< Jeremiáš 34 >

1 Slovo, kteréž se stalo k Jeremiášovi od Hospodina, (když Nabuchodonozor král Babylonský, a všecko vojsko jeho, i všecka království země pod moc jeho přináležející, všickni také národové bojovali proti Jeruzalému a proti všechněm městům jeho), řkoucí:
Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi gulu lake lonse lankhondo, pamodzi ndi maufumu onse a pa dziko lapansi amene ankawalamulira ndiponso anthu a mitundu yonse ankathira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda yonse yozungulira Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Takto praví Hospodin Bůh Izraelský: Jdi a rci Sedechiášovi králi Judskému, rci, pravím, jemu: Takto dí Hospodin: Aj, já dám toto město v ruku krále Babylonského, aby je vypálil ohněm.
“Yehova, Mulungu wa Israeli akuti: Pita kwa Zedekiya mfumu ya Yuda ndipo ukamuwuze kuti Yehova akuti mzinda uno ndidzawupereka mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni ndipo adzawutentha ndi moto.
3 I ty neznikneš ruky jeho, ale jistotně jat a v ruku jeho vydán budeš, a oči tvé uzří oči krále Babylonského, i ústa jeho s ústy tvými mluviti budou, a do Babylona se dostaneš.
Iweyo sudzapulumuka mʼmanja mwake koma udzagwidwa ndithu ndipo adzakupereka mʼmanja mwake. Udzayiona mfumu ya ku Babuloni maso ndi maso ako ndipo udzayankhula nayo pakamwa ndi pakamwa. Ndipo udzapita ku Babuloni.
4 A však slyš slovo Hospodinovo, Sedechiáši králi Judský: Takto praví Hospodin o tobě: Neumřeš od meče,
“Koma iwe Zedekiya mfumu ya Yuda, imva lonjezo ili la Yehova. Izi ndi zimene Yehova akunena za iwe: Sudzaphedwa pa nkhondo;
5 V pokoji umřeš. A jakož pálívali otcům tvým, králům předešlým, kteříž byli před tebou, tak páliti budou tobě, a říkajíce: Ach, pane, kvíliti budou nad tebou; nebo slovo toto já mluvil jsem, dí Hospodin.
udzafera pa mtendere. Monga anthu ankafukiza lubani poyika maliro a makolo ako akale, amene anali mafumu iwe usanalowe ufumu, choncho nawenso podzayika maliro ako adzafukiza lubani ndipo polira azidzati, ‘Kalanga, mbuye wanga!’ Ine mwini ndalonjeza zimenezi, akutero Yehova.”
6 I mluvil Jeremiáš prorok Sedechiášovi, králi Judskému, všecka slova ta v Jeruzalémě,
Ndipo mneneri Yeremiya anawuza zonsezi Zedekiya mfumu ya Yuda, mu Yerusalemu.
7 Když vojsko krále Babylonského bojovalo proti Jeruzalému a proti všechněm městům Judským ostatním, proti Lachis a proti Azeku; nebo ta byla pozůstala z měst Judských města hrazená.
Nthawi imeneyi nʼkuti gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni likuthira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda ina yotsala ya Yuda, Lakisi ndi Azeka. Imeneyi yokha ndiye inali mizinda yotetezedwa yotsala ya ku Yuda.
8 Slovo, kteréž se stalo k Jeremiášovi od Hospodina, když učinil král Sedechiáš smlouvu se vším lidem, kterýž byl v Jeruzalémě, o vyhlášení jim svobody,
Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya. Nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Zedekiya atachita pangano ndi anthu onse a mu Yerusalemu kuti alengeze zakuti akapolo awo adzawamasule.
9 Aby propustil jeden každý služebníka svého a jeden každý děvku svou, Hebrejského neb Hebrejskou, svobodné, aby nepodroboval sobě v službu Žida, bratra svého, nižádný.
Aliyense amene anali ndi akapolo a Chihebri, aamuna kapena aakazi awamasule; palibe amene ayenera kusunga mu ukapolo Myuda mnzake.
10 Tedy uposlechla všecka knížata a všecken lid, kterýž byl v smlouvu všel, aby propustil jeden každý služebníka svého a jeden každý děvku svou svobodné, aby nepodroboval jich v službu více; uposlechli, pravím, a propustili.
Choncho akuluakulu pamodzi ndi anthu onse amene anachita pangano ili anagwirizana kuti amasule akapolo awo aamuna ndi aakazi ndi kuti asawasungenso mu ukapolo. Iwo anachitadi zimenezi ndipo anawamasuladi.
11 Potom pak rozmyslivše se, zase pobrali služebníky své a děvky své, kteréž byli propustili svobodné, a podrobili je sobě za služebníky a děvky.
Koma pambuyo pake anasintha maganizo awo ndi kuwatenganso amuna ndi akazi amene anawamasula aja ndipo anawasandutsanso akapolo.
