< Ezechiel 36 >

1 Ty synu člověčí, prorokuj i o horách Izraelských a rci: Hory Izraelské, slyšte slovo Hospodinovo.
“Iwe mwana wa munthu, yankhula kwa mapiri a Israeli ndipo unene kuti, ‘Inu mapiri a Israeli, imvani mawu a Yehova.’
2 Takto praví Panovník Hospodin: Proto že říká ten nepřítel o vás: Aj, to dobře, takéť i výsosti věčné v dědictví se nám dostanou,
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mdani wanu ankanena kuti, ‘Aa! Dziko lamapiri lakalekale lija lasanduka lathu.’
3 Protož prorokuj a rci: Takto praví Panovník Hospodin: Proto, proto že poplénili a sehltili vás vůkol, abyste byli za dědictví ostatku národů, a vydáni jste v pomluvu a v zlou pověst lidem,
Choncho nenera ndipo uwawuze kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anakusakazani ndi kukuponderezani ku mbali zonse motero kuti munakhala mʼmanja mwa anthu a mitundu ina yonse ndipo anthu ankakunenani ndi kukunyozani,
4 Protož hory Izraelské, slyšte slovo Panovníka Hospodina: Takto praví Panovník Hospodin horám i pahrbkům, potokům i údolím, pustinám hrozným i městům opuštěným, jenž jsou za loupež a posměch ostatku národů okolních,
choncho, inu mapiri a Israeli, imvani zimene Ine Ambuye Yehova ndikuwuza mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa, mabwinja ndi mizinda yosiyidwa imene yakhala ikufunkhidwa komanso kunyozedwa ndi anthu a mitundu ina okuzungulirani.
5 Protož takto dí Panovník Hospodin: jistě že v ohni horlivosti své mluviti budu proti ostatku těch národů, i proti vší zemi Idumejské, kteříž sobě osobili zemi mou za dědictví, veselíce se z celého srdce, a pléníce s chutí, aby sídlo vyhnaných z něho bylo v loupež.
Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mu mkwiyo wanga woopsa ndinayankhula kuyimba mlandu mitundu ina yonse ya anthu makamaka a ku Edomu. Iwowa mwa chimwemwe chodzaza tsaya ndi mwa nkhwidzi analanda dziko langa ndi kulisandutsa lawo ndi kutengeratu dziko la msipu kukhala lawo.’
6 Protož prorokuj o zemi Izraelské, a mluv k horám a pahrbkům, potokům i k údolím: Takto praví Panovník Hospodin: Aj, já v horlivosti své a v prchlivosti své mluvím, proto že pohanění od národů snášíte.
Nʼchifukwa chake, lengeza ku dziko la Israeli, ndipo uwuze mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikuyankhula ndi mtima wokwiya kwambiri chifukwa inu munalandira chitonzo cha anthu a mitundu ina.’
7 Protož takto praví Panovník Hospodin: já zdvihna ruku svou, přisahám, že ti národové, kteříž jsou vůkol vás, pohanění své nésti musejí.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikulumbira nditakweza dzanja langa kuti mitundu ya anthu idzatozedwanso.
8 Vy pak hory Izraelské, ratolesti své vypouštěti, a ovoce své přinášeti budete lidu mému Izraelskému, když se přiblíží a přijdou.
“Koma Inu mapiri a Israeli mudzaphukanso nthambi ndipo mudzawabalira zipatso anthu anga a Israeli, pakuti ali pafupi kubwerera kwawo.
9 Nebo aj, já jsem s vámi, a patřím na vás, abyste dělány a osívány byly.
Taonani, Ine ndili mbali yanu ndipo ndidzakukomerani mtima. Mudzalimidwa ndi kudzalidwa.
10 A rozmnožím v vás lidi, všecken dům Izraelský, jakýžkoli jest, i budou se osazovati města, a pustiny vzdělávati.
Ndidzachulukitsa chiwerengero cha anthu anu, nyumba yonse ya Israeli. Mʼmizinda mudzakhalanso anthu ndipo mabwinja adzamangidwanso.
11 Rozmnožím, pravím, v vás lidi i hovada, a budou se množiti a ploditi, i učiním, že bydliti budete jako za předešlých let vašich, čině vám dobře, více než v prvotinách vašich. A zvíte, že já jsem Hospodin.
Ndidzachulukitsa chiwerengero cha amuna pamodzi ndi ziweto zomwe, ndipo adzachuluka kwambiri ndi kubereka ana ambiri. Ndidzakhazika anthu mʼdzikomo monga analili kale, ndi kukulemeretsani kuposa kale. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
12 Nebo uvedu do vás lidi, lid svůj Izraelský, a budou tebou dědičně vládnouti; a budeš jim za dědictví, aniž kdy více siroby na ně uvedeš.
