< Zefaniya 2 >

1 Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi, inu mtundu wochititsa manyazi,
Buthanani ndawonye, buthanani ndawonye, wena sizwe esiyangisayo,
2 isanafike nthawi yachiweruzo, nthawi yanu isanawuluke ngati mungu, usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova, tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.
isikhathi esimisiweyo singakafiki losuku ludlule njengamakhoba, ukuthukuthela okwesabekayo kukaThixo kungakafiki kuwe, usuku lolaka lukaThixo lungakafiki kuwe.
3 Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko, inu amene mumachita zimene amakulamulani. Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa; mwina mudzatetezedwa pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.
Dingani uThixo, lonke lina abathobekileyo belizwe, lina elenza lokho akulayayo. Dingani ukulunga, dingani ukuthobeka; mhlawumbe lingavikelwa ngosuku lwentukuthelo kaThixo.
4 Gaza adzasiyidwa ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja. Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu ndipo Ekroni adzazulidwa.
IGaza izadelwa le-Ashikheloni isale isingamanxiwa. Abantu base-Ashidodi bazaxotshwa emini, le-Ekroni isitshulwe.
5 Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu mtundu wa Akereti; mawu a Yehova akutsutsa iwe Kanaani, dziko la Afilisti. “Ndidzakuwononga ndipo palibe amene adzatsale.”
Maye kini lina elihlala ngasolwandle, lina sizwe samaKherethi; ilizwi likaThixo limelana lani, wena Khenani, lizwe lamaFilistiya. “Ngizakutshabalalisa, njalo kakho ozasala.”
6 Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti, lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.
Ilizwe elingasolwandle lizakuba yindawo yabelusi lezibaya zezimvu.
7 Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda; adzapezako msipu. Nthawi ya madzulo adzagona mʼnyumba za Asikeloni. Yehova Mulungu wawo adzawasamalira; adzabwezeretsa mtendere wawo.
Ilizwe lizakuba ngelabaseleyo abendlu kaJuda; bazathola amadlelo khona. Kusihlwa bazalala phansi ezindlini zase-Ashikheloni. UThixo uNkulunkulu wabo uzabalondoloza; uzabenza baphumelele futhi.
8 “Ndamva kunyoza kwa Mowabu ndi chipongwe cha Amoni, amene ananyoza anthu anga ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.
“Ngizizwile izithuko zeMowabi lokuchothoza kwama-Amoni, abathuka abantu bami besongela lelizwe labo.
9 Choncho, pali Ine Wamoyo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, “Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu, Amoni adzasanduka ngati Gomora; malo a zomeramera ndi maenje a mchere, dziko la bwinja mpaka muyaya. Anthu anga otsala adzawafunkha; opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”
Ngakho ngeqiniso elinjengoba ngikhona,” kutsho uThixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli, “impela iMowabi izakuba njengeSodoma, ama-Amoni abe njengeGomora, indawo yokhula lemigodi yetshwayi, ilizwe elichithekileyo nini lanini. Abaseleyo babantu bami bazabaphanga; abaphephileyo babantu bami bazathatha ilizwe labo.”
10 Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo, chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.
Lokhu yikho abazakuthola kungumvuzo wokuzigqaja kwabo, ngenxa yokuthuka lokuklolodela abantu bakaThixo uSomandla.
11 Yehova adzawachititsa mantha kwambiri pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo. Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira, uliwonse ku dziko la kwawo.
UThixo uzakwesabeka kubo lapho esetshabalalisa bonke onkulunkulu belizwe. Izizwe ezisemakhunjini wonke zizamkhonza, ngulowo elizweni lakhe.
12 “Inunso anthu a ku Kusi, mudzaphedwa ndi lupanga.”
“Lani futhi, lina maKhushi lizabulawa ngenkemba yami.”
13 Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto ndi kuwononga Asiriya, kusiya Ninive atawonongekeratu ndi owuma ngati chipululu.
Uzakwelulela isandla sakhe enyakatho achithe i-Asiriya, atshiye iNiniva itshabalele ngokupheleleyo njalo yome njengenkangala.
14 Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko, pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse. Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu adzakhala pa nsanamira zake. Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera, mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha, nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.
Imihlambi yezimvu leyenkomo izalala phansi khonapho, lezidalwa zezinhlobo zonke. Isikhova senkangala lomandukulo kuzahlala ensikeni zakhe. Ukukhala kwazo kuzezwakala emawindini, imfucuza izakuba eminyango, imijabo yemisedari ichayeke.
15 Umenewu ndiye mzinda wosasamala umene kale unali wotetezedwa. Unkanena kuti mu mtima mwake, “Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.” Taonani lero wasanduka bwinja, kokhala nyama zakutchire! Onse owudutsa akuwunyoza ndi kupukusa mitu yawo.
Leli lidolobho elingakhathaliyo elalizihlalele livikelekile. Lazitshela lathi: “Ngiyimi, kakho omunye ngaphandle kwami.” Yeka ukuchitheka eseliyikho, isikhundla sezinyamazana zeganga! Bonke abadlula kulo bahleka usulu balikhombe ngeminwe.

< Zefaniya 2 >