< Ezechiel 6 >

1 I stalo se ke mně slovo Hospodinovo, řkoucí:
Yehova anandipatsa uthenga uwu kuti,
2 Synu člověčí, obrať tvář svou proti horám Izraelským, a prorokuj proti nim,
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana ku mapiri a Israeli; yankhula nawo modzudzula
3 A rci: Hory Izraelské, slyšte slovo Panovníka Hospodina: Takto praví Panovník Hospodin horám a pahrbkům, prudkým potokům a údolím: Aj, já, já uvedu na vás meč, a zkazím výsosti vaše.
kuti, ‘Inu mapiri a ku Israeli, imvani mawu a Ambuye Yehova. Iye akuwuza mapiri, magomo, mitsinje ndi zigwa kuti: Ine ndizakuthirani nkhondo ndipo ndidzawononga nyumba zanu mʼmene mukupembedzeramo mafano.
4 A tak zpustnou oltářové vaši, a ztroskotáni budou sluneční obrazové vaši, a rozmeci zbité vaše před ukydanými bohy vašimi.
Maguwa anu ansembe adzagumulidwa ndipo maguwa anu ofukizira lubani adzaphwanyidwa; ndipo ndidzapha anthu anu pamaso pa mafano anu.
5 Povrhu také mrtvá těla synů Izraelských před ukydanými bohy jejich, a rozptýlím kosti vaše okolo oltářů vašich.
Ine ndidzagoneka mitembo ya Aisraeli pamaso pa mafano awo, ndipo ndidzamwaza mafupa anu mozungulira maguwa anu ansembe.
6 Kdekoli bydliti budete, města zpuštěna budou, a výsosti zpustnou. Pročež popléněni budou a zpustnou i oltářové vaši, potroskotáni budou a přestanou ukydaní bohové vaši, a sluneční obrazové vaši zpodtínáni, a tak vyhlazena budou díla vaše.
Konse kumene mumakhala, mizinda yanu idzasanduka bwinja. Nyumba zanu zopembedzera mafano zidzagumulidwa kotero kuti maguwa anu adzawonongedwa ndi kusakazidwa, mafano anu adzaphwanyidwa ndi kuwonongedwa. Maguwa anu ofukizirapo lubani adzagwetsedwa pansi ndipo zonse zimene munapanga zidzatheratu.
7 I padnou zbití u prostřed vás, a zvíte, že já jsem Hospodin.
Anthu anu adzaphedwa pakati panu, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
8 A pozůstavím některé z vás, kteříž by ušli meče, mezi pohany, když rozptýleni budete do zemí.
“Komabe ndidzasiya ena pangʼono opulumuka ku nkhondo. Iwowa ndidzawamwazira ku mayiko ena pakati pa anthu a mitundu ina.
9 I budou se rozpomínati na mne, kteříž z vás zachováni budou mezi národy, mezi něž budou zajati, že jsem kormoucen byl srdcem jejich smilným, kteréž odstoupilo ode mne, a očima jejich, kteréž smilníce, chodily za ukydanými bohy svými, a tak sami se býti hodné ošklivosti seznají pro nešlechetnosti, kteréž páchali ve všech ohavnostech svých.
Pamenepo opulumuka mwa inu adzandikumbukira ku mayiko kumene anatengedwa ukapolo. Ndidzawamvetsa chisoni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo ndi kundipandukira kuja ndiponso chifukwa kuti anayika mtima wawo pa mafano. Choncho adzachita okha manyazi chifukwa cha zoyipa zimene ankachita ndi miyambo yonyansa imene ankatsata.
10 A zvědí, že já jsem Hospodin, a že jsem ne nadarmo mluvil, že na ně uvedu zlé toto.
Ndipo iwo adzadziwa kuti ndine Yehova ndi kuti sindinkawaopseza chabe pamene ndinanena kuti ndidzawawononga.
11 Takto praví Panovník Hospodin: Tleskni rukou svou, a dupni nohou svou, a rci: Nastojte na dům Izraelský, že pro všecky ohavnosti nejhorší mečem, hladem a morem padnouti mají.
“Ambuye Yehova akuti: Womba mʼmanja mwako ndipo uponde mapazi ako pansi mwamphamvu ndipo ufuwule kuti, ‘Mayo!’ chifukwa cha zonyansa ndi zoyipa zonse zimene Aisraeli achita, pakuti adzaphedwa ndi lupanga, njala ndi mliri.
12 Ten, kdož daleko bude, morem umře, a kdo blízko, mečem padne, ostatní pak a obležený hladem umře, a tak docela vyleji prchlivost svou na ně.
Amene ali kutali adzafa ndi mliri, ndipo amene ali pafupi adzafa pa nkhondo, ndipo amene adzapulumuke ndi kusaphedwa adzafa ndi njala. Kotero ndidzakwaniritsa ukali wanga pa iwo.
13 A zvíte, že já jsem Hospodin, když budou zbití jejich u prostřed ukydaných bohů jejich vůkol oltářů jejich, na všelikém pahrbku vysokém, na všech vrších hor, a pod všelikým dřevem zeleným, i pod všelikým dubem hustým, na kterémkoli místě obětovávali vůni libou všelikým ukydaným bohům svým.
Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene anthu awo adzagona atafa pakati pa mafano awo mozungulira maguwa awo ansembe, pamwamba pa magomo ndi mapiri onse, pansi pa mtengo uliwonse watambalala ndi wa thundu uliwonse wamasamba ambiri, kumalo kumene ankapereka nsembe zonunkhira kwa mafano awo onse.
14 Nebo vztáhnu ruku svou na ně, a učiním zemi tuto zpustlou, zpustlejší než poušť Diblat, po všech obydlích jejich. I zvědí, že já jsem Hospodin.
Choncho ndidzawalanga ndi mkono wanga ndi kusandutsa dziko kukhala bwinja. Dziko lonse kumene akukhala kuyambira ku chipululu mpaka ku mzinda wa Ribula ndidzalisandutsa bwinja. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezechiel 6 >