< Zefaniya 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.
Ilizwi likaThixo elafika kuZefaniya indodana kaKhushi, indodana kaGedaliya, indodana ka-Amariya, indodana kaHezekhiya, ekubuseni kukaJosiya indodana ka-Amoni inkosi yakoJuda:
2 “Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse pa dziko lapansi,” akutero Yehova.
“Ngizakhucula konke ebusweni bomhlaba,” kutsho uThixo.
3 “Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe; ndidzawononga mbalame zamlengalenga ndi nsomba za mʼnyanja. Ndidzawononga anthu oyipa, ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.
“Ngizakhucula kokubili abantu lezinyamazana; ngizakhucula izinyoni zasemoyeni kanye lenhlanzi zasolwandle, lezithombe ezenza ababi bakhubeke. Lapho ngiqeda abantu ebusweni bomhlaba,” kutsho uThixo.
4 Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda ndi onse okhala mu Yerusalemu. Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala, mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
“Ngizakwelulela isandla sami koJuda lakubo bonke abahlala eJerusalema. Ngizaqeda konke okukaBhali okuseleyo kule indawo, amabizo abahedeni labaphristi abakhonza izithombe
5 amene amagwada pa madenga a nyumba zawo kupembedza zolengedwa zamumlengalenga, amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova, komanso mʼdzina la Moleki,
labo abakhothama phezu kwezindlu bakhonze ixuku lezinkanyezi, labo abakhothama bafunge ngoThixo, abafunga langoMoleki futhi,
6 amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova, osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
labo ababuyela emuva bedela ukulandela uThixo njalo abangamdinganga uThixo loba babuze ngaye.
7 Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova, chifukwa tsiku la Yehova layandikira. Yehova wakonzekera kupereka nsembe; wapatula iwo amene wawayitana.
Thula phambi kukaThixo Wobukhosi, ngoba usuku lukaThixo seluseduze. UThixo uselungise umhlatshelo; usebangcwelisile labo abanxusileyo.
8 Pa tsiku la nsembe ya Yehova ndidzalanga akalonga ndi ana aamuna a mfumu ndi onse amene amavala zovala zachilendo.
Ngosuku lomhlatshelo kaThixo ngizajezisa izikhulu lamadodana amakhosi labo bonke labo abagqoke izigqoko zezizweni.
9 Pa tsiku limenelo ndidzalanga onse amene safuna kuponda pa chiwundo, amene amadzaza nyumba ya ambuye awo ndi chiwawa ndi chinyengo.
Ngalolosuku ngizabajezisa bonke abaxwaya ukunyathela umbundu womnyango, abagcwalisa ithempeli labonkulunkulu babo ngodlakela langenkohliso.”
10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova, “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba, kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano, ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
UThixo, uthi, “Ngalolosuku ilizwi lokukhala lizaqonga ngaseSangweni leNhlanzi, ukulila kuvelela esiGabeni eSitsha lomsindo omkhulu wokufohloza uvela emaqaqeni.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika; a malonda anu onse adzapululidwa, ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
Lilani lina elihlala esigodini sokuthengisela saseMakhithashi, bonke abathengisi benu bazaqedwa, bonke abathengiselana ngesiliva bazabhujiswa.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale ndi kulanga onse amene sakulabadira, amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa, amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse, chabwino kaya choyipa.’
Ngalesosikhathi ngizaphenya iJerusalema ngezibane ngijezise labo abangakhathaliyo, abanjengewayini elitshiywe phakathi kwensipho zalo, abathi, ‘UThixo kayikwenza lutho, oluhle loba olubi.’
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa, nyumba zawo zidzagwetsedwa. Adzamanga nyumba, koma osakhalamo; adzadzala minda ya mpesa koma sadzamwako vinyo wake.”
Inotho yabo izaphangwa, izindlu zabo zidilizwe. Bazakwakha izindlu kodwa bangahlali kuzo; bazahlanyela izivini, kodwa iwayini bangalinathi.”
14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira, layandikira ndipo lifika msanga. Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa, ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
Usuku olukhulu lukaThixo seluseduze, njalo luza ngokuphangisa. Lalelani! Ukukhala ngosuku lukaThixo kuzakuba buhlungu, lokuklabalala kwebutho khonapho.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali, tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni, tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko, tsiku la mdima ndi lachisoni, tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
Lolosuku luzakuba lusuku lolaka, usuku losizi lokudabuka; usuku lokuhlupheka lokuchitheka, usuku lomnyama lokudana, usuku lwamayezi lobumnyama,
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo, tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa ndi nsanja za pa ngodya.
usuku lwecilongo lokuhlaba umkhosi wokulwa impi lamadolobho avikelweyo kanye lezinqaba zasemajikweni.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu ndipo adzayenda ngati anthu osaona, chifukwa achimwira Yehova, magazi awo adzamwazika ngati fumbi ndi mnofu wawo ngati ndowe.
“Ngizaletha usizi ebantwini njalo bazahamba njengeziphofu, ngoba bonile kuThixo. Igazi labo lizachithwa njengothuli lezibilini zabo njengamanyala.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo sadzatha kuwapulumutsa pa tsiku la ukali wa Yehova. Dziko lonse lapansi lidzanyeka mʼmoto wa nsanje yake chifukwa adzakantha modzidzimutsa onse okhala pa dziko lapansi.
Isiliva sabo loba igolide labo kakungeke kwenelise ukubasindisa ngosuku lolaka lukaThixo. Umhlaba wonke uzatshiswa emlilweni womona wakhe ngoba uzakwenza isiphetho ngokuphangisa kubo bonke abahlala emhlabeni.”

< Zefaniya 1 >