Ndidzachititsa anthu kuyenda pa inu, ndiye kuti inu anthu anga Aisraeli. Iwowo adzakhazikika pa inu, ndipo inu mudzakhala cholowa chawo. Simudzalandanso ana awo.
13 Takto praví Panovník Hospodin: Proto že říkají vám, že jsi ty ta země, kteráž zžíráš lidi, a sirotky činíš z národů svých,
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anthu amanena kuti, ndiwe dziko limene limadya anthu ake ‘kulanda ana a mtundu wake,’
14 Protož nebudeš více zžírati lidi, a národů svých více k sirobě přivoditi, praví panovník Hospodin.
nʼchifukwa chake, simudzadyanso anthu kapena kulanda ana a mtundu wako. Ine Ambuye Yehova ndikutero.
15 Aniž dopustím, aby více slýcháno bylo v tobě potupy národů, aniž útržky lidské snášeti budeš více, ani ku pádu přivoditi více národů svých, praví Panovník Hospodin.
Sindidzakulolaninso kumva mnyozo wa anthu a mitundu ina, kapena kupirira kunyogodola kwawo kapenanso kupunthwitsanso anthu a mʼdziko lako. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
16 I stalo se slovo Hospodinovo ke mně, řkoucí:
Yehova anandiyankhulanso kuti:
17 Synu člověčí, dům Izraelský, bydlíce v zemi své, poškvrnili jí cestou svou a skutky svými; podobná nečistotě ženy pro nečistotu oddělené byla cesta jejich před očima mýma.
“Iwe mwana wa munthu, pamene anthu a Israeli ankakhala mʼdziko lawolawo, analiyipitsa ndi makhalidwe awo ndiponso zochita zawo. Machitidwe awo pamaso panga anali onyansa pa zachipembedzo ngati msambo wa mkazi amene ali pa nthawi yake.
18 Pročež vylil jsem prchlivost svou na ně, proto že krev vylévali na zemi, a ukydanými bohy svými poškvrnili jí.
Tsono ndinawalanga chifukwa cha magazi amene anakhetsa mʼdzikomo, ndiponso chifukwa anayipitsa dziko ndi mafano awo.
19 I rozptýlil jsem je po národech, tak že rozplašeni jsou po zemích; podlé cesty jejich a podlé skutků jejich soudil jsem je.
Ndinawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndipo anabalalikira mʼmayiko onse. Ndinawalanga molingana ndi makhalidwe awo ndi zochita zawo.
20 Nýbrž odšedše mezi národy, kamž přišli, poškvrnili jména svatosti mé, když říkáno o nich: Že jsou lid Hospodinův, a že z jeho země vyšli.
Atafika kwa anthu a mitundu ina, kulikonse kumene anapitako, anayipitsa dzina langa loyera. Zinatero popeza anthu ponena za iwo ankanena kuti, ‘Awa ndi anthu a Yehova, komatu anachotsedwa ku dziko lake.’
21 Ale slitoval jsem se pro jméno svatosti své, kteréhož poškvrnili dům Izraelský mezi národy, kamž přišli.
Koma Ine ndinkadera nkhawa dzina langa loyera, limene Aisraeli analiyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapitako.
22 Protož rci domu Izraelskému: Takto praví Panovník Hospodin: Ne pro vás já to učiním, ó dome Izraelský, ale pro jméno svatosti své, kteréhož jste poškvrnili mezi národy, kamž jste přišli,
“Nʼchifukwa chake awuze Aisraeliwo kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndidzachita zimene ndidzachitezo osati chifukwa cha inuyo Aisraelinu ayi, koma chifukwa cha dzina langa, limene mwaliyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene munapitako.
23 Abych posvětil jména svého velikého, kteréž bylo poškvrněno mezi národy, kteréhož jste poškvrnili u prostřed nich, aby poznali národové, že já jsem Hospodin, praví Panovník Hospodin, když posvěcen budu v vás před očima jejich.
Ndidzaonetsa chiyero cha dzina langa lotchuka, limene layipitsidwa pakati pawo. Anthu a mitundu inayo atadzazindikira kuti ndaonetsa kudzera mwa inu kuti dzina langa ndi loyera, iwo adzadziwanso kuti Ine ndine Yehova. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
24 Nebo poberu vás z národů, a shromáždím vás ze všech zemí, a uvedu vás do země vaší.
“Pakuti Ine ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina. Ndidzakusonkhanitsani kuchoka ku mayiko onse ndi kukubwezerani ku dziko lanulanu.
25 A pokropím vás vodou čistou, a čisti budete; ode všech poškvrn vašich, i ode všech ukydaných bohů vašich očistím vás.
Ndidzakuwazani madzi oyera, ndipo mudzakhala oyera mtima. Zonse zimene zimakuyipitsani zidzachoka. Ndidzakuyeretsani pochotsa mafano anu onse.
