulle to Mænd være paa eet Leje; den ene skal tages med, og den anden skal lades tilbage.
Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa.
35 To Kvinder skulle male paa samme Kværn; den ene skal tages med, og den anden skal lades tilbage.
Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.
36 [To Mænd skulle være paa Marken; den ene skal tages med, og den anden skal lades tilbage.‟]
Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”
37 Og de svare og sige til ham: „Hvor, Herre?‟ Men han sagde til dem: „Hvor Aadselet er, der ville ogsaa Ørnene samle sig.‟
Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?” Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”

< Lukas 17 >