< Jeremiáš 21 >

1 Slovo, kteréž se stalo k Jeremiášovi od Hospodina, když poslal k němu král Sedechiáš Paschura syna Malkiášova a Sofoniáše syna Maaseiášova, kněze, aby řekli:
Mfumu Zedekiya inatuma Pasuri mwana wa Malikiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa Yeremiya.
2 Poraď se medle o nás s Hospodinem, nebo Nabuchodonozor král Babylonský bojuje proti nám, zdali by snad naložil Hospodin s námi podlé všech divných skutků svých, aby on odtáhl od nás.
Iwo amati akanene kwa Yeremiya mawu akuti, “Tinenere kwa Yehova chifukwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni akutithira nkhondo. Mwina mwake Yehova nʼkutichitira zodabwitsa kuti Nebukadinezarayo achoke kwathu kuno.”
3 Tedy řekl Jeremiáš k nim: Tak rcete Sedechiášovi:
Koma Yehova anawuza Yeremiya kuti ayankhe Pasuri ndi Zefaniya kuti, “Kamuwuzeni Zedekiya kuti,
4 Takto praví Hospodin Bůh Izraelský: Aj, já odvrátím nástroje válečné, kteréž jsou v rukou vašich, jimiž vy bojujete proti králi Babylonskému a Kaldejským, kteříž oblehli vás vně za zdí, a shromáždím je do prostřed města tohoto.
‘Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ndikulandeni zida zimene zili mʼmanja mwanu zimene mukugwiritsa ntchito polimbana ndi mfumu ya ku Babuloni ndi ankhondo ake amene akuzingani kunja kwa lingali. Ndipo ndidzasonkhanitsa zidazo mʼkati mwa mzindawu.
5 Bojovati zajisté budu já proti vám rukou vztaženou a ramenem silným, a to v hněvě a v rozpálení i v prchlivosti veliké.
Ineyo mwini wakene ndi mkono wotambasula ndi dzanja lamphamvu, ndidzachita nanu nkhondo ndili wokwiya, wokalipa ndi waukali.
6 A raním obyvatele města tohoto, tak že lidé i hovada morem velikým pomrou.
Ndidzakantha amene amakhala mu mzinda muno, anthu pamodzi ndi zirombo, ndipo zidzafa ndi mliri woopsa.
7 Potom pak (dí Hospodin), dám Sedechiáše krále Judského a služebníky jeho i lid, totiž ty, kteříž pozůstanou v městě tomto po moru, po meči a po hladu, v ruku Nabuchodonozora krále Babylonského, a v ruku nepřátel jejich, a tak v ruku hledajících bezživotí jejich. Kterýžto je zbije ostrostí meče, neodpustí jim, aniž jich šanovati bude, aniž se smiluje.
Pambuyo pake, ndidzapereka Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi anthu a mu mzinda muno amene adzapulumuke pa nthawi ya mliri, lupanga ndi njala kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi kwa adani awo amene ankafuna kuwapha. Iye adzawapha ndi lupanga. Sadzawachitira chifundo kapena kuwamvera chisoni kapenanso kuwakomera mtima.’
8 Protož rci lidu tomuto: Takto praví Hospodin: Aj, já kladu před vás cestu života i cestu smrti.
“Yehova anati ndiwawuzenso anthu amenewa kuti asankhe pakati pa moyo ndi imfa.
9 Kdokoli zůstane v městě tomto, zahyne od meče, neb hladem, neb morem, ale kdož vyjde a poddá se Kaldejským, kteříž oblehli vás, jistotně živ zůstane, a bude míti život svůj místo kořisti.
Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzaphedwa ndi lupanga, njala kapena mliri. Koma aliyense amene apite kukadzipereka kwa Ababuloni amene akuzinganiwa adzakhala ndi moyo, adzapulumuka.
10 Nebo postavil jsem zůřivou tvář svou proti městu tomuto k zlému, a ne k dobrému, dí Hospodin. V ruku krále Babylonského vydáno bude, i vypálí je ohněm.
Ine ndatsimikiza kuchitira mzinda uno choyipa osati chabwino, akutero Yehova. Udzaperekedwa mʼdzanja la mfumu ya ku Babuloni, ndipo iyeyo adzawutentha ndi moto.
11 Domu pak krále Judského rci: Slyšte slovo Hospodinovo,
“Komanso, uwuze banja laufumu la Yuda kuti, ‘Imva mawu a Yehova;
12 Ó dome Davidův, takto praví Hospodin: Držívejte každého jitra soud, a vychvacujte obloupeného z ruky násilníka, aby nevyšla jako oheň prchlivost má, a nehořela, tak že by nebylo žádného, kdo by uhasiti mohl, pro nešlechetnost předsevzetí vašich.
inu a mʼbanja la Davide, Yehova akuti, “‘Weruzani mwachilungamo mmawa uliwonse; pulumutsani mʼdzanja la wozunza aliyense amene walandidwa katundu wake, kuopa kuti ukali wanga ungabuke ndi kuyaka ngati moto wosazimitsika chifukwa cha zoyipa zimene mwachita.
13 Aj já, dí Hospodin, na tebe, kteráž přebýváš v údolí tomto, skálo roviny této, kteříž říkáte: Kdo by přitáhl na nás, aneb kdo by všel do příbytků našich?
Ndidzalimbana nanu, inu amene mukukhala pamwamba pa chigwa, inu okhala ngati thanthwe lapachidikha, akutero Yehova. Inu amene mumanena kuti, ‘Ndani amene angabwere kudzalimbana nafe? Ndani amene angathe kulowa mʼmalinga mwathu?’
14 Nebo trestati vás budu podlé skutků vašich, dí Hospodin, a zanítím oheň v lese tvém, kterýž zžíře všecko vůkol něho.
Ndidzakulangani molingana ndi ntchito zanu, akutero Yehova. Ndidzatentha nkhalango zanu; moto udzapsereza zonse zimene zakuzungulirani.’”

< Jeremiáš 21 >