12 I stalo se slovo Hospodinovo k Jeremiášovi od Hospodina, řkoucí:
Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti:
13 Takto praví Hospodin Bůh Izraelský: Já jsem učinil smlouvu s otci vašimi toho dne, když jsem je vyvedl z země Egyptské, z domu služebníků, řka:
“Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Ine ndinachita pangano ndi makolo anu pamene ndinawatulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo. Ine ndinati,
14 Po vyplnění sedmi let propouštívejte jeden každý bratra svého Žida, kterýž by prodán byl tobě, a sloužilť by šest let, propusť, pravím, jej svobodného od sebe. Ale neuposlechli otcové vaši mne, aniž naklonili ucha svého.
‘Chaka chachisanu ndi chiwiri chilichonse aliyense wa inu ayenera kumasula mʼbale wake wa Chihebri amene anadzigulitsa yekha kwa inuyo. Iyeyo amasulidwe akagwira ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, mumulole apite mwaufulu.’ Komatu makolo anu sanandimvere kapena kusamala konse.
15 Vy zajisté usmyslivše sobě dnes, učinili jste to, což jest spravedlivého před očima mýma, že jste vyhlásili svobodu jeden každý bližnímu svému, učinivše smlouvu před oblíčejem mým v domě tom, kterýž nazván jest od jména mého.
Posachedwa pomwepa inu munalapa ndi kuchita zinthu zabwino pamaso panga: Aliyense wa inu anamasula mʼbale wake. Ndipo munachita pangano pamaso panga mʼNyumba imene imadziwika ndi dzina langa kuti mudzachitadi zimenezi.
16 Ale zase zpáčivše se, zlehčili jste jméno mé, že jste vzali zase jeden každý služebníka svého a jeden každý děvku svou, kteréž jste byli propustili svobodné podlé žádosti jejich, a podrobili jste je, aby byli vaši služebníci a děvky.
Koma tsopano mwasintha maganizo anu ndipo mwayipitsa dzina langa. Mwatenganso ukapolo aamuna ndi aakazi amene munawamasula aja kuti apite kumene akufuna. Mwawakakamiza kuti akhalebe akapolo anu.
17 Protož takto praví Hospodin: Vy neuposlechli jste mne, abyste vyhlásili svobodu jeden každý bratru svému, a jeden každý bližnímu svému, aj, já vyhlašuji proti vám svobodu, dí Hospodin, meči, moru a hladu, a vydám vás ku posmýkání po všech královstvích země.
“Nʼchifukwa chake Yehova akuti: Inu simunandimvere Ine; simunalengeze kuti abale anu amasulidwe. Chabwino! Ine ndidzakupatsani ufulu; ufulu wake ukhala wophedwa ndi nkhondo, mliri ndi njala. Ndidzakusandutsani chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
18 Vydám zajisté ty lidi, jenž přestoupili smlouvu mou, kteříž nevykonali slov smlouvy té, kterouž učinili před oblíčejem mým, když tele rozťali na dvé, a prošli mezi díly jeho,
Inu simunasunge pangano limene munachita ndi Ine. Simunasamale lonjezo limene munachita pamaso panga. Choncho ndidzakusandutsani ngati mwana wangʼombe uja amene ankamudula pawiri napita pakati pa zigawozo.
19 Totiž knížata Judská a knížata Jeruzalémská, komorníci, a kněží, i všecken lid té země, kteříž prošli mezi díly toho telete.
Amene ankadutsa pakati pa zigawozo anali atsogoleri a Yuda ndi Yerusalemu, akuluakulu a bwalo, ansembe ndi anthu onse a mʼdzikomo.
20 Vydám je, pravím, v ruku nepřátel jejich, a v ruku hledajících bezživotí jejich, i budou těla mrtvá jejich za pokrm ptactvu nebeskému, a šelmám zemským.
Onsewa ndidzawapereka kwa adani awo amene akufuna kuwapha. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo za dziko lapansi.
21 Sedechiáše také krále Judského, i knížata jeho vydám v ruku nepřátel jejich, a v ruku hledajících bezživotí jejich, v ruku, pravím, vojska krále Babylonského, kteříž odtáhli od vás.
“Ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda ndi nduna zake kwa adani awo amene akufuna kuwapha, kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni limene nthawi ino layamba kubwerera mʼmbuyo.
22 Aj, já přikáži, dí Hospodin, a přivedu je zase na město toto, aby bojovali proti němu, a vezmouce je, vypálili je ohněm; města také Judská obrátím v poušť, tak že nebude žádného obyvatele.
Taonani, Ine ndidzawalamula, akutero Yehova, ndipo ndidzawabweretsanso ku mzinda uno. Adzathira nkhondo mzindawu, kuwulanda ndi kuwutentha. Ndipo Ine ndidzasandutsa chipululu mizinda ya Yuda kotero kuti palibe amene adzakhalemo.”

< Jeremiáš 34 >