< Nyimbo ya Solomoni 7 >

1 Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola mu nsapato wavalazo! Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali, ntchito ya manja ya mmisiri waluso.
Zinhle kangakanani izinyawo zakho emanyathelweni, ndodakazi yenkosana! Amalunga amathangazi akho anjengemiceciso, umsebenzi wezandla zengcitshi.
2 Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo. Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu utazunguliridwa ndi maluwa okongola.
Inkaba yakho injengomganu oyingubhe ongasweli iwayini elixutshanisiweyo. Isisu sakho sinjengenqumbi yengqoloyi ezingelezelwe yimiduze.
3 Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala, ngati mphoyo zamapasa.
Amabele akho womabili anjengabantwana ababili bomziki, abangamaphahla empala.
4 Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu. Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni, amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu. Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni, yoyangʼana ku Damasiko.
Intamo yakho injengomphotshongo wempondo zendlovu. Amehlo akho ayiziziba zeHeshiboni ngasesangweni leBeti-Rabimi. Impumulo yakho injengomphotshongo weLebhanoni okhangelene leDamaseko.
5 Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli. Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu; mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.
Ikhanda lakho phezu kwakho linjengeKharmeli, lenwele zekhanda lakho ezilengayo zinjengokuyibubende; inkosi ibotshwe emikhandlweni.
6 Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa, iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!
Umuhle kangakanani, njalo uthandeka kangakanani, thando, ezinjabulweni.
7 Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa, ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.
Lobu ubude bakho bunjengesihlahla selala, lamabele akho njengamaxha.
8 Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa; ndidzathyola zipatso zake.” Mawere ako ali ngati maphava a mphesa, fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,
Ngathi: Ngizakhwela esihlahleni selala ngibambe ingatsha zaso. Khathesi-ke amabele akho azakuba njengamahlukuzo evini, lephunga lamakhala akho linjengama-aphula,
9 ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri. Mkazi Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga, ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.
lolwanga lwakho lunjengewayini elihle eliya kusithandwa sami kakuhle, kusenza indebe zabaleleyo zikhulume.
10 Wokondedwayo ine ndine wake, ndipo chilakolako chake chili pa ine.
Ngingowesithandwa sami, lesifiso saso singakimi.
11 Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi, tikagone ku midzi.
Woza, sithandwa sami, kasiphumele egangeni, silale ebusuku emizaneni;
12 Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa, tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira, ngati maluwa ake ayamba kuoneka, komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa. Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.
kasivuke ngovivi siye ezivinini, sibone ukuthi amavini asehluma, ekhupha impoko, lokuthi amapomegranati akhahlele yini. Lapho ngizakunika uthando lwami.
13 Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino, ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma, zatsopano ndi zakale zomwe, zimene ndakusungira wokondedwa wanga.
Amamandrake akhupha iphunga elimnandi, langasemasangweni ethu kukhona zonke inhlobo zezithelo ezimnandi kakhulu, ezintsha lezindala, engizibekele wena, sithandwa sami.

< Nyimbo ya Solomoni 7 >