26 A dám vám srdce nové, a ducha nového dám do vnitřností vašich, a odejma srdce kamenné z těla vašeho, dám vám srdce masité.
Ndidzakupatsani mtima watsopano ndi kulowetsa mzimu watsopano mwa inu. Ndidzachotsa mwa inu mtima wanu wowuma ngati mwala ndi kukupatsani mtima wofewa ngati mnofu.
27 Ducha svého, pravím, dám do vnitřností vašich, a učiním, abyste v ustanoveních mých chodili, a soudů mých ostříhali a činili je.
Ndipo ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo ndidzakuthandizani kutsatira malangizo anga ndi kukusungitsani mosamala kwambiri malamulo anga.
28 I budete bydliti v zemi, kterouž jsem byl dal otcům vašim, a budete lidem mým, a já budu vaším Bohem.
Mudzakhala mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu. Mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
29 Nebo vysvobodím vás ze všelijakých poškvrn vašich, a přivolám obilé, a rozmnožím je, a nedopustím na vás hladu.
Ndidzakupulumutsani ku zonse zokuyipitsani. Ndidzakuchulukitsirani tirigu ndipo sindidzakugwetseraninso njala.
30 Rozmnožím i ovoce stromů a úrody polní, tak že neponesete více potupy hladu mezi národy.
Ndidzachulukitsa zipatso za mʼmitengo yanu ndi zokolola za mʼmunda mwanu, kotero kuti simudzanyozedwanso pakati pa anthu a mitundu ina chifukwa cha njala.
31 I rozpomenete se na zlé cesty vaše a na skutky vaše nedobré, tak že sami se býti hodné ošklivosti uznáte pro nepravosti vaše a pro ohavnosti vaše.
Pamenepo mudzakumbukira makhalidwe anu oyipa ndi ntchito zanu zoyipa. Machimo anu ndi ntchito zanu zonyansa zidzakuchititsa nokha manyazi.
32 Ne pro vás já to učiním, praví Panovník Hospodin, známo vám buď. Zahanbětež se a zastyďte za cesty své, dome Izraelský.
Tsono dziwani kuti Ine sindidzachita zimenezi chifukwa cha inuyo ayi, ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse. Ndiyetu chitani manyazi ndipo mugwetse nkhope zanu, inu Aisraeli chifukwa cha makhalidwe anu!
33 Takto praví Panovník Hospodin: V ten den, v kterémž vás očistím ode všech nepravostí vašich, osadím města, a vzdělány budou pustiny.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limene ndidzayeretse machimo anu onse, ndidzayikamonso anthu mʼmizinda yanu, ndipo ndidzamanganso nyumba pa mabwinja.
34 A tak země pustá bude dělána, kteráž prvé byla pouští před očima každého tudy jdoucího.
Dziko limene linasanduka chipululu lizidzalimidwanso. Mʼmalo moti aliyense wopitamo alione dzikolo ngati chipululu tsopano adzaliona lolimidwa.
35 I řeknou: Země tato zpuštěná jest jako zahrada Eden, ano i města pustá, zkažená a zbořená jsou ohrazena a osazena.
Iwo adzati, ‘Dziko ili, limene linali chipululu, lasanduka munda wa Edeni. Mizinda imene inali mabwinja osiyidwa ndi owonongedwa, tsopano ndi yotetezedwa ndi yokhalamo anthu.
36 I zvědí národové, kteříž pozůstanou vůkol vás, že já Hospodin vystavěl jsem zbořeniny, a vysadil pustiny. Já Hospodin mluvil jsem i učiním.
Ndipo anthu a mitundu ina okhala pafupi nanu amene anatsala adzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndinamanganso mizinda yowonongeka ndi kudzalanso zinthu zatsopano mʼmalo mʼmene munali chipululu. Ine Yehova ndayankhula ndipo ndidzazichitadi.’
37 Takto praví Panovník Hospodin: Ještě toho hledati bude při mně dům Izraelský, abych je rozmnožil. Rozmnožím je lidmi jako stády.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzalolanso Aisraeli kuti andipemphe zoti ndiwachitire: Ndidzachulukitsa anthu awo ngati nkhosa.
38 Jako stádo k obětem, jako stádo Jeruzalémské při slavnostech jeho, tak města pustá budou plná stád lidí, i zvědí, že já jsem Hospodin.
Adzachulukadi ngati nkhosa zomwe ankapereka ngati nsembe ku Yerusalemu pa nthawi za chikondwerero. Choncho mizinda ya mabwinja idzadzaza ndi anthu. Zikadzatero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezechiel 36 >