< Plaè 1 >

1 Ach, město tak lidné, jakť jest samotné zůstalo, a učiněno jako vdova! Nejznamenitější mezi národy, přední mezi krajinami pod plat uvedeno.
Haa! Mzinda uja wasiyidwa wokhawokha, umene kale unali wodzaza ndi anthu! Kale unali wotchuka pakati pa mitundu ya anthu! Tsopano wasanduka ngati mkazi wamasiye. Kale unali mfumukazi ya onse pa dziko lapansi, tsopano wasanduka kapolo.
2 Ustavičně pláče v noci, a slzy jeho na lících jeho, ze všech milovníků svých nemá žádného potěšitele; všickni přátelé jeho nevěrně se k němu mají, obrátili se mu v nepřátely.
Ukulira mowawidwa mtima usiku wonse, misozi ili pa masaya pake. Mwa abwenzi ake onse, palibe ndi mmodzi yemwe womutonthoza. Abwenzi ake onse amuchitira chiwembu; onse akhala adani ake.
3 Zastěhoval se Juda, proto že byl trápen a u veliké porobě, však osadiv se mezi pohany, nenalézá odpočinutí; všickni, kteříž jej honí, postihají jej v těsně.
Yuda watengedwa ku ukapolo, kukazunzika ndi kukagwira ntchito yolemetsa. Iye akukhala pakati pa anthu a mitundu ina; ndipo alibe malo opumulira. Onse omuthamangitsa iye amupitirira, ndipo alibe kwina kothawira.
4 Cesty Siona kvílí, že žádný nepřichází k slavnosti. Všecky brány jeho zpustly, kněží jeho vzdychají, panny jeho smutné jsou, on pak sám pln jest hořkosti.
Misewu yopita ku Ziyoni ikulira, chifukwa palibe ndi mmodzi yemwe akubwera ku maphwando ake. Zipata zake zonse zili pululu, ansembe akubuwula. Anamwali ake akulira, ndipo ali mʼmasautso woopsa.
5 Nepřátelé jeho jsou hlavou, odpůrcům jeho šťastně se vede; nebo jej Hospodin zarmoutil pro množství přestoupení jeho. Maličcí jeho odešli do zajetí před oblíčejem nepřítele.
Adani ake asanduka mabwana ake; odana naye akupeza bwino. Yehova wamubweretsera mavuto chifukwa cha machimo ake ambiri. Ana ake atengedwa ukapolo pamaso pa mdani.
6 A tak odňata od dcery Sionské všecka okrasa její. Knížata její jsou podobná jelenům, kteříž nenalézají pastvy, a ucházejí bez moci před tím, kdož je honí.
Ulemerero wonse wa mwana wamkazi wa Ziyoni wachokeratu. Akalonga ake ali ngati mbawala zosowa msipu; alibe mphamvu zothawira owathamangitsa.
7 Rozpomínáť se dcera Jeruzalémská ve dnech trápení svého a kvílení svého na všecka svá utěšení, kteráž mívala ode dnů starodávních, když padá lid její od ruky nepřítele, nemajíc žádného, kdo by ji retoval. Protivníciť se jí dívajíce, posmívají se klesnutí jejímu.
Pa masiku a masautso ndi kuzunzika kwake, Yerusalemu amakumbukira chuma chonse chimene mʼmasiku amakedzana chinali chake. Anthu ake atagwidwa ndi adani ake, panalibe aliyense womuthandiza. Adani ake ankamuyangʼana ndi kumuseka chifukwa cha kuwonongeka kwake.
8 Těžce hřešila dcera Jeruzalémská, protož jako nečistá odloučena jest. Všickni, kteříž ji v poctivosti mívali, neváží jí sobě, proto že vidí nahotu její; ona pak vzdychá, obrácena jsuci zpět.
Yerusalemu wachimwa kwambiri ndipo potero wakhala wodetsedwa. Onse amene ankamulemekeza pano akumunyoza, chifukwa aona umaliseche wake. Iye mwini akubuwula ndipo akubisa nkhope yake.
9 Nečistota její na podolcích jejích; nepamatovala na skončení své, protož patrně klesá, nemajíc žádného, kdo by ji potěšil. Popatřiž, Hospodine, na trápení mé, neboť se vyvýšil nepřítel.
Uve wake umaonekera pa zovala zake; iye sanaganizire za tsogolo lake. Nʼchifukwa chake kugwa kwake kunali kwakukulu; ndipo analibe womutonthoza. “Inu Yehova, taonani masautso anga, pakuti mdani wapambana.”
10 Sáhl rukou svou nepřítel na všecky drahé věci její; nebo musí se dívati pohanům, an chodí do svatyně její, o čemž jsi byl přikázal, aby tobě nevcházeli do shromáždění.
Adani amulanda chuma chake chonse; iye anaona mitundu ya anthu achikunja ikulowa mʼmalo ake opatulika, amene Inu Mulungu munawaletsa kulowa mu msonkhano wanu.
11 Všecken lid její vzdychajíce, hledají chleba, vynakládají nejdražší věci své za pokrm k očerstvení života. Vzezřiž, Hospodine, a popatřiž, neboť jsem v nevážnosti.
