< Malaki 1 >

1 Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
Isiphrofethi, Ilizwi likaThixo ku-Israyeli ngoMalaki.
2 Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
“Ngilithandile,” kutsho uThixo. “Kodwa liyabuza lithi, ‘Usithande njani?’” UThixo uthi, “U-Esawu wayengasimfowabo kaJakhobe na? Yebo uJakhobe ngimthandile,
3 koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
kodwa u-Esawu ngimzondile, futhi ngenze izintaba zakhe zaba lugwadule lelifa lakhe ladliwa ngamakhanka asenkangala.”
4 Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
U-Edomi angathi, “Kungaze kube sinyathezelwe phansi kodwa sizawavuselela amanxiwa.” Kodwa nanku okutshiwo nguThixo uSomandla, uthi: “Bangakha, kodwa ngizadiliza. Bazakuthiwa Yilizwe Elibi, abantu abazahlala bethukuthelelwe nguThixo.
5 Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
Lizakubona ngawenu amehlo lithi, ‘Umkhulu uThixo, angale kwemingcele yako-Israyeli!’”
6 “Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
“Indodana iyamesaba uyise, lenceku iyayesaba inkosi yayo. Aluba nginguyihlo kungaphi pho ukwesatshwa kwami? Aluba ngiyinkosi kungaphi ukuhlonitshwa kwami na?” kutsho uThixo uSomandla. “Yini, hawu baphristi, eleyisa ibizo lami. Kodwa lingabuza lithi, ‘Sileyise ngani ibizo lakho?’
7 “Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
Libeka ukudla okungcolileyo e-alithareni lami. Kodwa lingabuza lithi, ‘Sikungcolise kanjani wena na?’ Ngokuthi itafula likaThixo liyeyiseka.
8 Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Nxa liletha izifuyo eziyiziphofu ukuba ngumhlatshelo, kambe kakukubi lokho na? Nxa lisenza umhlatshelo ngezifuyo eziyizilima loba ezilezifo, kakukubi lokho na? Ake lizame ukukunika umbusi wenu! Angalithabela lina na? Angalithanda kambe lina yini?” kutsho uThixo uSomandla.
9 “Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
“Ngakho-ke ncengani uNkulunkulu ukuthi abe lobubele kithi. Ngeminikelo enjalo ephuma ezandleni zenu, kambe angalamukela?” kutsho uThixo uSomandla.
10 “Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
“Oh, sekuze kungathi omunye wenu angavala iminyango yethempeli ukuze lingabi lilokhu libasa imililo engelamsebenzi e-alithareni lami! Kangithokozi ngani lina,” kutsho uThixo uSomandla, “njalo kangiyikwamukela umnikelo wezandla zenu.
11 Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Ibizo lami lizaba likhulu phakathi kwezizwe, kusukela ekuphumeni kwelanga kusiya ekutshoneni kwalo. Ezindaweni zonke impepha leminikelo ehlanzekileyo izalethwa ebizweni lami, ngoba ibizo lami lizakuba likhulu phakathi kwezizwe,” kutsho uThixo uSomandla.
12 “Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
“Kodwa liyalingcolisa ngoba lithi, ‘Itafula kaThixo ingcolisiwe,’ lokudla okukulo, ‘Kuyadeleleka.’
13 Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
Njalo lichila amakhala ngokweyisa lithi, ‘Kuyasidina thina lokhu!’” Kutsho uThixo uSomandla. “Nxa liletha izifuyo ezilimeleyo kumbe ezigulayo lizozinikela zibe yimihlatshelo, lithi ngizemukele yini ezandleni zenu?” uyabuza uThixo.
14 “Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”
“Uqalekisiwe umkhohlisi olenqama enhle emhlambini wakhe, athembise ukunikela ngayo, kodwa abesenikela ngesifuyo esilesici kuThixo. Ngoba ngiyinkosi enkulu,” kutsho uThixo uSomandla, “njalo ibizo lami kufanele lesatshwe phakathi kwezizwe.”

< Malaki 1 >