< Yesaya 1 >

1 Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
Umbono kaIsaya indodana kaAmozi, awubona ngoJuda leJerusalema, ensukwini zaboUziya, uJothamu, uAhazi, uHezekhiya, amakhosi akoJuda.
2 Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi! Pakuti Yehova wanena kuti, “Ndinabala ana ndi kuwalera, koma anawo andiwukira Ine.
Zwanini, mazulu, ubeke indlebe, mhlaba, ngoba iNkosi isikhulumile, yathi: Ngondlile ngakhulisa abantwana, kodwa bona bangivukele.
3 Ngʼombe imadziwa mwini wake, bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake, koma Israeli sadziwa, anthu anga samvetsa konse.”
Inkabi iyamazi umniniyo, lobabhemi umkolo womnikazi wakhe; kodwa uIsrayeli kazi, abantu bami kabaqedisisi.
4 Haa, mtundu wochimwa, anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoyipa, ana odzipereka ku zoyipa! Iwo asiya Yehova; anyoza Woyerayo wa Israeli ndipo afulatira Iyeyo.
Hawu, isizwe esonayo, abantu abasindwa yibubi, inzalo yabenzi bobubi, abantwana abonakalisayo! Bayitshiyile iNkosi, bamdelele oNgcwele kaIsrayeli, bahlehlele nyovane.
5 Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe? Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira? Mutu wanu wonse uli ndi mabala, mtima wanu wonse wafowokeratu.
Lizatshayelwani futhi? Belizaqhubeka livukela; ikhanda lonke liyagula, lenhliziyo yonke ibuthakathaka.
6 Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu palibe pabwino, paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu, mabala ake ngosatsuka, ngosamanga ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
Kusukela kungaphansi yonyawo kuze kufike ekhanda kakulandawo ephilileyo kukho, kodwa izilonda lemivimvinya lamanxeba ophayo; kakukhanywanga, kakubotshwanga, kakuthanjiswanga ngamafutha.
7 Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; minda yanu ikukololedwa ndi alendo inu muli pomwepo, dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
Ilizwe lakini liyincithakalo, imizi yenu itshiswe ngomlilo, umhlaba wenu abezizwe bawudla phambi kwenu, njalo kulencithakalo, njengokugenqulwa ngabemzini.
8 Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha ngati nsanja mʼmunda wampesa, ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka, ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
Indodakazi yeZiyoni isele-ke njengedumba esivinini, njengengalane ensimini yamakhomane, njengomuzi ovinjezelweyo.
9 Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira opulumuka, tikanawonongeka ngati Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
Uba iNkosi yamabandla ibingasitshiyelanga insali eyingcosana, besizakuba njengeSodoma, sifanane leGomora.
10 Imvani mawu a Yehova, inu olamulira Sodomu; mverani lamulo la Mulungu wathu, inu anthu a ku Gomora!
Zwanini ilizwi leNkosi, babusi beSodoma, libeke indlebe kumlayo kaNkulunkulu wethu, bantu beGomora.
11 Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka?” “Zandikola nsembe zanu zopsereza za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa; sindikusangalatsidwanso ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
Buyini kimi ubunengi bemihlatshelo yenu? itsho iNkosi. Ngenelisiwe yiminikelo yokutshiswa yezinqama langamahwahwa okunonisiweyo; legazi lamajongosi lelamawundlu lelezimpongo kangithokozi ngalo.
12 Ndani anakulamulirani kuti mubwere nazo pamaso panga? Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
Lapho lisizabonakala phambi kwami, ngubani obize lokhu esandleni senu, ukugxoba amaguma ami?
13 Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
Lingabe lisaletha umnikelo oyize; impepha iyisinengiso kimi; ukuthwasa kwenyanga, lesabatha, ukubizwa kwenhlangano, ngingekumele; kuyisiphambeko, ngitsho umhlangano onzulu.
14 Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera; ndatopa kuzinyamula.
Umphefumulo wami uyakuzonda ukuthwasa kwezinyanga zenu lemikhosi yenu emisiweyo; kungumthwalo kimi, sengikhathele yikukuthwala.
