< Ezechiel 8 >

1 I stalo se léta šestého, v pátý den šestého měsíce, že jsem seděl v domě svém, a starší Judští seděli přede mnou. I připadla na mne tu ruka Panovníka Hospodina.
Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira.
2 A viděl jsem, a aj, podobenství na pohledění jako oheň. Od bedr jeho dolů oheň, od bedr pak jeho vzhůru na pohledění jako blesk, na pohledění jako nějaká velmi prudká světlost.
Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira.
3 Tedy vztáh podobenství ruky, vzal mne za kštici hlavy mé, a vyzdvihl mne Duch mezi nebe a mezi zemi, a uvedl mne do Jeruzaléma u viděních Božích, k vratům brány vnitřní, kteráž patří na půlnoci, kdež byla stolice modly k horlivosti a k zůřivosti popouzející.
Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu.
4 A aj, sláva Boha Izraelského byla tam na pohledění jako ta, kterouž jsem viděl v údolí.
Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.
5 I řekl mi: Synu člověčí, pozdvihni nyní očí svých k cestě na půlnoci. Tedy pozdvihl jsem oči svých k cestě na půlnoci, a aj, na půlnoci u brány oltářové ta modla horlení, právě kudyž se vchází.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.
6 V tom řekl mi: Synu člověčí, vidíš-liž ty, co tito činí, ohavnosti tak veliké, kteréž činí dům Izraelský tuto, tak že se vzdáliti musím od svatyně své? Ale obrátě se, uzříš ještě větší ohavnosti.
Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”
7 I přivedl mne ke dveřům síně, kdež jsem uzřel, a aj, díra jedna byla v stěně.
Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo.
8 A řekl mi: Synu člověčí, kopej medle tu stěnu. I kopal jsem stěnu, a aj, dvéře jedny.
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.
9 Tedy řekl mi: Vejdi, a viz ohavnosti tyto nejhorší, kteréž oni činí zde.
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.”
10 Protož všed, uzřel jsem, a aj, všeliké podobenství zeměplazů a hovad ohyzdných, i všech ukydaných bohů domu Izraelského vyryto bylo na stěně vůkol a vůkol.
Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza.
11 A sedmdesáte mužů z starších domu Izraelského, s Jazaniášem synem Safanovým, stojícím u prostřed nich, stáli před nimi, maje každý kadidlnici svou v ruce své, tak že hustý oblak kadění vzhůru vstupoval.
Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.
12 I řekl mi: Viděl-lis, synu člověčí, co starší domu Izraelského činí ve tmě, jeden každý v pokojích svých malovaných? Nebo říkají: Nikoli na nás nepatří Hospodin, opustil Hospodin zemi.
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’
13 Dále mi řekl: Obrátě se, uzříš ještě větší ohavnosti, kteréž oni činí.
Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’”
14 I přivedl mne k vratům brány domu Hospodinova, kteráž jest na půlnoci, a aj, ženy seděly tam, plačíce Tammuze.
Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi.
15 I řekl mi: Viděl-lis, synu člověčí? Obrátě se, uzříš ještě větší ohavnosti nad tyto.
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”
16 Tedy uvedl mne do síně domu Hospodinova vnitřní, a aj, u vrat chrámu Hospodinova, mezi síňcí a oltářem bylo okolo pětmecítma mužů, jejichž záda byla k chrámu Hospodinovu, tváři pak jejich k východu, kteříž klaněli se proti východu slunce.
Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.
17 I řekl mi: Viděl-lis, synu člověčí? Zdali lehká věc jest domu Judovu, aby činili ohavnosti tyto, kteréž činí zde? Nebo naplnivše zemi nátiskem, obrátili se, aby mne popouzeli, a aj, přičinějí ratolest vinnou k nosům svým.
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo!
18 Protož i já také učiním podlé prchlivosti; neslitujeť se oko mé, aniž se smiluji. I budou volati v uši mé hlasem velikým, a nevyslyším jich.
Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”

< Ezechiel 8 >