< Zekariya 2 >
1 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona munthu atanyamula chingwe choyezera mʼmanja mwake.
Ngaphakamisa amehlo, phambi kwami kwakulomuntu ophethe intambo yokulinganisa!
2 Ndipo ndinafunsa kuti, “Kodi ukupita kuti?” Anandiyankha kuti, “Akukayeza Yerusalemu kuti ndidziwe mulifupi mwake ndi mulitali mwake.”
Ngabuza ngathi, “Uya ngaphi na?” Wangiphendula wathi, “Ngiyalinganisa iJerusalema, ukubona ukuthi ibanzi njalo inde kanganani.”
3 Taonani, mngelo amene amayankhula nane uja akuchoka, mngelo wina anabwera kudzakumana naye
Ingilosi leyo eyayikhuluma lami yasisuka, kweza enye ingilosi iyihlangabeza
4 ndipo anamuwuza kuti, “Thamanga, kamuwuze mnyamatayo kuti, ‘Yerusalemu udzakhala mzinda wopanda malinga chifukwa mudzakhala anthu ambiri ndiponso ziweto zochuluka.
yathi kuyo: “Gijima utshele ijaha leliyana uthi, ‘IJerusalema izakuba lidolobho elingelamiduli ngenxa yobunengi babantu lezifuyo phakathi kwalo.
5 Ndipo Ine mwini ndidzakhala linga lamoto kuteteza mzindawo,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakhala ulemerero mʼkati mwake.’
Mina ngokwami ngizakuba ngumduli womlilo olizungezileyo,’ kutsho uThixo, ‘njalo ngizakuba yinkazimulo ngaphakathi kwalo.’
6 “Tulukani! Tulukani! Thawaniko ku dziko la kumpoto,” akutero Yehova, “pakuti ndinakumwazirani ku mphepo zinayi zamlengalenga,” akutero Yehova.
Wozani! Wozani! Balekani kulelolizwe lasenyakatho,” kutsho uThixo, “ngoba ngilichithachithile kuyo yonke imimoya yomine yezulu,” kutsho uThixo.
7 “Tuluka, iwe Ziyoni! Thawa, iwe amene umakhala mʼdziko la mwana wamkazi wa Babuloni!”
“Woza, yeyi wena Ziyoni! Balekani lina elihlala eNdodakazini yaseBhabhiloni!”
8 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Atatha kundilemekeza wanditumiza kwa anthu a mitundu ina amene anakufunkhani; pakuti aliyense wokhudza inu wakhudza mwanadiso wanga.
Ngoba lokhu kutshiwo nguThixo uSomandla, uthi: “Ngemva kokuba Olodumo esengithumile ukumelana lezizwe eziliphangileyo ngoba loba ngubani oke alithinte lina uthinta igugu lakhe
9 Ndithu Ine ndidzawamenya anthuwo ndi dzanja langa ndipo amene anali akapolo awo ndiye adzawalande zinthu. Pamenepo mudzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye wandituma.
ngempela ngizaphakamisela isandla sami kubo ukuze izigqili zabo zibaphange. Lapho-ke lizakwazi ukuthi uThixo uSomandla nguye ongithumileyo.
10 “Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, fuwula ndipo sangalala. Pakuti taona ndikubwera, ndipo ndidzakhala pakati pako,” akutero Yehova.
Memeza ujabule, we Ndodakazi yaseZiyoni. Ngoba ngiyeza, njalo ngizahlala phakathi kwenu,” kutsho uThixo.
11 “Nthawi imeneyo anthu a mitundu yambiri adzabwera kwa Yehova ndipo adzasanduka anthu anga. Ndidzakhala pakati pako ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe.
“Izizwe ezinengi zizahlanganiswa loThixo ngalelolanga njalo zizakuba ngabantu bami. Ngizahlala phakathi kwenu njalo lizakwazi ukuthi uThixo uSomandla ungithumile kini.
12 Yehova adzachititsa kuti Yuda akhale chuma chake mʼdziko lopatulika ndipo adzasankhanso Yerusalemu.
UThixo uzamthatha uJuda njengelifa abe yisabelo sakhe elizweni elingcwele njalo uzaphinda ayikhethe iJerusalema.
13 Khalani chete pamaso pa Yehova anthu nonse, chifukwa Iye wavumbuluka kuchoka ku malo ake opatulika.”
Pholani lithule phambi kukaThixo, bantu lonke, ngoba uphakamile waphuma endaweni yakhe engcwele.”