15 Mukamatambasula manja anu popemphera, Ine sindidzakuyangʼanani; ngakhale muchulukitse mapemphero anu, sindidzakumverani. Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
Lalapho liselula izandla zenu ngizalifihlela amehlo ami; njalo nxa lisandisa umkhuleko kangiyikuzwa; izandla zenu zigcwele igazi.
16 sambani, dziyeretseni. Chotsani pamaso panu ntchito zanu zoyipa! Lekani kuchita zoyipa,
Gezani, lizihlambulule; susani ububi bezenzo zenu phambi kwamehlo ami; yekelani ukwenza okubi;
17 phunzirani kuchita zabwino! Funafunani chilungamo, thandizani oponderezedwa. Tetezani ana amasiye, muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
fundani ukwenza okuhle; dingani isahlulelo; sizani ocindezelweyo; yehlulelani intandane; melani umfelokazi.
18 Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.
Wozani khathesi, siqondisane, itsho iNkosi; loba izono zenu zinjengokubomvu gebhu, zizakuba mhlophe njengeliqhwa elikhithikileyo; loba zibomvu njengokubomvu kakhulu, zizakuba njengoboya bezimvu.
19 Ngati muli okonzeka kundimvera mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
Uba livuma lilalela, lizakudla okuhle kwelizwe;
20 koma mukakana ndi kuwukira mudzaphedwa ndi lupanga.” Pakuti Yehova wayankhula.
kodwa uba lisala libe lenkani, lizadliwa yinkemba; ngoba umlomo weNkosi ukhulumile.
21 Taonani momwe mzinda wokhulupirika wasandukira wadama! Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama; mu mzindamo munali chilungamo, koma tsopano muli anthu opha anzawo!
Yeka, umuzi othembekileyo usube liwule! Wawugcwele isahlulelo, ukulunga kwakuhlezi kuwo, kodwa khathesi ababulali.
22 Siliva wako wasanduka wachabechabe, vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
Isiliva sakho sesibe ngamanyele; iwayini lakho laxubana lamanzi.
23 Atsogoleri ako ndi owukira, anthu ogwirizana ndi mbala; onse amakonda ziphuphu ndipo amathamangira mphatso. Iwo sateteza ana amasiye; ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
Iziphathamandla zakho zingabahlamuki labangane bamasela; ngulowo lalowo uthanda isipho, azingele izivalamlomo; kazehluleli izintandane, lendaba yomfelokazi kayifiki kuzo.
24 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu, Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti, “Haa, odana nane ndidzawatha, ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
Ngakho itsho iNkosi, iNkosi yamabandla, oLamandla wakoIsrayeli: E, ngizaziduduza ngezitha zami, ngiziphindisele kwabamelana lami.
25 Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe; ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa, monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
Ngizabuyisela isandla sami phezu kwakho, ngicwengisise amanyele akho, ngisuse yonke ingcekeza yokucwengwa kwakho.
26 Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana, aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja. Kenaka iweyo udzatchedwa mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.”
Ngizabuyisela abahluleli bakho njengekuqaleni, labeluleki bakho njengakuqala; emva kwalokho ubizwe ngokuthi ngumuzi wokulunga, umuzi othembekileyo.
27 Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama, anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
IZiyoni izahlengwa ngesahlulelo, labaphendukayo bayo ngokulunga.
28 Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi, ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
Lokwephulwa kwabaphambuki lokwezoni kuzakuba kanyekanye, labadela iNkosi baqedwe.
29 “Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani; mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene munayipatula.
Ngoba bazakuba lenhloni ngezihlahla zama-okhi elaliziloyisa, liyangeke ngezivande elizikhethileyo.
30 Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
Ngoba lizakuba njengesihlahla se-okhi omahlamvu aso ayabuna, lanjengesivande esingelamanzi.
31 Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma, ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali; motero zonse zidzayakira limodzi, popanda woti azimitse motowo.”
Njalo olamandla uzakuba lifilakisi eliyizibi, lomenzi walo abe yinhlansi; njalo kuzakutsha kokubili kanyekanye, kungabi khona ocitshayo.

< Yesaya 1 >