< Kazatel 8 >

1 Kdo se může vrovnati moudrému, a kdo může vykládati všelikou věc? Moudrost člověka osvěcuje oblíčej jeho, a nestydatost tváři jeho proměňuje.
Ndani angafanane ndi munthu wanzeru? Ndani angadziwe kutanthauzira zinthu? Nzeru imabweretsa chimwemwe pa nkhope ya munthu ndipo imasintha maonekedwe ake awukali.
2 Jáť radím: Výpovědi královské ostříhej, a však podlé přísahy Boží.
Ine ndikuti, mvera lamulo la mfumu, chifukwa unalumbira pamaso pa Mulungu.
3 Nepospíchej odjíti od tváři jeho, aniž trvej v zpouře; nebo cožť by koli chtěl, učinil by.
Usafulumire kuchoka pamaso pa mfumu. Usawumirire chinthu choyipa, pakuti mfumu idzachita chilichonse chomwe imasangalatsidwa nacho.
4 Nebo kde slovo královské, tu i moc jeho, a kdo dí jemu: Co děláš?
Popeza mawu a mfumu ali ndi mphamvu, ndani anganene kwa mfumuyo kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
5 Kdo ostříhá přikázaní, nezví o ničem zlém. I čas i příčiny zná srdce moudrého.
Aliyense amene amamvera lamulo lake sadzapeza vuto lililonse, ndipo munthu wanzeru amadziwa nthawi yoyenera ndi machitidwe ake.
6 Nebo všeliké předsevzetí má čas a příčiny. Ale i to neštěstí veliké člověka se přídrží,
Pakuti pali nthawi yoyenera ndiponso machitidwe a chinthu chilichonse, ngakhale kuti mavuto ake a munthu amupsinja kwambiri.
7 Že neví, co budoucího jest. Nebo jak se stane, kdo mu oznámí?
Popeza palibe munthu amene amadziwa zamʼtsogolo, ndani angamuwuze zomwe zidzachitika mʼtsogolo?
8 Není člověka, kterýž by moci měl nad životem, aby zadržel duši, aniž má moc nade dnem smrti; nemá ani braně v tom boji, aniž vysvobodí bezbožnost bezbožného.
Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.
9 Ve všem tom viděl jsem, přiloživ mysl svou ke všemu tomu, co se děje pod sluncem, že časem panuje člověk nad člověkem k jeho zlému.
Zonsezi ndinaziona pamene ndinalingalira mu mtima mwanga, zonse zimene zimachitika pansi pano. Ilipo nthawi imene ena amalamulira anzawo mwankhanza.
10 A tehdáž viděl jsem bezbožné pohřbené, že se zase navrátili, ale kteříž z místa svatého odešli, v zapomenutí dáni jsou v městě tom, v kterémž dobře činili. I to také jest marnost.
Kenaka, ndinaona anthu oyipa akuyikidwa mʼmanda, iwo amene ankalowa ndi kumatuluka mʼmalo opatulika ndipo ankatamandidwa mu mzindawo pamene ankachita zimenezi. Izinso ndi zopandapake.
11 Nebo že ne i hned ortel dochází pro skutek zlý, protož vroucí jest k tomu srdce synů lidských, aby činili zlé věci.
Pamene chigamulo cha anthu opalamula mlandu chikuchedwa, mitima ya anthu imadzaza ndi malingaliro ochita zolakwa.
12 A ačkoli hříšník činí zle na stokrát, a vždy se mu odkládá, já však vím, že dobře bude bojícím se Boha, kteříž se bojí oblíčeje jeho.
Ngakhale munthu woyipa apalamule milandu yambirimbiri, nʼkumakhalabe ndi moyo wautali, ine ndikudziwa kuti anthu owopa Mulungu zinthu zidzawayendera bwino, omwe amapereka ulemu pamaso pa Mulungu.
13 S bezbožným pak nedobře se díti bude, aniž se prodlí dnové jeho; minou jako stín, proto že jest bez bázně před oblíčejem Božím.
Koma popeza oyipa saopa Mulungu zinthu sizidzawayendera bwino, ndipo moyo wawo sudzakhalitsa monga mthunzi.
14 Jest marnost, kteráž se děje na zemi: Že bývají spravedliví, jimž se však vede, jako by činili skutky bezbožných; zase bývají bezbožní, kterýmž se však vede, jako by činili skutky spravedlivých. Protož jsem řekl: I to také jest marnost.
Palinso chinthu china chopanda phindu chomwe chimachitika pa dziko lapansi: anthu olungama amalangidwa ngati anthu osalungama. Pamene oyipa amalandira zabwino ngati kuti ndi anthu abwino.
15 A tak chválil jsem veselí, proto že nic nemá lepšího člověk pod sluncem, jediné aby jedl a pil, a veselil se, a že to pozůstává jemu z práce jeho ve dnech života jeho, kteréž dal jemu Bůh pod sluncem.
Nʼchifukwa chake ndikuti munthu azikondwerera moyo, pakuti munthu alibe chinanso chabwino pansi pano choposa kudya, kumwa ndi kumadzikondweretsa. Akamatero, munthuyo adzakhala ndi chimwemwe pa ntchito yake masiku onse a moyo wake amene Mulungu wamupatsa pansi pano.
16 A ač jsem se vydal srdcem svým na to, abych moudrost vystihnouti mohl, a vyrozuměti bídě, kteráž bývá na zemi, pro kterouž ani ve dne ani v noci nespí,
Pamene ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe nzeru ndi kuonetsetsa ntchito za munthu pa dziko lapansi, osapeza tulo usana ndi usiku,
17 A však viděl jsem při každém skutku Božím, že nemůže člověk vystihnouti skutku dějícího se pod sluncem. O čež pracuje člověk, vyhledati chtěje, ale nenalézá; nýbrž byť i myslil moudrý, že se doví, nebude moci nic najíti.
pamenepo ndinaona zonse zimene Mulungu anazichita. Palibe munthu amene angathe kuzimvetsa zonse zimene zimachitika pansi pano. Ngakhale munthu ayesetse kuzifufuza, sangathe kupeza tanthauzo lake. Ngakhale munthu wanzeru atanena kuti iye amadziwa, sangathe kuzimvetsetsa zinthuzo.

< Kazatel 8 >