Anthu ake onse akubuwula pamene akufunafuna chakudya; asinthanitsa chuma chawo ndi chakudya kuti akhale ndi moyo. “Inu Yehova, taonani ndipo ganizirani, chifukwa ine ndanyozeka.”
12 Nic-liž vám do toho, ó všickni, kteříž tudyto jdete? Pohleďte a vizte, jest-li bolest podobná bolesti mé, kteráž jest mi učiněna, jak mne zámutkem naplnil Hospodin v den prchlivosti hněvu svého.
“Kodi zimenezi mukuziyesa zachabe, inu nonse mukudutsa? Yangʼanani ndipo muone. Kodi pali mavuto ofanana ndi amene andigwerawa, amene Ambuye anandibweretsera pa tsiku la ukali wake?
13 Seslal s výsosti oheň do kostí mých, kterýž opanoval je; roztáhl sít nohám mým, obrátil mne zpět, obrátil mne v pustinu, celý den neduživá jsem.
“Anatumiza moto kuchokera kumwamba, unalowa mpaka mʼmafupa anga. Anayala ukonde kuti ukole mapazi anga ndipo anandibweza. Anandisiya wopanda chilichonse, wolefuka tsiku lonse.
14 Tuze svázáno jest rukou jeho jho přestoupení mých, tuze spletené houžve připadly na hrdlo mé, porazilo sílu mou; vydal mne Pán v ruku nepřátel, nemohuť povstati.
“Wazindikira machimo anga onse ndipo ndi manja ake anawaluka pamodzi. Machimowa afika pakhosi panga, ndipo Ambuye wandithetsa mphamvu. Iye wandipereka kwa anthu amene sindingalimbane nawo.
15 Pošlapal Pán všecky mé silné u prostřed mne, svolal proti mně zástupy, aby potřel mládence mé, tlačil Pán presem pannu dceru Judskou.
“Ambuye wakana anthu anga onse amphamvu omwe ankakhala nane: wasonkhanitsa gulu lankhondo kuti lilimbane nane, kuti litekedze anyamata anga; mʼmalo ofinyira mphesa Ambuye wapondereza anamwali a Yuda.
16 Pro tyť věci já pláči, z očí mých, z očí mých tekou vody, a že jest vzdálen ode mne potěšitel, kterýž by očerstvil duši mou; synové moji jsou pohubeni, nebo ssilil se nepřítel.
“Chifukwa cha zimenezi ndikulira ndipo maso anga adzaza ndi misozi. Palibe aliyense pafupi woti anditonthoze, palibe aliyense wondilimbitsa mtima. Ana anga ali okhaokha chifukwa mdani watigonjetsa.
17 Rozprostírá dcera Sionská ruce své, nemá žádného, kdo by ji potěšil; vzbudiltě Hospodin proti Jákobovi všudy vůkol něho nepřátely jeho, mezi nimiž jest dcera Jeruzalémská jako pro nečistotu oddělená.
“Ziyoni wakweza manja ake, koma palibe aliyense womutonthoza. Yehova walamula kuti abale ake a Yakobo akhale adani ake; Yerusalemu wasanduka chinthu chodetsedwa pakati pawo.
18 Spravedlivý jest Hospodin, neboť jsem na odpor činila ústům jeho. Slyšte medle všickni lidé, a vizte bolest mou; panny mé i mládenci moji odebrali se do zajetí.
“Yehova ndi wolungama, koma ndine ndinawukira malamulo ake. Imvani inu anthu a mitundu yonse; onani masautso anga. Anyamata ndi anamwali anga agwidwa ukapolo.
19 Volala jsem na milovníky své, oni oklamali mne; kněží moji a starci moji v městě pomřeli, hledajíce pokrmu, aby posilnili života svého.
“Ndinayitana abwenzi anga koma anandinyenga. Ansembe ndi akuluakulu anga anafa mu mzinda pamene ankafunafuna chakudya kuti akhale ndi moyo.
20 Popatřiž, ó Hospodine, neboť mi úzko; vnitřnosti mé zkormouceny jsou, srdce mé svadne ve mně, proto že jsem na odpor velice činila. Vně meč na sirobu přivodí, v domě pouhá smrt.
“Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira! Ndikuzunzika mʼkati mwanga, ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa chifukwa ndakhala osamvera. Mʼmisewu anthu akuphedwa, ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.
21 Slýchajíť, že já vzdychám, ale není žádného, kdo by mne potěšil. Všickni nepřátelé moji slyšíce o mých bídách, radují se, že jsi to učinil, a přivedl den předohlášený, ale budouť mně podobní.
“Anthu amva kubuwula kwanga, koma palibe wonditonthoza. Adani anga onse amva masautso anga; iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita. Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija kuti iwonso adzakhale ngati ine.
22 Nechť přijde všecka nešlechetnost jejich před oblíčej tvůj, a učiň jim, jakož jsi učinil mně pro všecka přestoupení má; neboť jsou mnohá úpění má, a srdce mé neduživé.
“Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu; muwalange ngati mmene mwandilangira ine chifukwa cha machimo anga onse. Ndikubuwula kwambiri ndipo mtima wanga walefuka.”

< Plaè 1 >