< Pieseò 1 >

1 Píseň nejpřednější z písní Šalomounových.
Nyimbo ya Solomoni, nyimbo yoposa nyimbo zonse.
2 Ó by mne políbil políbením úst svých; nebo lepší jsou milosti tvé nežli víno.
Undipsompsone ndi milomo yako chifukwa chikondi chako nʼchokoma kuposa vinyo.
3 Pro vůni masti tvé jsou výborné, mast rozlitá jméno tvé; protož tě mladice milují.
Mafuta ako odzola ndi onunkhira bwino; dzina lako lili ngati mafuta onunkhira otsanulidwa. Nʼchifukwa chake atsikana amakukonda!
4 Táhniž mne, a poběhnem za tebou. Uvedltě mne král do pokojů svých, plésati a veseliti se v tobě budeme, a vychvalovati milosti tvé více než víno; upřímí milují tě.
Nditenge ndipo ndizikutsata, tiye tifulumire! Mfumu indilowetse mʼchipinda chake. Abwenzi Ife timasangalala ndi kukondwera nawe, tidzatamanda chikondi chako kupambana vinyo. Mkazi Amachita bwinotu potamanda iwe!
5 Jsemť černá, ale milostná, ó dcery Jeruzalémské, tak jako stanové Cedarští, jako opony Šalomounovy.
Ndine wakuda, komatu ndine wokongola, inu akazi a ku Yerusalemu, ine ndine wakuda ngati tenti ya ku Kedara, ngati makatani a tenti ya Solomoni.
6 Nehleďte na mne, žeť jsem snědá, nebo jsem obhořela od slunce. Synové matky mé rozpálivše se proti mně, postavili mne, abych ostříhala vinic, a vinice své nehlídala jsem.
Musandiyangʼane monyoza chifukwa ndine wakuda, ndine wakuda chifukwa cha dzuwa. Alongo anga anandikwiyira ndipo anandigwiritsa ntchito mʼminda ya mpesa; munda wangawanga sindinawusamalire.
7 Oznam mi ty, kteréhož miluje duše má, kde paseš? Kde dáváš odpočinutí o poledni? Nebo proč mám býti tak jako poběhlá při stádích tovaryšů tvých?
Ndiwuze iwe, amene ndimakukonda, kumene umadyetsa ziweto zako ndi kumene umagoneka nkhosa zako nthawi yamasana. Ndikhalirenji ngati mkazi wachiwerewere pambali pa ziweto za abwenzi ako?
8 Jestliže nevíš, ó nejkrašší mezi ženami, vyjdi po šlepějích ovcí, a pas kozlátka svá podlé obydlí pastýřů.
Ngati sukudziwa iwe wokongola kwambiri kuposa akazi ena, ngati sukudziwa, tsatira makwalala a nkhosa ndipo udyetse ana ambuzi pambali pa matenti a abusa.
9 Jízdě v vozích Faraonových připodobňuji tě, ó milostnice má.
Iwe bwenzi langa, uli ngati kavalo wamkazi ku magaleta a Farao.
10 Líce tvá okrášlena jsou ozdobami, a hrdlo tvé halžemi.
Masaya ako ndi okongola ndi ndolo zamʼmakutuzo, khosi lako likukongola ndi mikanda yamiyala yamtengowapatali.
11 Ozdob zlatých naděláme tobě s proměnami stříbrnými.
Tidzakupangira ndolo zagolide zokongoletsedwa ndi mikanda yasiliva.
12 Dotud, dokudž král stolí, nardus můj vydává vůni svou.
Pamene mfumu inali pa malo ake odyera, mafuta anga onunkhira anamveka fungo lake.
13 Svazček mirry jest mi milý můj, na prsech mých odpočívaje.
Wokondedwa wanga ali ngati kathumba ka mure kwa ine, kamene kamakhala pakati pa mawere angawa.
14 Milý můj jest mi hrozen cyprový na vinicích v Engadi.
Wokondedwa wanga ali ngati mpukutu wa maluwa ofiira, ochokera ku minda ya mpesa ya ku Eni-Gedi.
15 Aj, jak jsi ty krásná, přítelkyně má, aj, jak jsi krásná! Oči tvé jako holubičí.
Iwe wokondedwa wanga, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe chiphadzuwa, maso ako ali ngati nkhunda.
16 Aj, jak jsi ty krásný, milý můj, jak utěšený! I to lůže naše zelená se.
Iwe bwenzi langa, ndiwe wokongoladi! Ndithu, ndiwe wokongoladi kwambiri! Ndipo malo athu ogonapo ndi msipu wobiriwira.
17 Trámové domů našich jsou z cedrů, a pavlače naše z boroví.
Mitanda ya nyumba yathu ndi ya mkungudza, phaso lake ndi la mtengo wa payini.

< Pieseò 1 >