< Ámos 7 >

1 Toto mi ukázal Panovník Hospodin, že aj, formoval kobylky, když nejprvé počala růsti otava, když aj, otava byla po královském posečení.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
2 I stalo se, když snědly byliny zemské, že jsem řekl: Panovníče Hospodine, odpustiž, prosím. Kdož zůstane Jákobovi? Neboť ho maličko jest.
Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
3 I želel Hospodin toho. Nestaneť se, řekl Hospodin.
Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
4 Tedy ukázal mi Panovník Hospodin, a aj, Panovník Hospodin volal, že při svou povede ohněm. A spáliv propast velikou, spálil i díl.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
5 Já pak řekl jsem: Panovníče Hospodine, přestaniž, prosím. Kdož zůstane Jákobovi? Neboť ho maličko jest.
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
6 I želel Hospodin toho. A ani toho se nestane, řekl Panovník Hospodin.
Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
7 Potom ukázal mi, a aj, Pán stál na zdi podlé pravidla vzdělané, v jehož ruce bylo pravidlo.
Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
8 I řekl mi Hospodin: Co vidíš, Amose? Řekl jsem: Pravidlo. I řekl Pán: Aj, já položím pravidlo u prostřed lidu svého Izraelského, nebuduť již více promíjeti jemu.
Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
9 Nebo zpuštěny budou výsosti Izákovy, a svatyně Izraelovy zpustnou, tehdáž, když povstanu proti domu Jeroboámovu s mečem.
“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
10 Tedy poslal Amaziáš kněz Bethelský k Jeroboámovi králi Izraelskému, řka: Spuntoval se proti tobě Amos u prostřed domu Izraelského, ta země nemohla by snésti všech slov jeho.
Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
11 Nebo takto praví Amos: Od meče umře Jeroboám, a Izrael jistotně přestěhován bude z země své.
Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
12 Potom řekl Amaziáš Amosovi: Ó vidoucí, ujdi, radímť, utec do země Judské, a jez tam chléb, a tam prorokuj.
Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
13 Ale v Bethel již více neprorokuj, nebo ono svatyně králova i dům královský jest.
Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
14 Tedy odpovídaje Amos, řekl Amaziášovi: Nebylť jsem já prorokem, ano ani synem prorockým, ale byl jsem skotákem, a česával jsem plané fíky.
Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
15 Ale Hospodin mne vzal, když jsem chodil za stádem, a řekl mi Hospodin: Jdi, prorokuj lidu mému Izraelskému.
Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
16 Nyní tedy slyšiž slovo Hospodinovo. Ty pravíš: Neprorokuj v Izraeli, a nekaž v domě Izákově.
Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
17 Protož takto praví Hospodin: Žena tvá cizoložiti bude v městě, synové pak tvoji i dcery tvé od meče padnou; a země tvá provazcem dělena bude, a ty v zemi nečisté umřeš, Izrael pak jistotně přestěhován bude z země své.
“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”

< Ámos 7 >